< Miyambo 10 >

1 Miyambo ya Solomoni: Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.
The proverbs of Solomon. A wise son maketh a glad father: but a foolish son is the heaviness of his mother.
2 Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
Treasures of wickedness profit nothing: but righteousness delivereth from death.
3 Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala; koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.
The LORD will not allow the soul of the righteous to famish: but he casteth away the substance of the wicked.
4 Wochita zinthu mwaulesi amasauka, koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.
He becometh poor that dealeth with a slack hand: but the hand of the diligent maketh rich.
5 Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru, koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.
He that gathereth in summer is a wise son: but he that sleepeth in harvest is a son that causeth shame.
6 Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama, koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.
Blessings are upon the head of the just: but violence covereth the mouth of the wicked.
7 Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso, koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.
The memory of the just is blessed: but the name of the wicked shall perish.
8 Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo, koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.
The wise in heart will receive commandments: but a prating fool shall fall.
9 Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka; koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.
He that walketh uprightly walketh surely: but he that perverteth his ways shall be known.
10 Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto, koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.
He that winketh with the eye causeth sorrow: but a prating fool shall fall.
11 Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo, koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.
The mouth of a righteous man is a well of life: but violence covereth the mouth of the wicked.
12 Udani umawutsa mikangano, koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.
Hatred stirreth up strifes: but love covereth all sins.
13 Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu, koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.
In the lips of him that hath understanding wisdom is found: but a rod is for the back of him that is void of understanding.
14 Anzeru amasunga chidziwitso koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.
Wise men lay up knowledge: but the mouth of the foolish is near destruction.
15 Chuma cha munthu wolemera ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.
The rich man’s wealth is his strong city: the destruction of the poor is their poverty.
16 Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama, koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.
The labour of the righteous tendeth to life: the fruit of the wicked to sin.
17 Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo, koma wonyoza chidzudzulo amasochera.
He is in the way of life that keepeth instruction: but he that refuseth reproof erreth.
18 Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama, ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.
He that hideth hatred with lying lips, and he that uttereth a slander, is a fool.
19 Mawu akachuluka zolakwa sizisowa, koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.
In the multitude of words there lacketh not sin: but he that holdeth his lips is wise.
20 Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri, koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.
The tongue of the just is as choice silver: the heart of the wicked is little worth.
21 Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri; koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.
The lips of the righteous feed many: but fools die for lack of wisdom.
22 Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma, ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.
The blessing of the LORD, it maketh rich, and he addeth no sorrow with it.
23 Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa, koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.
It is as sport to a fool to do mischief: but a man of understanding hath wisdom.
24 Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira; chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.
The fear of the wicked, it shall come upon him: but the desire of the righteous shall be granted.
25 Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa, koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.
As the whirlwind passeth, so is the wicked no more: but the righteous is an everlasting foundation.
26 Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso, ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.
As vinegar to the teeth, and as smoke to the eyes, so is the sluggard to them that send him.
27 Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo; koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.
The fear of the LORD prolongeth days: but the years of the wicked shall be shortened.
28 Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe, koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.
The hope of the righteous shall be gladness: but the expectation of the wicked shall perish.
29 Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino, koma wochita zoyipa adzawonongeka.
The way of the LORD is strength to the upright: but destruction shall be to the workers of iniquity.
30 Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.
The righteous shall never be removed: but the wicked shall not inhabit the earth.
31 Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru, koma lilime lokhota lidzadulidwa.
The mouth of the just bringeth forth wisdom: but the perverse tongue shall be cut out.
32 Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula, koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.
The lips of the righteous know what is acceptable: but the mouth of the wicked speaketh perverseness.

< Miyambo 10 >