< Miyambo 11 >

1 Muyeso wachinyengo Yehova umamunyansa, koma amakondwera ndi muyeso woyenera.
False balances are an abomination vnto the Lord: but a perfite weight pleaseth him.
2 Kunyada kukalowa, pamafikanso manyazi, koma pamene pali kudzichepetsa pameneponso pali nzeru.
When pride commeth, then commeth shame: but with the lowly is wisdome.
3 Ungwiro wa anthu olungama umawatsogolera, koma anthu osakhulupirika amawonongeka ndi chinyengo chawo.
The vprightnes of the iust shall guide them: but the frowardnes of the transgressers shall destroy them.
4 Chuma sichithandiza pa tsiku lawukali wa Mulungu, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
Riches auaile not in the day of wrath: but righteousnes deliuereth from death.
5 Chilungamo cha anthu angwiro chimawongolera moyo wawo, koma ntchito zoyipa zimagwetsa mwini wake yemweyo.
The righteousnes of the vpright shall direct his way: but the wicked shall fall in his owne wickednes.
6 Chilungamo cha anthu oyera mtima chimawapulumutsa, koma anthu onyenga adzagwidwa ndi zilakolako zawo zomwe.
The righteousnesse of the iust shall deliuer them: but the transgressers shall be taken in their owne wickednes.
7 Pamene munthu woyipa wafa, chiyembekezo chake chimathanso. Chiyembekezo cha munthu wosalungama chimawonongeka.
When a wicked man dieth, his hope perisheth, and the hope of the vniust shall perish.
8 Munthu wolungama amapulumutsidwa ku mavuto, koma mʼmalo mwake amagwa mʼmavutomo ndi anthu oyipa.
The righteous escapeth out of trouble, and the wicked shall come in his steade.
9 Munthu wosapembedza amawononga mnansi wake ndi pakamwa pake, koma munthu wolungama amapulumuka chifukwa cha kudziwa zinthu.
An hypocrite with his mouth hurteth his neighbour: but the righteous shall be deliuered by knowledge.
10 Anthu olungama zinthu zikamawayendera bwino, mzinda wonse umakondwera, ndipo oyipa akamawonongeka anthu amafuwula mwachimwemwe.
In the prosperitie of the righteous the citie reioyceth, and when the wicked perish, there is ioye.
11 Mzinda umakwezeka chifukwa cha madalitso a anthu oyera mtima, koma umawonongedwa chifukwa cha pakamwa pa anthu oyipa.
By the blessing of the righteous, the citie is exalted: but it is subuerted by the mouth of the wicked.
12 Munthu wonyoza mnzake ndi wopanda nzeru, koma munthu wanzeru zomvetsa zinthu amakhala chete.
He that despiseth his neighbour, is destitute of wisedome: but a man of vnderstanding will keepe silence.
13 Amene amanka nachita ukazitape amawulula zinsinsi; koma munthu wokhulupirika amasunga pakamwa pake.
Hee that goeth about as a slanderer, discouereth a secret: but hee that is of a faithfull heart concealeth a matter.
14 Pakasoweka uphungu mtundu wa anthu umagwa; koma pakakhala aphungu ambiri pamakhalanso chipulumutso.
Where no counsell is, the people fall: but where many counsellers are, there is health.
15 Woperekera mlendo chikole adzapeza mavuto, koma wodana ndi za chikole amakhala pa mtendere.
Hee shall be sore vexed, that is suretie for a stranger, and he that hateth suretiship, is sure.
16 Mkazi wodekha amalandira ulemu, koma amuna ankhanza amangopata chuma.
A gracious woman atteineth honour, and the strong men atteine riches.
17 Munthu wachifundo amadzipindulira zabwino koma munthu wankhanza amadzibweretsera mavuto.
Hee that is mercifull, rewardeth his owne soule: but he that troubleth his own flesh, is cruel.
18 Munthu woyipa amalandira malipiro wopanda phindu, koma wochita chilungamo amakolola mphotho yeniyeni.
The wicked worketh a deceitful worke: but hee that soweth righteousnes, shall receiue a sure rewarde.
19 Munthu wochita za chilungamo amapeza moyo, koma wothamangira zoyipa adzafa.
As righteousnes leadeth to life: so hee that followeth euill, seeketh his owne death.
20 Yehova amanyansidwa ndi anthu a mtima wokhotakhota koma amakondwera ndi anthu a makhalidwe angwiro.
They that are of a froward heart, are abomination to the Lord: but they that are vpright in their way, are his delite.
21 Zoonadi, anthu oyipa adzalangidwa, koma anthu olungama adzapulumuka.
Though hande ioyne in hande, the wicked shall not be vnpunished: but the seede of the righteous shall escape.
22 Monga imaonekera mphete yagolide ikakhala pa mphuno ya nkhumba, ndi momwenso amaonekera mkazi wokongola wamʼkamwa.
As a iewell of golde in a swines snoute: so is a faire woman, which lacketh discretion.
23 Zokhumba za anthu olungama zimathera pa zabwino zokhazokha, koma chiyembekezo cha anthu oyipa chimathera mu ukali wa Mulungu.
The desire of the righteous is onely good: but the hope of the wicked is indignation.
24 Munthu wina amapatsako anzake zinthu mwaufulu nʼkumangolemererabe; wina amamana chomwe akanatha kupereka, koma kumanka nasawukabe.
There is that scattereth, and is more increased: but hee that spareth more then is right, surely commeth to pouertie.
25 Munthu wopereka mowolowamanja adzalemera; iye amene amathandiza ena iyenso adzathandizidwa.
The liberall person shall haue plentie: and he that watereth, shall also haue raine.
26 Anthu amatemberera womana anzake chakudya, koma madalitso amakhala pamutu pa munthu amene amagulitsa chakudyacho.
He that withdraweth the corne, the people will curse him: but blessing shalbe vpon the head of him that selleth corne.
27 Iye amene amafunafuna zabwino mwakhama amapeza zabwinozo, koma wofunafuna zoyipa zidzamupeza.
He that seeketh good things, getteth fauour: but he that seeketh euill, it shall come to him.
28 Aliyense amene amadalira chuma chake adzafota, koma wolungama adzaphukira ngati tsamba lobiriwira.
He that trusteth in his riches, shall fall: but the righteous shall florish as a leafe.
29 Wovutitsa a mʼnyumba mwake adzalowa mʼmavuto, ndipo chitsiru chidzakhala kapolo wa munthu wa nzeru.
He that troubleth his owne house, shall inherite the winde, and the foole shalbe seruant to the wise in heart.
30 Chipatso cha ntchito zabwino ndi moyo, ndipo kusatsata malamulo kumawonongetsa moyo.
The fruite of the righteous is as a tree of life, and he that winneth soules, is wise.
31 Ngati anthu olungama amalandira mphotho zawo pa dziko lapansi, kuli bwanji anthu osapembedza ndi ochimwa!
Beholde, the righteous shalbe recompensed in the earth: howe much more the wicked and the sinner?

< Miyambo 11 >