< Miyambo 11 >

1 Muyeso wachinyengo Yehova umamunyansa, koma amakondwera ndi muyeso woyenera.
False scales are an abomination to the LORD; But a perfect weight is his delight.
2 Kunyada kukalowa, pamafikanso manyazi, koma pamene pali kudzichepetsa pameneponso pali nzeru.
When pride cometh, then cometh disgrace; But with the humble is wisdom.
3 Ungwiro wa anthu olungama umawatsogolera, koma anthu osakhulupirika amawonongeka ndi chinyengo chawo.
The integrity of the upright shall guide them; But the perverseness of transgressors shall destroy them.
4 Chuma sichithandiza pa tsiku lawukali wa Mulungu, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
Riches do not profit in the day of wrath; But righteousness delivereth from death.
5 Chilungamo cha anthu angwiro chimawongolera moyo wawo, koma ntchito zoyipa zimagwetsa mwini wake yemweyo.
The righteousness of the good man maketh his way plain; But the wicked falleth through his wickedness.
6 Chilungamo cha anthu oyera mtima chimawapulumutsa, koma anthu onyenga adzagwidwa ndi zilakolako zawo zomwe.
The righteousness of the upright delivereth them; But transgressors are ensnared in their own mischief.
7 Pamene munthu woyipa wafa, chiyembekezo chake chimathanso. Chiyembekezo cha munthu wosalungama chimawonongeka.
When the wicked man dieth, his hope cometh to an end; Yea, the expectation of the unjust cometh to an end.
8 Munthu wolungama amapulumutsidwa ku mavuto, koma mʼmalo mwake amagwa mʼmavutomo ndi anthu oyipa.
The righteous man is delivered from trouble, And the wicked cometh into it in his stead.
9 Munthu wosapembedza amawononga mnansi wake ndi pakamwa pake, koma munthu wolungama amapulumuka chifukwa cha kudziwa zinthu.
By his mouth the vile man destroyeth his neighbor; But by the knowledge of the righteous are men delivered.
10 Anthu olungama zinthu zikamawayendera bwino, mzinda wonse umakondwera, ndipo oyipa akamawonongeka anthu amafuwula mwachimwemwe.
When it goeth well with the righteous, the city rejoiceth; And when the wicked perish, there is shouting.
11 Mzinda umakwezeka chifukwa cha madalitso a anthu oyera mtima, koma umawonongedwa chifukwa cha pakamwa pa anthu oyipa.
By the blessing of the upright the city is exalted; But it is overthrown by the mouth of the wicked.
12 Munthu wonyoza mnzake ndi wopanda nzeru, koma munthu wanzeru zomvetsa zinthu amakhala chete.
He who despiseth his neighbor is void of understanding; A man of discernment holdeth his peace.
13 Amene amanka nachita ukazitape amawulula zinsinsi; koma munthu wokhulupirika amasunga pakamwa pake.
He who goeth about as a tale-bearer revealeth secrets; But he who is of a faithful spirit concealeth a matter.
14 Pakasoweka uphungu mtundu wa anthu umagwa; koma pakakhala aphungu ambiri pamakhalanso chipulumutso.
Where there is no counsel, the people fall; But in a multitude of counsellors there is safety.
15 Woperekera mlendo chikole adzapeza mavuto, koma wodana ndi za chikole amakhala pa mtendere.
He that is surety for another shall smart for it; But he that hateth suretyship is sure.
16 Mkazi wodekha amalandira ulemu, koma amuna ankhanza amangopata chuma.
A graceful woman obtaineth honor, Even as strong men obtain riches.
17 Munthu wachifundo amadzipindulira zabwino koma munthu wankhanza amadzibweretsera mavuto.
He that doeth good to himself is a man of kindness; But he that tormenteth his own flesh is cruel.
18 Munthu woyipa amalandira malipiro wopanda phindu, koma wochita chilungamo amakolola mphotho yeniyeni.
The wicked toileth for deceitful wages; But he who soweth righteousness shall have a sure reward.
19 Munthu wochita za chilungamo amapeza moyo, koma wothamangira zoyipa adzafa.
As righteousness tendeth to life, So he who pursueth evil pursueth it to his death.
20 Yehova amanyansidwa ndi anthu a mtima wokhotakhota koma amakondwera ndi anthu a makhalidwe angwiro.
The perverse in heart are the abomination of the LORD; But the upright in their way are his delight.
21 Zoonadi, anthu oyipa adzalangidwa, koma anthu olungama adzapulumuka.
From generation to generation the wicked shall not go unpunished; But the posterity of the righteous shall be delivered.
22 Monga imaonekera mphete yagolide ikakhala pa mphuno ya nkhumba, ndi momwenso amaonekera mkazi wokongola wamʼkamwa.
As a jewel of gold in a swine's snout, So is a beautiful woman who is without discretion.
23 Zokhumba za anthu olungama zimathera pa zabwino zokhazokha, koma chiyembekezo cha anthu oyipa chimathera mu ukali wa Mulungu.
The desire of the righteous is only good; But the expectation of the wicked is wrath.
24 Munthu wina amapatsako anzake zinthu mwaufulu nʼkumangolemererabe; wina amamana chomwe akanatha kupereka, koma kumanka nasawukabe.
There is that scattereth, and yet increaseth; And there is that withholdeth more than is right, yet he cometh to want.
25 Munthu wopereka mowolowamanja adzalemera; iye amene amathandiza ena iyenso adzathandizidwa.
The bountiful man shall be enriched, And he that watereth shall himself be watered.
26 Anthu amatemberera womana anzake chakudya, koma madalitso amakhala pamutu pa munthu amene amagulitsa chakudyacho.
Him that keepeth back corn the people curse; But blessing shall be upon the head of him that selleth it.
27 Iye amene amafunafuna zabwino mwakhama amapeza zabwinozo, koma wofunafuna zoyipa zidzamupeza.
He, who earnestly seeketh good, seeketh favor; But he that seeketh mischief, it shall come upon him.
28 Aliyense amene amadalira chuma chake adzafota, koma wolungama adzaphukira ngati tsamba lobiriwira.
He who trusteth in his riches shall fall; But the righteous shall flourish as a leaf.
29 Wovutitsa a mʼnyumba mwake adzalowa mʼmavuto, ndipo chitsiru chidzakhala kapolo wa munthu wa nzeru.
He that harasseth his household shall inherit wind; And the fool shall be the servant of the wise.
30 Chipatso cha ntchito zabwino ndi moyo, ndipo kusatsata malamulo kumawonongetsa moyo.
The fruit of a righteous man is a tree of life; And the wise man winneth souls.
31 Ngati anthu olungama amalandira mphotho zawo pa dziko lapansi, kuli bwanji anthu osapembedza ndi ochimwa!
Behold, the righteous man is requited on the earth; Much more the wicked man and the sinner!

< Miyambo 11 >