< Miyambo 11 >

1 Muyeso wachinyengo Yehova umamunyansa, koma amakondwera ndi muyeso woyenera.
La balance fausse est en abomination à l'Éternel; mais le poids juste lui est agréable.
2 Kunyada kukalowa, pamafikanso manyazi, koma pamene pali kudzichepetsa pameneponso pali nzeru.
L'orgueil est-il venu, aussitôt vient l'ignominie; mais la sagesse est avec les humbles.
3 Ungwiro wa anthu olungama umawatsogolera, koma anthu osakhulupirika amawonongeka ndi chinyengo chawo.
L'intégrité des hommes droits les conduit; mais la perversité des perfides les détruit.
4 Chuma sichithandiza pa tsiku lawukali wa Mulungu, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
Les biens ne serviront de rien au jour de l'indignation; mais la justice délivrera de la mort.
5 Chilungamo cha anthu angwiro chimawongolera moyo wawo, koma ntchito zoyipa zimagwetsa mwini wake yemweyo.
La justice de l'homme intègre aplanit son chemin; mais le méchant tombera par sa méchanceté.
6 Chilungamo cha anthu oyera mtima chimawapulumutsa, koma anthu onyenga adzagwidwa ndi zilakolako zawo zomwe.
La justice des hommes droits les délivre; mais les perfides sont pris par leur malice.
7 Pamene munthu woyipa wafa, chiyembekezo chake chimathanso. Chiyembekezo cha munthu wosalungama chimawonongeka.
Quand l'homme méchant meurt, son attente périt, et l'espérance des violents est anéantie.
8 Munthu wolungama amapulumutsidwa ku mavuto, koma mʼmalo mwake amagwa mʼmavutomo ndi anthu oyipa.
Le juste est délivré de la détresse; mais le méchant y tombe à sa place.
9 Munthu wosapembedza amawononga mnansi wake ndi pakamwa pake, koma munthu wolungama amapulumuka chifukwa cha kudziwa zinthu.
L'impie ruine son prochain par ses paroles; mais les justes sont délivrés par la science.
10 Anthu olungama zinthu zikamawayendera bwino, mzinda wonse umakondwera, ndipo oyipa akamawonongeka anthu amafuwula mwachimwemwe.
La ville se réjouit du bien des justes; mais il y a un chant de triomphe quand les méchants périssent.
11 Mzinda umakwezeka chifukwa cha madalitso a anthu oyera mtima, koma umawonongedwa chifukwa cha pakamwa pa anthu oyipa.
La ville est élevée par la bénédiction des hommes droits; mais elle est renversée par la bouche des méchants.
12 Munthu wonyoza mnzake ndi wopanda nzeru, koma munthu wanzeru zomvetsa zinthu amakhala chete.
Celui qui méprise son prochain, est dépourvu de sens; mais l'homme prudent se tait.
13 Amene amanka nachita ukazitape amawulula zinsinsi; koma munthu wokhulupirika amasunga pakamwa pake.
Celui qui va médisant, révèle le secret; mais celui qui a un cœur loyal, le cache.
14 Pakasoweka uphungu mtundu wa anthu umagwa; koma pakakhala aphungu ambiri pamakhalanso chipulumutso.
Le peuple tombe, faute de prudence; mais la délivrance est dans la multitude des gens de bon conseil.
15 Woperekera mlendo chikole adzapeza mavuto, koma wodana ndi za chikole amakhala pa mtendere.
Celui qui cautionne un étranger, ne peut manquer d'avoir du mal; mais celui qui hait ceux qui frappent dans la main, est en sécurité.
16 Mkazi wodekha amalandira ulemu, koma amuna ankhanza amangopata chuma.
La femme gracieuse obtient de l'honneur, et les hommes violents obtiennent des richesses.
17 Munthu wachifundo amadzipindulira zabwino koma munthu wankhanza amadzibweretsera mavuto.
L'homme bienfaisant se fait du bien à soi-même; mais celui qui est cruel trouble sa propre chair.
18 Munthu woyipa amalandira malipiro wopanda phindu, koma wochita chilungamo amakolola mphotho yeniyeni.
Le méchant fait une œuvre qui le trompe; mais la récompense est assurée à celui qui sème la justice.
19 Munthu wochita za chilungamo amapeza moyo, koma wothamangira zoyipa adzafa.
Ainsi la justice mène à la vie; mais celui qui poursuit le mal cherche la mort.
20 Yehova amanyansidwa ndi anthu a mtima wokhotakhota koma amakondwera ndi anthu a makhalidwe angwiro.
Ceux qui ont le cœur dépravé, sont en abomination à l'Éternel; mais ceux qui marchent en intégrité, lui sont agréables.
21 Zoonadi, anthu oyipa adzalangidwa, koma anthu olungama adzapulumuka.
Tôt ou tard, le méchant ne demeurera point impuni; mais la race des justes sera délivrée.
22 Monga imaonekera mphete yagolide ikakhala pa mphuno ya nkhumba, ndi momwenso amaonekera mkazi wokongola wamʼkamwa.
Une belle femme, qui se détourne de la raison, est comme une bague d'or au groin d'un pourceau.
23 Zokhumba za anthu olungama zimathera pa zabwino zokhazokha, koma chiyembekezo cha anthu oyipa chimathera mu ukali wa Mulungu.
Le souhait des justes n'est que le bien; mais l'attente des méchants c'est l'indignation.
24 Munthu wina amapatsako anzake zinthu mwaufulu nʼkumangolemererabe; wina amamana chomwe akanatha kupereka, koma kumanka nasawukabe.
Tel répand son bien, qui l'augmentera encore davantage; et tel le resserre plus qu'il ne faut, qui sera dans la disette.
25 Munthu wopereka mowolowamanja adzalemera; iye amene amathandiza ena iyenso adzathandizidwa.
Celui qui est bienfaisant sera rassasié, et celui qui arrose, sera aussi arrosé lui-même.
26 Anthu amatemberera womana anzake chakudya, koma madalitso amakhala pamutu pa munthu amene amagulitsa chakudyacho.
Celui qui retient le blé est maudit du peuple; mais la bénédiction est sur la tête de celui qui le vend.
27 Iye amene amafunafuna zabwino mwakhama amapeza zabwinozo, koma wofunafuna zoyipa zidzamupeza.
Celui qui recherche le bien, acquiert de la faveur; mais le mal arrivera à celui qui le poursuit.
28 Aliyense amene amadalira chuma chake adzafota, koma wolungama adzaphukira ngati tsamba lobiriwira.
Celui qui se fie en ses richesses, tombera; mais les justes reverdiront comme la feuille.
29 Wovutitsa a mʼnyumba mwake adzalowa mʼmavuto, ndipo chitsiru chidzakhala kapolo wa munthu wa nzeru.
Celui qui ne gouverne pas sa maison avec ordre, aura le vent pour héritage; et le fou sera le serviteur de celui qui a le cœur sage.
30 Chipatso cha ntchito zabwino ndi moyo, ndipo kusatsata malamulo kumawonongetsa moyo.
Le fruit du juste est un arbre de vie, et le sage gagne les cœurs.
31 Ngati anthu olungama amalandira mphotho zawo pa dziko lapansi, kuli bwanji anthu osapembedza ndi ochimwa!
Voici, le juste reçoit sur la terre sa rétribution; combien plus le méchant et le pécheur?

< Miyambo 11 >