< Miyambo 10 >
1 Miyambo ya Solomoni: Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.
Provérbios de Salomão. O filho sábio alegra a seu pai, mas o filho louco é a tristeza de sua mãe.
2 Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
Os tesouros da impiedade de nada aproveitam; porém a justiça livra da morte.
3 Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala; koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.
O Senhor não deixa ter fome a alma do justo, mas a fazenda dos ímpios rechaça.
4 Wochita zinthu mwaulesi amasauka, koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.
O que trabalha com mão enganosa empobrece, mas a mão dos diligentes enriquece.
5 Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru, koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.
O que ajunta no verão é filho entendido, mas o que dorme na sega é filho que faz envergonhar.
6 Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama, koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.
Bençãos há sobre a cabeça do justo, mas a violência cobre a boca dos ímpios.
7 Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso, koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.
A memória do justo é abençoada, mas o nome dos ímpios apodrecerá.
8 Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo, koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.
O sábio de coração aceita os mandamentos, mas o louco de lábios será transtornado.
9 Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka; koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.
Quem anda em sinceridade, anda seguro; mas o que perverte os seus caminhos será conhecido.
10 Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto, koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.
O que acena com os olhos dá dores, e o tolo de lábios será transtornado.
11 Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo, koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.
A boca do justo é fonte de vida, mas a boca dos ímpios cobre a violência.
12 Udani umawutsa mikangano, koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.
O ódio excita contendas, mas o amor cobre todas as transgressões.
13 Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu, koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.
Nos lábios do entendido se acha a sabedoria, mas a vara é para as costas do falto de entendimento.
14 Anzeru amasunga chidziwitso koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.
Os sábios escondem a sabedoria; mas a boca do tolo está perto da ruína.
15 Chuma cha munthu wolemera ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.
A fazenda do rico é a cidade da sua fortaleza: a pobreza dos pobres é a sua ruína.
16 Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama, koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.
A obra do justo conduz à vida, as novidades do ímpio ao pecado.
17 Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo, koma wonyoza chidzudzulo amasochera.
O caminho para a vida é daquele que guarda a correção, mas o que deixa a repreensão faz errar.
18 Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama, ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.
O que encobre o ódio tem lábios falsos, e o que produz má fama é um insensato.
19 Mawu akachuluka zolakwa sizisowa, koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.
Na multidão de palavras não há falta de transgressão, mas o que modera os seus lábios é prudente.
20 Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri, koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.
Prata escolhida é a língua do justo: o coração dos ímpios é de nenhum preço.
21 Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri; koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.
Os lábios do justo apascentam a muitos, mas os tolos, por falta de entendimento, morrem.
22 Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma, ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.
A benção do Senhor é a que enriquece; e não lhe acrescenta dores.
23 Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa, koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.
Como brincadeira é para o tolo fazer abominação, mas sabedoria para o homem entendido.
24 Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira; chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.
O temor do ímpio virá sobre ele, mas o desejo dos justos Deus lhe cumprirá.
25 Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa, koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.
Como passa a tempestade, assim o ímpio mais não é; mas o justo tem perpétuo fundamento.
26 Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso, ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.
Como vinagre para os dentes, como o fumo para os olhos, assim é o preguiçoso para aqueles que o mandam.
27 Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo; koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.
O temor do Senhor aumenta os dias, mas os anos dos ímpios serão abreviados.
28 Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe, koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.
A esperança dos justos é alegria, mas a expectação dos ímpios perecerá.
29 Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino, koma wochita zoyipa adzawonongeka.
O caminho do Senhor é fortaleza para os retos, mas ruína será para os que obram iniquidade.
30 Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.
O justo nunca jamais será abalado, mas os ímpios não habitarão a terra.
31 Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru, koma lilime lokhota lidzadulidwa.
A boca do justo em abundância produz sabedoria, mas a língua da perversidade será desarreigada.
32 Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula, koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.
Os beiços do justo sabem o que agrada, mas a boca dos ímpios anda cheia de perversidades.