< Miyambo 11 >
1 Muyeso wachinyengo Yehova umamunyansa, koma amakondwera ndi muyeso woyenera.
Les balances fausses sont en abomination au Seigneur; le poids juste Lui est agréable.
2 Kunyada kukalowa, pamafikanso manyazi, koma pamene pali kudzichepetsa pameneponso pali nzeru.
Où est l'orgueil, il y aura confusion; la bouche des humbles s'exercent à la sagesse.
3 Ungwiro wa anthu olungama umawatsogolera, koma anthu osakhulupirika amawonongeka ndi chinyengo chawo.
Le juste en mourant laisse des regrets; la mort des impies cause l'indifférence ou la joie.
4 Chuma sichithandiza pa tsiku lawukali wa Mulungu, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
5 Chilungamo cha anthu angwiro chimawongolera moyo wawo, koma ntchito zoyipa zimagwetsa mwini wake yemweyo.
L'équité trace des voies irréprochables; l'impiété trébuche contre l'injustice.
6 Chilungamo cha anthu oyera mtima chimawapulumutsa, koma anthu onyenga adzagwidwa ndi zilakolako zawo zomwe.
L'équité des hommes droits les sauve; les pervers sont pris dans leur propre perdition.
7 Pamene munthu woyipa wafa, chiyembekezo chake chimathanso. Chiyembekezo cha munthu wosalungama chimawonongeka.
L'espérance des justes ne meurt pas avec eux; l'orgueil des impies ne leur survit point.
8 Munthu wolungama amapulumutsidwa ku mavuto, koma mʼmalo mwake amagwa mʼmavutomo ndi anthu oyipa.
Le juste échappe aux chasseurs d'hommes; à sa place, l'impie leur est livré.
9 Munthu wosapembedza amawononga mnansi wake ndi pakamwa pake, koma munthu wolungama amapulumuka chifukwa cha kudziwa zinthu.
La bouche de l'impie tend un piège aux citoyens; l'intelligence du juste les guide dans la bonne voie.
10 Anthu olungama zinthu zikamawayendera bwino, mzinda wonse umakondwera, ndipo oyipa akamawonongeka anthu amafuwula mwachimwemwe.
Grâce aux justes, une cité prospère;
11 Mzinda umakwezeka chifukwa cha madalitso a anthu oyera mtima, koma umawonongedwa chifukwa cha pakamwa pa anthu oyipa.
au contraire, elle est renversée par la bouche des impies.
12 Munthu wonyoza mnzake ndi wopanda nzeru, koma munthu wanzeru zomvetsa zinthu amakhala chete.
L'insensé se joue des citoyens; un homme prudent ramène le calme.
13 Amene amanka nachita ukazitape amawulula zinsinsi; koma munthu wokhulupirika amasunga pakamwa pake.
L'homme à la langue double divulgue les conseils de l'assemblée; l'homme fidèle garde le secret sur les affaires.
14 Pakasoweka uphungu mtundu wa anthu umagwa; koma pakakhala aphungu ambiri pamakhalanso chipulumutso.
Ceux qui n'ont point de gouvernail tombent comme des feuilles. Le salut réside dans une grande puissance.
15 Woperekera mlendo chikole adzapeza mavuto, koma wodana ndi za chikole amakhala pa mtendere.
Le méchant fait le mal, même quand il se rapproche du juste; il n'aime pas son renom de fermeté.
16 Mkazi wodekha amalandira ulemu, koma amuna ankhanza amangopata chuma.
La femme gracieuse fait la gloire de son mari; la femme qui hait la justice est un trône de déshonneur. Les paresseux manquent de richesses; les forts travaillent à en amasser.
17 Munthu wachifundo amadzipindulira zabwino koma munthu wankhanza amadzibweretsera mavuto.
L'homme charitable fait du bien à son âme; l'homme sans pitié perd son corps.
18 Munthu woyipa amalandira malipiro wopanda phindu, koma wochita chilungamo amakolola mphotho yeniyeni.
L'impie fait des œuvres iniques; la race des justes recueille la récompense de la vérité.
19 Munthu wochita za chilungamo amapeza moyo, koma wothamangira zoyipa adzafa.
Un fils juste est né pour la vie; ce que poursuit l'impie mène à la mort.
20 Yehova amanyansidwa ndi anthu a mtima wokhotakhota koma amakondwera ndi anthu a makhalidwe angwiro.
Les voies tortueuses sont en abomination au Seigneur; mais Il agrée tous ceux qui sont irréprochables dans leurs voies.
21 Zoonadi, anthu oyipa adzalangidwa, koma anthu olungama adzapulumuka.
Celui qui, dans une pensée injuste, met sa main dans la main d'autrui ne sera point impuni; au contraire, qui sème la justice en récoltera le digne salaire.
22 Monga imaonekera mphete yagolide ikakhala pa mphuno ya nkhumba, ndi momwenso amaonekera mkazi wokongola wamʼkamwa.
Tel est un pendant d'oreille au museau d'une truie; telle est la beauté chez la femme sans sagesse.
23 Zokhumba za anthu olungama zimathera pa zabwino zokhazokha, koma chiyembekezo cha anthu oyipa chimathera mu ukali wa Mulungu.
Le désir du juste est bon sans réserve; l'espérance des impies périra.
24 Munthu wina amapatsako anzake zinthu mwaufulu nʼkumangolemererabe; wina amamana chomwe akanatha kupereka, koma kumanka nasawukabe.
Il en est qui, en distribuant leurs biens, les augmentent; il en est qui, même en s'amusant, s'appauvrissent.
25 Munthu wopereka mowolowamanja adzalemera; iye amene amathandiza ena iyenso adzathandizidwa.
Toute âme simple est bénie; l'homme irascible n'est pas honoré.
26 Anthu amatemberera womana anzake chakudya, koma madalitso amakhala pamutu pa munthu amene amagulitsa chakudyacho.
Que celui qui amasse du blé le tienne en réserve pour les peuples; la bénédiction est sur la tête de celui qui en fait part à autrui.
27 Iye amene amafunafuna zabwino mwakhama amapeza zabwinozo, koma wofunafuna zoyipa zidzamupeza.
Celui qui médite le bien cherche une grâce salutaire; celui qui songe au mal le recueillera pour lui-même.
28 Aliyense amene amadalira chuma chake adzafota, koma wolungama adzaphukira ngati tsamba lobiriwira.
Celui qui se fie en sa richesse tombera; celui qui s'attache aux choses justes fleurira.
29 Wovutitsa a mʼnyumba mwake adzalowa mʼmavuto, ndipo chitsiru chidzakhala kapolo wa munthu wa nzeru.
Celui qui ne s'occupe pas de sa propre maison n'aura que le vent pour héritage; l'insensé sera le serviteur du sage.
30 Chipatso cha ntchito zabwino ndi moyo, ndipo kusatsata malamulo kumawonongetsa moyo.
Du fruit de la justice naît l'arbre de vie; les âmes des pervers seront emportées avant le temps.
31 Ngati anthu olungama amalandira mphotho zawo pa dziko lapansi, kuli bwanji anthu osapembedza ndi ochimwa!
Si le juste est difficilement sauvé, que penser de l'impie et du pécheur?