< Miyambo 10 >
1 Miyambo ya Solomoni: Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.
Proverbs of Solomon. A wise son causes a father to rejoice, And a foolish son [is] an affliction to his mother.
2 Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
Treasures of wickedness do not profit, And righteousness delivers from death.
3 Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala; koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.
YHWH does not cause the soul of the righteous to hunger, And He thrusts away the desire of the wicked.
4 Wochita zinthu mwaulesi amasauka, koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.
Poor [is] he who is working [with] a slothful hand, And the hand of the diligent makes rich.
5 Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru, koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.
Whoever is gathering in summer [is] a wise son, Whoever is sleeping in harvest [is] a son causing shame.
6 Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama, koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.
Blessings [are] for the head of the righteous, And the mouth of the wicked covers violence.
7 Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso, koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.
The remembrance of the righteous [is] for a blessing, And the name of the wicked rots.
8 Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo, koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.
The wise in heart accepts commands, And a talkative fool kicks.
9 Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka; koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.
Whoever is walking in integrity walks confidently, And whoever is perverting his ways is known.
10 Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto, koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.
Whoever is winking the eye gives grief, And a talkative fool kicks.
11 Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo, koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.
A fountain of life [is] the mouth of the righteous, And the mouth of the wicked covers violence.
12 Udani umawutsa mikangano, koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.
Hatred awakens contentions, And love covers over all transgressions.
13 Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu, koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.
Wisdom is found in the lips of the intelligent, And a rod [is] for the back of him who is lacking understanding.
14 Anzeru amasunga chidziwitso koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.
The wise lay up knowledge, and the mouth of a fool [is] near ruin.
15 Chuma cha munthu wolemera ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.
The wealth of the rich [is] his strong city, The ruin of the poor [is] their poverty.
16 Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama, koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.
The wage of the righteous [is] for life, The increase of the wicked for sin.
17 Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo, koma wonyoza chidzudzulo amasochera.
A traveler to life [is] he who is keeping instruction, And whoever is forsaking rebuke is erring.
18 Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama, ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.
Whoever is covering hatred with lying lips, And whoever is bringing out an evil report is a fool.
19 Mawu akachuluka zolakwa sizisowa, koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.
In the abundance of words transgression does not cease, And whoever is restraining his lips [is] wise.
20 Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri, koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.
The tongue of the righteous [is] chosen silver, The heart of the wicked—as a little thing.
21 Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri; koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.
The lips of the righteous delight many, And fools die for lack of heart.
22 Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma, ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.
The blessing of YHWH—it makes rich, And He adds no grief with it.
23 Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa, koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.
To execute inventions [is] as play to a fool, And wisdom to a man of understanding.
24 Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira; chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.
The feared thing of the wicked meets him, And the desire of the righteous is given.
25 Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa, koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.
As the passing by of a windstorm, So the wicked is not, And the righteous is a perpetual foundation.
26 Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso, ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.
As vinegar to the teeth, And as smoke to the eyes, So [is] the slothful to those sending him.
27 Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo; koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.
The fear of YHWH adds days, And the years of the wicked are shortened.
28 Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe, koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.
The hope of the righteous [is] joyful, And the expectation of the wicked perishes.
29 Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino, koma wochita zoyipa adzawonongeka.
The way of YHWH [is] strength to the perfect, And ruin to workers of iniquity.
30 Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.
The righteous is not moved for all time, And the wicked do not inhabit the earth.
31 Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru, koma lilime lokhota lidzadulidwa.
The mouth of the righteous utters wisdom, And the tongue of contrariness is cut out.
32 Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula, koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.
The lips of the righteous know a pleasing thing, And the mouth of the wicked perverseness!