< Miyambo 10 >

1 Miyambo ya Solomoni: Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.
امثال سلیمان: پسر حکیم پدر خود رامسرور می‌سازد، اما پسر احمق باعث حزن مادرش می‌شود.۱
2 Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
گنجهای شرارت منفعت ندارد، اما عدالت از موت رهایی می‌دهد.۲
3 Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala; koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.
خداوند جان مرد عادل را نمی گذارد گرسنه بشود، اما آرزوی شریران را باطل می‌سازد.۳
4 Wochita zinthu mwaulesi amasauka, koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.
کسی‌که به‌دست سست کار می‌کند فقیرمی گردد، اما دست چابک غنی می‌سازد.۴
5 Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru, koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.
کسی‌که در تابستان جمع کند پسر عاقل است، اما کسی‌که در موسم حصاد می‌خوابد، پسر شرم‌آورنده است.۵
6 Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama, koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.
بر سر عادلان برکت‌ها است، اما ظلم دهان شریران را می‌پوشاند.۶
7 Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso, koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.
یادگار عادلان مبارک است، اما اسم شریران خواهد گندید.۷
8 Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo, koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.
دانادل، احکام را قبول می‌کند، اما احمق پرگو تلف خواهد شد.۸
9 Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka; koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.
کسی‌که به راستی راه رود، در امنیت سالک گردد، و کسی‌که راه خود را کج می‌سازد آشکارخواهد شد.۹
10 Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto, koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.
هر‌که چشمک می‌زند الم می‌رساند، امااحمق پرگو تلف می‌شود.۱۰
11 Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo, koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.
دهان عادلان چشمه حیات‌است، اما ظلم دهان شریران را می‌پوشاند.۱۱
12 Udani umawutsa mikangano, koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.
بغض نزاعها می‌انگیزاند، اما محبت هر گناه را مستور می‌سازد.۱۲
13 Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu, koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.
در لبهای فطانت پیشگان حکمت یافت می‌شود، اما چوب به جهت پشت مردناقص العقل است.۱۳
14 Anzeru amasunga chidziwitso koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.
حکیمان علم را ذخیره می‌کنند، اما دهان احمق نزدیک به هلاکت است.۱۴
15 Chuma cha munthu wolemera ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.
اموال دولتمندان شهر حصاردار ایشان می‌باشد، اما بینوایی فقیران هلاکت ایشان است.۱۵
16 Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama, koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.
عمل مرد عادل مودی به حیات‌است، امامحصول شریر به گناه می‌انجامد.۱۶
17 Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo, koma wonyoza chidzudzulo amasochera.
کسی‌که تادیب را نگاه دارد در طریق حیات‌است، اما کسی‌که تنبیه را ترک نماید گمراه می‌شود.۱۷
18 Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama, ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.
کسی‌که بغض را می‌پوشاند دروغگومی باشد. کسی‌که بهتان را شیوع دهد احمق است.۱۸
19 Mawu akachuluka zolakwa sizisowa, koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.
کثرت کلام از گناه خالی نمی باشد، اما آنکه لبهایش را ضبط نماید عاقل است.۱۹
20 Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri, koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.
زبان عادلان نقره خالص است، اما دل شریران لاشی ء می‌باشد.۲۰
21 Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri; koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.
لبهای عادلان بسیاری را رعایت می‌کند، اما احمقان از بی‌عقلی می‌میرند.۲۱
22 Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma, ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.
برکت خداوند دولتمند می‌سازد، و هیچ زحمت بر آن نمی افزاید.۲۲
23 Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa, koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.
جاهل در عمل بد اهتزاز دارد، و صاحب فطانت در حکمت.۲۳
24 Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira; chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.
خوف شریران به ایشان می‌رسد، و آرزوی عادلان به ایشان عطا خواهد شد.۲۴
25 Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa, koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.
مثل گذشتن گردباد، شریر نابود می‌شود، امامرد عادل بنیاد جاودانی است.۲۵
26 Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso, ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.
چنانکه سرکه برای دندان و دود برای چشمان است، همچنین است مرد کاهل برای آنانی که او را می‌فرستند.۲۶
27 Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo; koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.
ترس خداوند عمر را طویل می‌سازد، اماسالهای شریران کوتاه خواهد شد.۲۷
28 Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe, koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.
انتظار عادلان شادمانی است، اما امیدشریران ضایع خواهد شد.۲۸
29 Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino, koma wochita zoyipa adzawonongeka.
طریق خداوند به جهت کاملان قلعه است، اما به جهت عاملان شر هلاکت می‌باشد.۲۹
30 Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.
مرد عادل هرگز متحرک نخواهد شد، اماشریران در زمین ساکن نخواهند گشت.۳۰
31 Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru, koma lilime lokhota lidzadulidwa.
دهان صدیقان حکمت را می‌رویاند، امازبان دروغگویان از ریشه‌کنده خواهد شد.۳۱
32 Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula, koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.
لبهای عادلان به امور مرضیه عارف است، اما دهان شریران پر از دروغ‌ها است.۳۲

< Miyambo 10 >