< Miyambo 10 >

1 Miyambo ya Solomoni: Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.
El hijo sabio alegra al padre, pero el necio es un dolor para su madre.
2 Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
La riqueza que proviene del pecado no tiene ningún beneficio, pero la justicia da la salvación de la muerte.
3 Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala; koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.
El Señor no permitirá que los rectos necesiten alimento, pero no saciarán su hambre los malhechores.
4 Wochita zinthu mwaulesi amasauka, koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.
El que tarda en su trabajo se empobrece, pero la mano del que está listo se enriquece.
5 Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru, koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.
El que en verano cosecha es un hijo que hace sabiamente; pero el que toma su descanso cuando se corta el grano es un hijo que causa vergüenza.
6 Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama, koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.
Las bendiciones están en la cabeza de los rectos, pero la cara de los pecadores estará cubierta de dolor.
7 Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso, koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.
La memoria de los rectos es una bendición, pero el nombre del malhechor se convertirá en polvo.
8 Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo, koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.
El hombre sabio de corazón se dejará gobernar, pero el hombre cuya charla es tonta caerá.
9 Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka; koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.
Aquel cuyos caminos son rectos irá a salvo, pero aquel cuyos caminos están torcidos será arruinado.
10 Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto, koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.
El que hace señales con sus ojos es causa de problemas, pero el que hace que un hombre vea sus errores es una causa de paz.
11 Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo, koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.
La boca del hombre recto es fuente de vida, pero la boca del malhechor es una copa amarga.
12 Udani umawutsa mikangano, koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.
El odio es una causa de actos violentos, pero todos los errores están cubiertos por el amor.
13 Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu, koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.
En los labios del que tiene conocimiento, se ve sabiduría; pero una vara está lista para la espalda de aquel que no tiene sentido.
14 Anzeru amasunga chidziwitso koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.
Los sabios acumulan conocimiento, pero la boca del necio es destrucción que está cerca.
15 Chuma cha munthu wolemera ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.
La propiedad del hombre rico es su pueblo fuerte: la necesidad del pobre es su destrucción.
16 Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama, koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.
La obra de los rectos da vida: el aumento del malhechor es una causa del pecado.
17 Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo, koma wonyoza chidzudzulo amasochera.
El que toma nota de la enseñanza es una forma de vida, pero el que abandona el entrenamiento es una causa de error.
18 Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama, ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.
El odio está encubierto por los labios del hombre mentiroso, y el que propaga mentiras es un insensato.
19 Mawu akachuluka zolakwa sizisowa, koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.
Donde se habla mucho, el pecado no tendrá fin, pero el que tiene la boca cerrada lo hace sabiamente.
20 Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri, koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.
La lengua del hombre recto es como plata probada; el corazón del malhechor es de poco valor.
21 Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri; koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.
Los labios del hombre recto dan de comer a los hombres, pero los necios mueren por falta de juicio.
22 Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma, ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.
La bendición del Señor da riqueza: y no añade tristeza consigo.
23 Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa, koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.
Al necio le parece bien hacer el mal, pero el hombre de buen juicio se deleita con la sabiduría.
24 Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira; chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.
Lo temido por el malvado vendrá a él, pero el hombre recto obtendrá su deseo.
25 Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa, koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.
Cuando el viento de la tormenta ha pasado, el pecador ya no se ve, pero el hombre recto está a salvo para siempre.
26 Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso, ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.
Como bebida ácida para los dientes y como humo para los ojos, así es el que odia el trabajo a los que lo envían.
27 Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo; koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.
El temor del Señor da larga vida, pero los años del malhechor serán acortados.
28 Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe, koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.
La esperanza del hombre recto dará alegría, pero la espera del malhechor tendrá su fin en la tristeza.
29 Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino, koma wochita zoyipa adzawonongeka.
El camino del Señor es una torre fuerte para el hombre recto, pero destrucción para los que trabajan mal.
30 Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.
El hombre recto nunca será movido, pero los malhechores no tendrán un lugar de descanso seguro en la tierra.
31 Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru, koma lilime lokhota lidzadulidwa.
La boca del hombre recto está floreciendo con sabiduría, pero la lengua retorcida será cortada.
32 Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula, koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.
Los labios del hombre recto tienen conocimiento de lo que agrada, pero retorcidos son las bocas de los malhechores.

< Miyambo 10 >