< Miyambo 11 >

1 Muyeso wachinyengo Yehova umamunyansa, koma amakondwera ndi muyeso woyenera.
A false balance is an abomination to Adonai, but accurate weights are his delight.
2 Kunyada kukalowa, pamafikanso manyazi, koma pamene pali kudzichepetsa pameneponso pali nzeru.
When pride comes, then comes shame, but with humility comes wisdom.
3 Ungwiro wa anthu olungama umawatsogolera, koma anthu osakhulupirika amawonongeka ndi chinyengo chawo.
The integrity of the upright shall guide them, but the perverseness of the treacherous shall destroy them.
4 Chuma sichithandiza pa tsiku lawukali wa Mulungu, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
Riches don’t profit in the day of wrath, but righteousness delivers from death.
5 Chilungamo cha anthu angwiro chimawongolera moyo wawo, koma ntchito zoyipa zimagwetsa mwini wake yemweyo.
The righteousness of the blameless will direct his way, but the wicked shall fall by his own wickedness.
6 Chilungamo cha anthu oyera mtima chimawapulumutsa, koma anthu onyenga adzagwidwa ndi zilakolako zawo zomwe.
The righteousness of the upright shall deliver them, but the unfaithful will be trapped by evil desires.
7 Pamene munthu woyipa wafa, chiyembekezo chake chimathanso. Chiyembekezo cha munthu wosalungama chimawonongeka.
When a wicked man dies, hope perishes, and expectation of power comes to nothing.
8 Munthu wolungama amapulumutsidwa ku mavuto, koma mʼmalo mwake amagwa mʼmavutomo ndi anthu oyipa.
A upright person is delivered out of trouble, and the wicked takes his place.
9 Munthu wosapembedza amawononga mnansi wake ndi pakamwa pake, koma munthu wolungama amapulumuka chifukwa cha kudziwa zinthu.
With his mouth the godless man destroys his neighbor, but the upright will be delivered through knowledge.
10 Anthu olungama zinthu zikamawayendera bwino, mzinda wonse umakondwera, ndipo oyipa akamawonongeka anthu amafuwula mwachimwemwe.
When it goes well with the upright, the city rejoices. When the wicked perish, there is shouting.
11 Mzinda umakwezeka chifukwa cha madalitso a anthu oyera mtima, koma umawonongedwa chifukwa cha pakamwa pa anthu oyipa.
By the blessing of the upright, the city is exalted, but it is overthrown by the mouth of the wicked.
12 Munthu wonyoza mnzake ndi wopanda nzeru, koma munthu wanzeru zomvetsa zinthu amakhala chete.
One who despises his neighbor is void of wisdom, but a man of understanding holds his peace.
13 Amene amanka nachita ukazitape amawulula zinsinsi; koma munthu wokhulupirika amasunga pakamwa pake.
One who brings gossip betrays a confidence, but one who is of a trustworthy spirit is one who keeps a secret.
14 Pakasoweka uphungu mtundu wa anthu umagwa; koma pakakhala aphungu ambiri pamakhalanso chipulumutso.
Where there is no wise guidance, the nation falls, but in the multitude of counselors there is victory.
15 Woperekera mlendo chikole adzapeza mavuto, koma wodana ndi za chikole amakhala pa mtendere.
He who is collateral for a stranger will suffer for it, but he who refuses pledges of collateral is secure.
16 Mkazi wodekha amalandira ulemu, koma amuna ankhanza amangopata chuma.
A chen ·gracious· woman obtains kavod ·weighty glory·, but violent men obtain riches.
17 Munthu wachifundo amadzipindulira zabwino koma munthu wankhanza amadzibweretsera mavuto.
The man of cheshed ·loving-kindness· does good to his own soul, but he who is cruel troubles his own flesh.
18 Munthu woyipa amalandira malipiro wopanda phindu, koma wochita chilungamo amakolola mphotho yeniyeni.
Wicked people earn deceitful wages, but one who sows righteousness reaps a sure reward.
19 Munthu wochita za chilungamo amapeza moyo, koma wothamangira zoyipa adzafa.
He who is truly upright gets life. He who pursues evil gets death.
20 Yehova amanyansidwa ndi anthu a mtima wokhotakhota koma amakondwera ndi anthu a makhalidwe angwiro.
Those who are perverse in heart are an abomination to Adonai, but those whose ways are blameless are his delight.
21 Zoonadi, anthu oyipa adzalangidwa, koma anthu olungama adzapulumuka.
Most certainly, the evil man will not be unpunished, but the offspring of the upright will be delivered.
22 Monga imaonekera mphete yagolide ikakhala pa mphuno ya nkhumba, ndi momwenso amaonekera mkazi wokongola wamʼkamwa.
Like a gold ring in a pig’s snout, is a beautiful woman who lacks discretion.
23 Zokhumba za anthu olungama zimathera pa zabwino zokhazokha, koma chiyembekezo cha anthu oyipa chimathera mu ukali wa Mulungu.
The desire of the upright is only good. The expectation of the wicked is wrath.
24 Munthu wina amapatsako anzake zinthu mwaufulu nʼkumangolemererabe; wina amamana chomwe akanatha kupereka, koma kumanka nasawukabe.
There is one who scatters, and increases yet more. There is one who withholds more than is appropriate, but gains poverty.
25 Munthu wopereka mowolowamanja adzalemera; iye amene amathandiza ena iyenso adzathandizidwa.
The liberal soul shall be made fat. He who waters shall be watered also himself.
26 Anthu amatemberera womana anzake chakudya, koma madalitso amakhala pamutu pa munthu amene amagulitsa chakudyacho.
People curse someone who withholds grain, but blessing will be on the head of him who sells it.
27 Iye amene amafunafuna zabwino mwakhama amapeza zabwinozo, koma wofunafuna zoyipa zidzamupeza.
He who diligently seeks good seeks favor, but he who searches after evil, it shall come to him.
28 Aliyense amene amadalira chuma chake adzafota, koma wolungama adzaphukira ngati tsamba lobiriwira.
He who trusts in his riches will fall, but the upright shall flourish as the green leaf.
29 Wovutitsa a mʼnyumba mwake adzalowa mʼmavuto, ndipo chitsiru chidzakhala kapolo wa munthu wa nzeru.
He who troubles his own house shall inherit the wind. The foolish shall be servant to the wise of heart.
30 Chipatso cha ntchito zabwino ndi moyo, ndipo kusatsata malamulo kumawonongetsa moyo.
The fruit of the upright is a tree of life. He who is wise wins souls.
31 Ngati anthu olungama amalandira mphotho zawo pa dziko lapansi, kuli bwanji anthu osapembedza ndi ochimwa!
Behold, the upright are paid what they deserve here on earth; how much more the wicked and the sinner!

< Miyambo 11 >