< Miyambo 10 >

1 Miyambo ya Solomoni: Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.
Filius sapiens laetificat patrem: filius vero stultus moestitia est matris suae.
2 Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
Nil proderunt thesauri impietatis: iustitia vero liberabit a morte.
3 Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala; koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.
Non affliget Dominus fame animam iusti, et insidias impiorum subvertet.
4 Wochita zinthu mwaulesi amasauka, koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.
Egestatem operata est manus remissa: manus autem fortium divitias parat. Qui nititur mendaciis, hic pascit ventos: idem autem ipse sequitur aves volantes.
5 Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru, koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.
Qui congregat in messe, filius sapiens est: qui autem stertit aestate, filius confusionis.
6 Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama, koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.
Benedictio Domini super caput iusti: os autem impiorum operit iniquitas.
7 Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso, koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.
Memoria iusti cum laudibus: et nomen impiorum putrescet.
8 Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo, koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.
Sapiens corde praecepta suscipit: stultus caeditur labiis.
9 Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka; koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.
Qui ambulat simpliciter, ambulat confidenter: qui autem depravat vias suas, manifestus erit.
10 Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto, koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.
Qui annuit oculo, dabit dolorem: et stultus labiis verberabitur.
11 Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo, koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.
Vena vitae, os iusti: et os impiorum operit iniquitatem.
12 Udani umawutsa mikangano, koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.
Odium suscitat rixas: et universa delicta operit charitas.
13 Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu, koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.
In labiis sapientis invenitur sapientia: et virga in dorso eius qui indiget corde.
14 Anzeru amasunga chidziwitso koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.
Sapientes abscondunt scientiam: os autem stulti confusioni proximum est.
15 Chuma cha munthu wolemera ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.
Substantia divitis, urbs fortitudinis eius: pavor pauperum, egestas eorum.
16 Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama, koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.
Opus iusti ad vitam: fructus autem impii ad peccatum.
17 Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo, koma wonyoza chidzudzulo amasochera.
Via vitae, custodienti disciplinam: qui autem increpationes relinquit, errat.
18 Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama, ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.
Abscondunt odium labia mendacia: qui profert contumeliam, insipiens est.
19 Mawu akachuluka zolakwa sizisowa, koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.
In multiloquio non deerit peccatum: qui autem moderatur labia sua prudentissimus est.
20 Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri, koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.
Argentum electum, lingua iusti: cor autem impiorum pro nihilo.
21 Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri; koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.
Labia iusti erudiunt plurimos: qui autem indocti sunt, in cordis egestate morientur.
22 Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma, ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.
Benedictio Domini divites facit, nec sociabitur eis afflictio.
23 Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa, koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.
Quasi per risum stultus operatur scelus: sapientia autem est viro prudentia.
24 Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira; chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.
Quod timet impius, veniet super eum: desiderium suum iustus dabitur.
25 Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa, koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.
Quasi tempestas transiens non erit impius: iustus autem quasi fundamentum sempiternum.
26 Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso, ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.
Sicut acetum dentibus, et fumus oculis, sic piger his, qui miserunt eum.
27 Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo; koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.
Timor Domini apponet dies: et anni impiorum breviabuntur.
28 Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe, koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.
Expectatio iustorum laetitia: spes autem impiorum peribit.
29 Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino, koma wochita zoyipa adzawonongeka.
Fortitudo simplicis via Domini: et pavor his, qui operantur malum.
30 Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.
Iustus in aeternum non commovebitur: impii autem non habitabunt super terram.
31 Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru, koma lilime lokhota lidzadulidwa.
Os iusti parturiet sapientiam: lingua pravorum peribit.
32 Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula, koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.
Labia iusti considerant placita: et os impiorum perversa.

< Miyambo 10 >