< Miyambo 11 >
1 Muyeso wachinyengo Yehova umamunyansa, koma amakondwera ndi muyeso woyenera.
O KE kaupaona hoopunipuni, he koopailua ia ia Iehova; O ke kaupaona kupono, oia kona makemake.
2 Kunyada kukalowa, pamafikanso manyazi, koma pamene pali kudzichepetsa pameneponso pali nzeru.
A hiki mai ka haaheo, alaila hiki mai ka hilahila; Me ka poe naau haahaa hoi ka naauao.
3 Ungwiro wa anthu olungama umawatsogolera, koma anthu osakhulupirika amawonongeka ndi chinyengo chawo.
O ka pono o ka mea pololei oia kona alakai; Ma ka wahahee hoi e make ai ka poe hoopunipuni.
4 Chuma sichithandiza pa tsiku lawukali wa Mulungu, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
O ka waiwai, aohe mea ia e pono ai i ka la e inaina mai ai; Aka, o ka pono oia ke hoopakele ae i ka make.
5 Chilungamo cha anthu angwiro chimawongolera moyo wawo, koma ntchito zoyipa zimagwetsa mwini wake yemweyo.
O ka pono o ka poe pololei, oia ke kuhikuhi o kona ala; E haule hoi ka mea hewa i kona hewa iho.
6 Chilungamo cha anthu oyera mtima chimawapulumutsa, koma anthu onyenga adzagwidwa ndi zilakolako zawo zomwe.
Ma ka pono e pakele ai ka poe pololei; Ma ke kolohe hoi e heiia'i ka poe aia.
7 Pamene munthu woyipa wafa, chiyembekezo chake chimathanso. Chiyembekezo cha munthu wosalungama chimawonongeka.
I ka make ana o ke kanaka hewa, pau kona manaolana; E poho no hoi ka manao o ka poe hewa.
8 Munthu wolungama amapulumutsidwa ku mavuto, koma mʼmalo mwake amagwa mʼmavutomo ndi anthu oyipa.
Laweia'ku ka mea pono mai ka popilikia aku, A hiki mai ka mea hewa ma kona hakahaka.
9 Munthu wosapembedza amawononga mnansi wake ndi pakamwa pake, koma munthu wolungama amapulumuka chifukwa cha kudziwa zinthu.
Ma ka waha o ka aia e make ai kona hoa; Ma ka ike oiaio hoi e pakele ai ka poe pono.
10 Anthu olungama zinthu zikamawayendera bwino, mzinda wonse umakondwera, ndipo oyipa akamawonongeka anthu amafuwula mwachimwemwe.
I ka lanakila ana o ka poe pono e hauoli ke kulanakauhale; I ke pio ana o ka poe hewa he olioli no.
11 Mzinda umakwezeka chifukwa cha madalitso a anthu oyera mtima, koma umawonongedwa chifukwa cha pakamwa pa anthu oyipa.
Ma ka hoomaikaiia mai o ka poe pololei, E hookiekieia ke kulanakauhale; Ma ka waha o ka poe hewa, ua hoohioloia.
12 Munthu wonyoza mnzake ndi wopanda nzeru, koma munthu wanzeru zomvetsa zinthu amakhala chete.
O ka mea hailiili aku i kona hoanoho, he naaupo ia; A o ke kanaka naauao, noho hamau oia;
13 Amene amanka nachita ukazitape amawulula zinsinsi; koma munthu wokhulupirika amasunga pakamwa pake.
O ka mea holoholo olelo, hai wale aku ia i na mea huna; O ka mea manao oiaio, e huna ana no oia.
14 Pakasoweka uphungu mtundu wa anthu umagwa; koma pakakhala aphungu ambiri pamakhalanso chipulumutso.
Ma kahi e ahaolelo ole ai, e haule na kanaka; Ma ka lehulehu o ka poe kukakuka he maluhia.
15 Woperekera mlendo chikole adzapeza mavuto, koma wodana ndi za chikole amakhala pa mtendere.
E hihia no ka mea pai lima me ka malihini; A o ka mea hoole i ke pai lima ana, ua pakele ia.
16 Mkazi wodekha amalandira ulemu, koma amuna ankhanza amangopata chuma.
O ka wahine lokomaikai, e loaa io no ka mahaloia mai; E loaa no hoi ka waiwai i ka poe hana ikaika.
17 Munthu wachifundo amadzipindulira zabwino koma munthu wankhanza amadzibweretsera mavuto.
O ka mea minamina i kona uhane iho, he kanaka lokomaikai oia; O ka mea hoino i kona kino, he aloha ole kona.
18 Munthu woyipa amalandira malipiro wopanda phindu, koma wochita chilungamo amakolola mphotho yeniyeni.
O ka mea hewa, he hana inea kana; O ka mea lulu i ka pono, he uku oiaio kona.
19 Munthu wochita za chilungamo amapeza moyo, koma wothamangira zoyipa adzafa.
E like me ka pili ana o ka pono i ke ola, Pela e pili ai ka make i ka mea hana hewa.
20 Yehova amanyansidwa ndi anthu a mtima wokhotakhota koma amakondwera ndi anthu a makhalidwe angwiro.
He mea hoopailua ia Iehova ka poe naau hoopunipuni; Aka, o ka poe i pololei ka aoao, oia kona makemake.
21 Zoonadi, anthu oyipa adzalangidwa, koma anthu olungama adzapulumuka.
Ina e kui kahi lima i kekahi lima, aole nae e hoopakeleia ka mea hewa; O ka mamo hoi o ka poe pono, e hoopakeleia oia.
22 Monga imaonekera mphete yagolide ikakhala pa mphuno ya nkhumba, ndi momwenso amaonekera mkazi wokongola wamʼkamwa.
Me he apo gula la ma ka ihu o ka puaa, Pela ka wahine i maikai ka maka a nele i ka noonoo ole.
23 Zokhumba za anthu olungama zimathera pa zabwino zokhazokha, koma chiyembekezo cha anthu oyipa chimathera mu ukali wa Mulungu.
O ka makemake o ka mea pono, he hope maikai kona; O ka manaolana hoi o ka poe hewa, he inainaia mai ka hope.
24 Munthu wina amapatsako anzake zinthu mwaufulu nʼkumangolemererabe; wina amamana chomwe akanatha kupereka, koma kumanka nasawukabe.
Hoohelelei kekahi, a nui hou ae no nae; Aua hoi kekahi i ka mea ku ole i ka pono, a o ka nele ka hope.
25 Munthu wopereka mowolowamanja adzalemera; iye amene amathandiza ena iyenso adzathandizidwa.
O ka mea e hoomanawalea aku, e momona ia; A o ka mea e hoomauu aku, e hoomauuia mai oia.
26 Anthu amatemberera womana anzake chakudya, koma madalitso amakhala pamutu pa munthu amene amagulitsa chakudyacho.
O ka mea aua i ka ai, e hoino na kanaka ia ia; E kau ana hoi ka hoomaikaiia mai ma ke poo o ka mea kuai aku.
27 Iye amene amafunafuna zabwino mwakhama amapeza zabwinozo, koma wofunafuna zoyipa zidzamupeza.
O ka mea imi i ka maikai, imi no ia i ke alohaia mai; O ka mea imi i ka hewa, e hiki mai no ia io na la.
28 Aliyense amene amadalira chuma chake adzafota, koma wolungama adzaphukira ngati tsamba lobiriwira.
O ka mea paulele i kona waiwai, e haule oia; Aka, me he lala laau la e ulu ai ka poe pono.
29 Wovutitsa a mʼnyumba mwake adzalowa mʼmavuto, ndipo chitsiru chidzakhala kapolo wa munthu wa nzeru.
O ka mea hoonaukiuki i ko kona hale, e ili mai nona ka makani; E hookauwa aku auanei ka naaupo na ka mea naauao.
30 Chipatso cha ntchito zabwino ndi moyo, ndipo kusatsata malamulo kumawonongetsa moyo.
O ka hua no ka pono, oia ka laau o ke ola; O ka mea hoohuli i na uhane, oia ke akamai.
31 Ngati anthu olungama amalandira mphotho zawo pa dziko lapansi, kuli bwanji anthu osapembedza ndi ochimwa!
Aia hoi, e hooukuia ka mea pono ma ka honua; Pela no a oi aku ka mea hewa a me ka ino.