< Miyambo 10 >

1 Miyambo ya Solomoni: Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.
Salomon sananlaskut. Viisas poika on isänsä ilo, mutta hullu poika on äidillensä murheeksi.
2 Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
Väärin saatu tavara ei ole hyödyllinen; mutta vanhurskaus vapauttaa kuolemasta.
3 Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala; koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.
Ei Herra anna vanhurskasten sielun nälkää kärsiä, mutta jumalattomain väärin saadut hän hajoittaa.
4 Wochita zinthu mwaulesi amasauka, koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.
Petollinen käsi tekee köyhäksi, mutta ahkera saattaa rikkaaksi.
5 Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru, koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.
Joka suvella kokoo, hän on toimellinen, mutta joka elonaikana makaa, hän tulee häpiään.
6 Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama, koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.
Siunaus on vanhurskaan pään päällä, mutta jumalattoman suun peittää vääryys.
7 Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso, koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.
Vanhurskaan muisto pysyy siunauksessa, vaan jumalattomain nimi mätänee.
8 Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo, koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.
Joka sydämestänsä viisas on, hän ottaa käskyt vastaan; mutta jolla hullut huulet ovat, se saa haavoja.
9 Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka; koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.
Joka nuhteettomasti vaeltaa, hän elää murheetoinna; mutta joka väärällä tiellä vaeltaa, hän tulee ilmi.
10 Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto, koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.
Joka silmää iskee, hän vaivaa matkaan saattaa, ja jolla hullut huulet ovat, hän saa haavoja.
11 Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo, koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.
Vanhurskaan suu on elämän lähde, mutta jumalattoman suun peittää vääryys.
12 Udani umawutsa mikangano, koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.
Viha riidan saattaa, mutta rakkaus peittää kaikki rikokset.
13 Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu, koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.
Toimellisten huulissa löydetään viisaus, vaan tyhmäin selkään tarvitaan vitsa.
14 Anzeru amasunga chidziwitso koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.
Viisaat opin kätkevät, vaan hulluin suu on täynnä vahinkoa.
15 Chuma cha munthu wolemera ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.
Rikkaan tavara on hänen vahva kaupunkinsa; mutta köyhyys tekee köyhän pelkuriksi.
16 Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama, koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.
Vanhurskaus tekee työtä hengen ylöspitämiseksi, mutta jumalattoman saalis on symmiksi.
17 Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo, koma wonyoza chidzudzulo amasochera.
Joka kurituksen ottaa vastaan, hän on elämän tiellä; mutta joka rangaistuksen heittää pois, hän menee väärin.
18 Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama, ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.
Petolliset suut peittävät vainon, ja joka panettelee, hän on tyhmä.
19 Mawu akachuluka zolakwa sizisowa, koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.
Jossa paljo puhutaan, siitä ei synti ole kaukana; mutta joka huulensa hillitsee, hän on toimellinen.
20 Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri, koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.
Vanhurskaan kieli on kalliimpi hopiaa, mutta jumalattoman sydän on miinkuin ei mitään.
21 Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri; koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.
Vanhurskaan huulet monta ravitsevat, mutta hullut kuolevat hulluudessa.
22 Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma, ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.
Herran siunaus tekee rikkaaksi ilman vaivaa.
23 Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa, koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.
Hullu tekee pahaa ja nauraa sitä, vaan viisas pitää siitä vaarinsa.
24 Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira; chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.
Mitä jumalatoin pelkää, se hänelle tapahtuu, ja mitä vanhurskaat himoitsevat, sitä heille annetaan.
25 Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa, koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.
Jumalatoin on niinkuin tuulispää, joka menee ohitse ja tyhjiksi raukee; mutta vanhurskas pysyy ijankaikkisesti.
26 Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso, ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.
Niin kuin etikka tekee pahaa hampaille ja savu silmille, niin on laiska niiden mielestä paha, jotka hänen lähettävät.
27 Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo; koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.
Herran pelko enentää päiviä, vaan jumalattomain vuodet vähennetään.
28 Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe, koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.
Vanhurskaan toivo on ilo, mutta jumalattomain toivo katoo.
29 Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino, koma wochita zoyipa adzawonongeka.
Herran tie on hurskasten väkevyys, mutta pahointekiät ovat pelkurit.
30 Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.
Vanhurskas pysyy aina kohdallansa kukistamatta, mutta jumalattoman ei pidä asuman maan päällä.
31 Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru, koma lilime lokhota lidzadulidwa.
Vanhurskaan suu tuottaa viisauden, vaan vääräin kieli hukutetaan.
32 Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula, koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.
Vanhurskaan huulet opettavat terveellisiä asioita, vaan jumalattoman suu on täynnä vääryyttä.

< Miyambo 10 >