< Miyambo 11 >

1 Muyeso wachinyengo Yehova umamunyansa, koma amakondwera ndi muyeso woyenera.
Statera dolosa, abominatio est apud Deum: et pondus aequum, voluntas eius.
2 Kunyada kukalowa, pamafikanso manyazi, koma pamene pali kudzichepetsa pameneponso pali nzeru.
Ubi fuerit superbia, ibi erit et contumelia: ubi autem est humilitas, ibi et sapientia.
3 Ungwiro wa anthu olungama umawatsogolera, koma anthu osakhulupirika amawonongeka ndi chinyengo chawo.
Simplicitas iustorum diriget eos: et supplantatio perversorum vastabit illos.
4 Chuma sichithandiza pa tsiku lawukali wa Mulungu, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
Non proderunt divitiae in die ultionis: iustitia autem liberabit a morte.
5 Chilungamo cha anthu angwiro chimawongolera moyo wawo, koma ntchito zoyipa zimagwetsa mwini wake yemweyo.
Iustitia simplicis diriget viam eius: et in impietate sua corruet impius.
6 Chilungamo cha anthu oyera mtima chimawapulumutsa, koma anthu onyenga adzagwidwa ndi zilakolako zawo zomwe.
Iustitia rectorum liberabit eos: et in insidiis suis capientur iniqui.
7 Pamene munthu woyipa wafa, chiyembekezo chake chimathanso. Chiyembekezo cha munthu wosalungama chimawonongeka.
Mortuo homine impio, nulla erit ultra spes: et expectatio solicitorum peribit.
8 Munthu wolungama amapulumutsidwa ku mavuto, koma mʼmalo mwake amagwa mʼmavutomo ndi anthu oyipa.
Iustus de angustia liberatus est: et tradetur impius pro eo.
9 Munthu wosapembedza amawononga mnansi wake ndi pakamwa pake, koma munthu wolungama amapulumuka chifukwa cha kudziwa zinthu.
Simulator ore decipit amicum suum: iusti autem liberabuntur scientia.
10 Anthu olungama zinthu zikamawayendera bwino, mzinda wonse umakondwera, ndipo oyipa akamawonongeka anthu amafuwula mwachimwemwe.
In bonis iustorum exultabit civitas: et in perditione impiorum erit laudatio.
11 Mzinda umakwezeka chifukwa cha madalitso a anthu oyera mtima, koma umawonongedwa chifukwa cha pakamwa pa anthu oyipa.
Benedictione iustorum exaltabitur civitas: et ore impiorum subvertetur.
12 Munthu wonyoza mnzake ndi wopanda nzeru, koma munthu wanzeru zomvetsa zinthu amakhala chete.
Qui despicit amicum suum, indigens corde est: vir autem prudens tacebit.
13 Amene amanka nachita ukazitape amawulula zinsinsi; koma munthu wokhulupirika amasunga pakamwa pake.
Qui ambulat fraudulenter, revelat arcana: qui autem fidelis est, celat amici commissum.
14 Pakasoweka uphungu mtundu wa anthu umagwa; koma pakakhala aphungu ambiri pamakhalanso chipulumutso.
Ubi non est gubernator, populus corruet: salus autem, ubi multa consilia.
15 Woperekera mlendo chikole adzapeza mavuto, koma wodana ndi za chikole amakhala pa mtendere.
Affligetur malo, qui fidem facit pro extraneo: qui autem cavet laqueos, securus erit.
16 Mkazi wodekha amalandira ulemu, koma amuna ankhanza amangopata chuma.
Mulier gratiosa inveniet gloriam: et robusti habebunt divitias.
17 Munthu wachifundo amadzipindulira zabwino koma munthu wankhanza amadzibweretsera mavuto.
Benefacit animae suae vir misericors: qui autem crudelis est, etiam propinquos abiicit.
18 Munthu woyipa amalandira malipiro wopanda phindu, koma wochita chilungamo amakolola mphotho yeniyeni.
Impius facit opus instabile: seminanti autem iustitiam merces fidelis.
19 Munthu wochita za chilungamo amapeza moyo, koma wothamangira zoyipa adzafa.
Clementia praeparat vitam: et sectatio malorum mortem.
20 Yehova amanyansidwa ndi anthu a mtima wokhotakhota koma amakondwera ndi anthu a makhalidwe angwiro.
Abominabile Domino cor pravum: et voluntas eius in iis, qui simpliciter ambulant.
21 Zoonadi, anthu oyipa adzalangidwa, koma anthu olungama adzapulumuka.
Manus in manu non erit innocens malus: semen autem iustorum salvabitur.
22 Monga imaonekera mphete yagolide ikakhala pa mphuno ya nkhumba, ndi momwenso amaonekera mkazi wokongola wamʼkamwa.
Circulus aureus in naribus suis, mulier pulchra et fatua.
23 Zokhumba za anthu olungama zimathera pa zabwino zokhazokha, koma chiyembekezo cha anthu oyipa chimathera mu ukali wa Mulungu.
Desiderium iustorum omne bonum est: praestolatio impiorum furor.
24 Munthu wina amapatsako anzake zinthu mwaufulu nʼkumangolemererabe; wina amamana chomwe akanatha kupereka, koma kumanka nasawukabe.
Alii dividunt propria, et ditiores fiunt: alii rapiunt non sua, et semper in egestate sunt.
25 Munthu wopereka mowolowamanja adzalemera; iye amene amathandiza ena iyenso adzathandizidwa.
Anima, quae benedicit, impinguabitur: et qui inebriat, ipse quoque inebriabitur.
26 Anthu amatemberera womana anzake chakudya, koma madalitso amakhala pamutu pa munthu amene amagulitsa chakudyacho.
Qui abscondit frumenta, maledicetur in populis: benedictio autem super caput vendentium.
27 Iye amene amafunafuna zabwino mwakhama amapeza zabwinozo, koma wofunafuna zoyipa zidzamupeza.
Bene consurgit diluculo qui quaerit bona: qui autem investigator malorum est, opprimetur ab eis.
28 Aliyense amene amadalira chuma chake adzafota, koma wolungama adzaphukira ngati tsamba lobiriwira.
Qui confidit in divitiis suis, corruet: iusti autem quasi virens folium germinabunt.
29 Wovutitsa a mʼnyumba mwake adzalowa mʼmavuto, ndipo chitsiru chidzakhala kapolo wa munthu wa nzeru.
Qui conturbat domum suam, possidebit ventos: et qui stultus est, serviet sapienti.
30 Chipatso cha ntchito zabwino ndi moyo, ndipo kusatsata malamulo kumawonongetsa moyo.
Fructus iusti lignum vitae: et qui suscipit animas, sapiens est.
31 Ngati anthu olungama amalandira mphotho zawo pa dziko lapansi, kuli bwanji anthu osapembedza ndi ochimwa!
Si iustus in terra recipit, quanto magis impius et peccator?

< Miyambo 11 >