< Miyambo 11 >

1 Muyeso wachinyengo Yehova umamunyansa, koma amakondwera ndi muyeso woyenera.
La fausse balance est en abomination à l’Éternel, mais le poids juste lui est agréable.
2 Kunyada kukalowa, pamafikanso manyazi, koma pamene pali kudzichepetsa pameneponso pali nzeru.
[Quand] vient l’orgueil, la honte vient aussi; mais la sagesse est avec les hommes modestes.
3 Ungwiro wa anthu olungama umawatsogolera, koma anthu osakhulupirika amawonongeka ndi chinyengo chawo.
L’intégrité des hommes droits les guide, mais la perversité des perfides les détruit.
4 Chuma sichithandiza pa tsiku lawukali wa Mulungu, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
Les richesses ne profitent de rien au jour de la colère, mais la justice délivre de la mort.
5 Chilungamo cha anthu angwiro chimawongolera moyo wawo, koma ntchito zoyipa zimagwetsa mwini wake yemweyo.
La justice de l’homme intègre rend droite sa voie, mais le méchant tombe par sa méchanceté.
6 Chilungamo cha anthu oyera mtima chimawapulumutsa, koma anthu onyenga adzagwidwa ndi zilakolako zawo zomwe.
La justice des hommes droits les délivre, mais les perfides sont pris dans leur avidité.
7 Pamene munthu woyipa wafa, chiyembekezo chake chimathanso. Chiyembekezo cha munthu wosalungama chimawonongeka.
Quand l’homme méchant meurt, son espérance périt, et l’attente des iniques périt.
8 Munthu wolungama amapulumutsidwa ku mavuto, koma mʼmalo mwake amagwa mʼmavutomo ndi anthu oyipa.
Le juste est délivré de la détresse, et le méchant [y] entre à sa place.
9 Munthu wosapembedza amawononga mnansi wake ndi pakamwa pake, koma munthu wolungama amapulumuka chifukwa cha kudziwa zinthu.
Par sa bouche l’impie perd son prochain; mais les justes sont délivrés par la connaissance.
10 Anthu olungama zinthu zikamawayendera bwino, mzinda wonse umakondwera, ndipo oyipa akamawonongeka anthu amafuwula mwachimwemwe.
La ville se réjouit du bien-être des justes; et quand les méchants périssent il y a des cris de joie.
11 Mzinda umakwezeka chifukwa cha madalitso a anthu oyera mtima, koma umawonongedwa chifukwa cha pakamwa pa anthu oyipa.
La ville s’élève par la bénédiction des hommes droits, mais elle est renversée par la bouche des méchants.
12 Munthu wonyoza mnzake ndi wopanda nzeru, koma munthu wanzeru zomvetsa zinthu amakhala chete.
Qui méprise son prochain est dépourvu de sens, mais l’homme intelligent se tait.
13 Amene amanka nachita ukazitape amawulula zinsinsi; koma munthu wokhulupirika amasunga pakamwa pake.
Celui qui va rapportant révèle le secret, mais celui qui est d’un esprit fidèle couvre la chose.
14 Pakasoweka uphungu mtundu wa anthu umagwa; koma pakakhala aphungu ambiri pamakhalanso chipulumutso.
Quand il n’y a pas de direction le peuple tombe, mais il y a salut dans le grand nombre des conseillers.
15 Woperekera mlendo chikole adzapeza mavuto, koma wodana ndi za chikole amakhala pa mtendere.
On se trouve mal de cautionner un étranger, mais celui qui hait ceux qui frappent [dans la main] est en sûreté.
16 Mkazi wodekha amalandira ulemu, koma amuna ankhanza amangopata chuma.
Une femme gracieuse obtient l’honneur, et les hommes forts obtiennent la richesse.
17 Munthu wachifundo amadzipindulira zabwino koma munthu wankhanza amadzibweretsera mavuto.
L’homme bon fait du bien à son âme, mais le cruel trouble sa chair.
18 Munthu woyipa amalandira malipiro wopanda phindu, koma wochita chilungamo amakolola mphotho yeniyeni.
Le méchant fait une œuvre trompeuse, mais celui qui sème la justice a un vrai salaire.
19 Munthu wochita za chilungamo amapeza moyo, koma wothamangira zoyipa adzafa.
Comme la justice [tend] à la vie, celui qui poursuit le mal [tend] à sa mort.
20 Yehova amanyansidwa ndi anthu a mtima wokhotakhota koma amakondwera ndi anthu a makhalidwe angwiro.
Ceux qui sont pervers de cœur sont en abomination à l’Éternel, mais ceux qui sont intègres dans leurs voies lui sont agréables.
21 Zoonadi, anthu oyipa adzalangidwa, koma anthu olungama adzapulumuka.
Certainement l’inique ne sera point tenu pour innocent; mais la semence des justes sera délivrée.
22 Monga imaonekera mphete yagolide ikakhala pa mphuno ya nkhumba, ndi momwenso amaonekera mkazi wokongola wamʼkamwa.
Une femme belle et dépourvue de sens, c’est un anneau d’or au nez d’un pourceau.
23 Zokhumba za anthu olungama zimathera pa zabwino zokhazokha, koma chiyembekezo cha anthu oyipa chimathera mu ukali wa Mulungu.
Le désir des justes n’est que le bien; l’attente des méchants, c’est la fureur.
24 Munthu wina amapatsako anzake zinthu mwaufulu nʼkumangolemererabe; wina amamana chomwe akanatha kupereka, koma kumanka nasawukabe.
Tel disperse, et augmente encore; et tel retient plus qu’il ne faut, mais n’en a que disette.
25 Munthu wopereka mowolowamanja adzalemera; iye amene amathandiza ena iyenso adzathandizidwa.
L’âme qui bénit sera engraissée, et celui qui arrose sera lui-même arrosé.
26 Anthu amatemberera womana anzake chakudya, koma madalitso amakhala pamutu pa munthu amene amagulitsa chakudyacho.
Celui qui retient le blé, le peuple le maudit; mais la bénédiction sera sur la tête de celui qui le vend.
27 Iye amene amafunafuna zabwino mwakhama amapeza zabwinozo, koma wofunafuna zoyipa zidzamupeza.
Qui recherche le bien cherche la faveur, mais le mal arrive à qui le recherche.
28 Aliyense amene amadalira chuma chake adzafota, koma wolungama adzaphukira ngati tsamba lobiriwira.
Celui-là tombe qui se confie en ses richesses; mais les justes verdissent comme la feuille.
29 Wovutitsa a mʼnyumba mwake adzalowa mʼmavuto, ndipo chitsiru chidzakhala kapolo wa munthu wa nzeru.
Celui qui trouble sa maison héritera le vent, et le fou deviendra serviteur de celui qui est sage de cœur.
30 Chipatso cha ntchito zabwino ndi moyo, ndipo kusatsata malamulo kumawonongetsa moyo.
Le fruit du juste est un arbre de vie, et le sage gagne les âmes.
31 Ngati anthu olungama amalandira mphotho zawo pa dziko lapansi, kuli bwanji anthu osapembedza ndi ochimwa!
Voici, le juste est rétribué sur la terre, combien plus le méchant et le pécheur!

< Miyambo 11 >