< Miyambo 11 >
1 Muyeso wachinyengo Yehova umamunyansa, koma amakondwera ndi muyeso woyenera.
La balance trompeuse est une abomination auprès du Seigneur; le poids juste est selon sa volonté.
2 Kunyada kukalowa, pamafikanso manyazi, koma pamene pali kudzichepetsa pameneponso pali nzeru.
Où sera l’orgueil, là aussi sera l’outrage; mais où est l’humilité, là aussi est la sagesse.
3 Ungwiro wa anthu olungama umawatsogolera, koma anthu osakhulupirika amawonongeka ndi chinyengo chawo.
La simplicité des justes les dirigera; et la trahison des pervers les ruinera.
4 Chuma sichithandiza pa tsiku lawukali wa Mulungu, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
Les richesses ne serviront pas, au jour de la vengeance; mais la justice délivrera de la mort.
5 Chilungamo cha anthu angwiro chimawongolera moyo wawo, koma ntchito zoyipa zimagwetsa mwini wake yemweyo.
La justice du simple dirigera sa voie; et dans son impiété succombera l’impie.
6 Chilungamo cha anthu oyera mtima chimawapulumutsa, koma anthu onyenga adzagwidwa ndi zilakolako zawo zomwe.
La justice des hommes droits les délivrera; et dans leurs propres embûches seront pris les iniques.
7 Pamene munthu woyipa wafa, chiyembekezo chake chimathanso. Chiyembekezo cha munthu wosalungama chimawonongeka.
Un homme impie mort, il n’y aura plus aucune espérance; et l’attente des ambitieux périra.
8 Munthu wolungama amapulumutsidwa ku mavuto, koma mʼmalo mwake amagwa mʼmavutomo ndi anthu oyipa.
Le juste a été délivré de l’angoisse, et l’impie sera livré pour lui.
9 Munthu wosapembedza amawononga mnansi wake ndi pakamwa pake, koma munthu wolungama amapulumuka chifukwa cha kudziwa zinthu.
Un dissimulé trompe par sa bouche son ami; mais les justes seront délivrés par la science.
10 Anthu olungama zinthu zikamawayendera bwino, mzinda wonse umakondwera, ndipo oyipa akamawonongeka anthu amafuwula mwachimwemwe.
Au bonheur des justes exultera une cité, et à la ruine des impies il y aura louange.
11 Mzinda umakwezeka chifukwa cha madalitso a anthu oyera mtima, koma umawonongedwa chifukwa cha pakamwa pa anthu oyipa.
Par la bénédiction des justes, sera exaltée une cité; et par la bouche des impies elle sera renversée.
12 Munthu wonyoza mnzake ndi wopanda nzeru, koma munthu wanzeru zomvetsa zinthu amakhala chete.
Celui qui méprise son ami manque de cœur; mais un homme prudent se taira.
13 Amene amanka nachita ukazitape amawulula zinsinsi; koma munthu wokhulupirika amasunga pakamwa pake.
Celui qui marche frauduleusement révèle les secrets; mais celui qui est fidèle d’esprit tient cachée la confidence de son ami.
14 Pakasoweka uphungu mtundu wa anthu umagwa; koma pakakhala aphungu ambiri pamakhalanso chipulumutso.
Où il n’y a point de gouvernement, le peuple croulera; mais le salut est là où il y a beaucoup de conseils.
15 Woperekera mlendo chikole adzapeza mavuto, koma wodana ndi za chikole amakhala pa mtendere.
Il sera affligé par le malheur, celui qui répond pour un étranger; mais celui qui se garde du lacs sera en sûreté.
16 Mkazi wodekha amalandira ulemu, koma amuna ankhanza amangopata chuma.
La femme gracieuse trouvera la gloire; et les forts auront des richesses.
17 Munthu wachifundo amadzipindulira zabwino koma munthu wankhanza amadzibweretsera mavuto.
Il fait du bien à son âme, l’homme miséricordieux; mais celui qui est cruel rejette même ses proches.
18 Munthu woyipa amalandira malipiro wopanda phindu, koma wochita chilungamo amakolola mphotho yeniyeni.
L’impie fait une œuvre qui n’est pas stable; mais pour celui qui sème la justice, il y a une récompense assurée.
19 Munthu wochita za chilungamo amapeza moyo, koma wothamangira zoyipa adzafa.
La clémence prépare la vie, et la recherche du mal, la mort.
20 Yehova amanyansidwa ndi anthu a mtima wokhotakhota koma amakondwera ndi anthu a makhalidwe angwiro.
Abominable est au Seigneur un cœur dépravé, et sa bienveillance est pour ceux qui marchent avec simplicité.
21 Zoonadi, anthu oyipa adzalangidwa, koma anthu olungama adzapulumuka.
Lors même qu’une main serait dans une main, le méchant ne sera pas innocent; mais la race des justes sera sauvée.
22 Monga imaonekera mphete yagolide ikakhala pa mphuno ya nkhumba, ndi momwenso amaonekera mkazi wokongola wamʼkamwa.
C’est un anneau d’or aux naseaux d’une truie, qu’une femme belle et insensée.
23 Zokhumba za anthu olungama zimathera pa zabwino zokhazokha, koma chiyembekezo cha anthu oyipa chimathera mu ukali wa Mulungu.
Le désir des justes est toute espèce de bien; l’attente des impies est la fureur.
24 Munthu wina amapatsako anzake zinthu mwaufulu nʼkumangolemererabe; wina amamana chomwe akanatha kupereka, koma kumanka nasawukabe.
Les uns partagent leurs propres biens et deviennent plus riches; les autres ravissent ce qui n’est pas à eux, et toujours ils sont dans la détresse.
25 Munthu wopereka mowolowamanja adzalemera; iye amene amathandiza ena iyenso adzathandizidwa.
L’âme qui bénit sera engraissée; et celui qui enivre, lui-même aussi sera enivré.
26 Anthu amatemberera womana anzake chakudya, koma madalitso amakhala pamutu pa munthu amene amagulitsa chakudyacho.
Celui qui cache le blé sera maudit des peuples; mais la bénédiction viendra sur la tête de ceux qui le vendent.
27 Iye amene amafunafuna zabwino mwakhama amapeza zabwinozo, koma wofunafuna zoyipa zidzamupeza.
C’est avec raison que se lève au point du jour celui qui cherche les biens; mais celui qui recherche les maux en sera accablé.
28 Aliyense amene amadalira chuma chake adzafota, koma wolungama adzaphukira ngati tsamba lobiriwira.
Celui qui se confie dans ses richesses tombera précipitamment; mais les justes comme la feuille verdoyante germeront.
29 Wovutitsa a mʼnyumba mwake adzalowa mʼmavuto, ndipo chitsiru chidzakhala kapolo wa munthu wa nzeru.
Celui qui trouble sa maison possédera les vents, et celui qui est insensé servira le sage.
30 Chipatso cha ntchito zabwino ndi moyo, ndipo kusatsata malamulo kumawonongetsa moyo.
Le fruit du juste est un arbre de vie; et celui qui prend soin des âmes est sage.
31 Ngati anthu olungama amalandira mphotho zawo pa dziko lapansi, kuli bwanji anthu osapembedza ndi ochimwa!
Si le juste sur la terre reçoit sa punition, combien plus l’impie et le pécheur?