< Miyambo 10 >

1 Miyambo ya Solomoni: Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.
Син мудрий — потіха для батька, а син нерозумний — то смуток для неньки його.
2 Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
Не поможуть неправедні скарби, а справедливість від смерти визво́лює.
3 Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala; koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.
Не допустить Господь голодува́ти душу праведного, а набу́ток безбожників згине.
4 Wochita zinthu mwaulesi amasauka, koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.
Ледача рука до убо́зтва веде, рука ж роботя́ща збагачує.
5 Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru, koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.
Хто літом збирає — син мудрий, хто ж дрімає в жнива́ — син безпутній.
6 Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama, koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.
Благослове́нства на голову праведного, а уста безбожним прикриє наси́льство.
7 Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso, koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.
Пам'ять про праведного — на благослове́ння, а йме́ння безбожних загине.
8 Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo, koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.
Заповіді мудросердий приймає, але́ дурногу́бий впаде́.
9 Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka; koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.
Хто в невинності ходить, той ходить безпечно, а хто кривить дороги свої, буде ви́явлений.
10 Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto, koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.
Хто оком моргає, той смуток дає, але дурногу́бий впаде́.
11 Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo, koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.
Уста праведного — то джерело життя, а уста безбожним прикриє насильство.
12 Udani umawutsa mikangano, koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.
Нена́висть побуджує сва́рки, а любов покриває всі ви́ни.
13 Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu, koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.
В устах розумного мудрість знахо́диться, а різка — на спину безтя́много.
14 Anzeru amasunga chidziwitso koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.
Прихо́вують мудрі знання́, а уста нерозумного — близькі́ до загибелі.
15 Chuma cha munthu wolemera ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.
Маєток багатого — місто тверди́нне його, поги́біль убогих — їхні зли́дні.
16 Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama, koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.
Дорібок праведного — на життя, прибу́ток безбожного — в гріх.
17 Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo, koma wonyoza chidzudzulo amasochera.
Хто напу́чування стереже́ — той на сте́жці життя, а хто нехту́є карта́ння, той блу́дить.
18 Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama, ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.
Хто нена́висть ховає, в того губи брехли́ві, а хто на́клепи ширить, той дурнове́рхий.
19 Mawu akachuluka zolakwa sizisowa, koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.
Не бракує гріха в многомо́вності, а хто стримує губи свої, той розумний.
20 Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri, koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.
Язик праведного — то добі́рне срібло́, а розум безбожних — мізе́рний.
21 Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri; koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.
Пасу́ть багатьох губи праведного, безглузді ж умирають з неро́зуму.
22 Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma, ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.
Благослове́ння Господнє — воно збагачає, і сму́тку воно не прино́сить з собою.
23 Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa, koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.
Нешляхе́тне робити — заба́ва неві́гласа, а мудрість — люди́ні розумній.
24 Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira; chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.
Чого нечести́вий боїться, те при́йде на нього, а пра́гнення праведних спо́вняться.
25 Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa, koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.
Як буря, яка пронесе́ться, то й гине безбожний, а праведний має дові́чну осно́ву.
26 Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso, ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.
Як о́цет зубам, і як дим для оче́й, так лінивий для тих, хто його посилає.
27 Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo; koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.
Страх Господній примножує днів, а ро́ки безбожних вкоро́тяться.
28 Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe, koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.
Сподіва́ння для праведних — радість, а наді́я безбожних загине.
29 Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino, koma wochita zoyipa adzawonongeka.
Дорога Господня — тверди́ня неви́нним, а заги́біль — злочинцям.
30 Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.
Повік праведний не захита́ється, а безбожники не поживуть на землі.
31 Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru, koma lilime lokhota lidzadulidwa.
Уста праведного дають мудрість, а лукавий язик буде втятий.
32 Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula, koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.
Уста праведного уподо́бання знають, а уста безбожних — лука́вство.

< Miyambo 10 >