< Miyambo 10 >

1 Miyambo ya Solomoni: Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.
The Proverbs of Solomon. A wise son maketh a glad father; but a foolish son is the grief of his mother.
2 Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
Treasures of wickedness profit nothing; but righteousness delivereth from death.
3 Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala; koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.
Jehovah suffereth not the soul of the righteous [man] to famish; but he repelleth the craving of the wicked.
4 Wochita zinthu mwaulesi amasauka, koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.
He cometh to want that dealeth with a slack hand; but the hand of the diligent maketh rich.
5 Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru, koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.
He that gathereth in summer is a wise son; he that sleepeth in harvest is a son that causeth shame.
6 Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama, koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.
Blessings are upon the head of a righteous [man]; but the mouth of the wicked covereth violence.
7 Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso, koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.
The memory of the righteous [man] shall be blessed; but the name of the wicked shall rot.
8 Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo, koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.
The wise in heart receiveth commandments; but a prating fool shall fall.
9 Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka; koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.
He that walketh in integrity walketh securely; but he that perverteth his ways shall be known.
10 Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto, koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.
He that winketh with the eye causeth grief, and a prating fool shall fall.
11 Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo, koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.
The mouth of a righteous [man] is a fountain of life; but the mouth of the wicked covereth violence.
12 Udani umawutsa mikangano, koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.
Hatred stirreth up strifes; but love covereth all transgressions.
13 Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu, koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.
In the lips of an intelligent [man] wisdom is found; but a rod is for the back of him that is void of understanding.
14 Anzeru amasunga chidziwitso koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.
The wise lay up knowledge; but the mouth of the fool is near destruction.
15 Chuma cha munthu wolemera ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.
The rich man's wealth is his strong city; the destruction of the poor is their poverty.
16 Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama, koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.
The labour of a righteous [man] [tendeth] to life; the revenue of a wicked [man], to sin.
17 Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo, koma wonyoza chidzudzulo amasochera.
Keeping instruction is the path to life; but he that forsaketh reproof goeth astray.
18 Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama, ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.
He that covereth hatred hath lying lips, and he that sendeth forth a slander is a fool.
19 Mawu akachuluka zolakwa sizisowa, koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.
In the multitude of words there wanteth not transgression; but he that restraineth his lips doeth wisely.
20 Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri, koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.
The tongue of the righteous [man] is [as] choice silver; the heart of the wicked is little worth.
21 Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri; koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.
The lips of a righteous [man] feed many; but fools die for want of understanding.
22 Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma, ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.
The blessing of Jehovah, it maketh rich, and he addeth no sorrow to it.
23 Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa, koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.
It is as sport to a foolish [man] to do wickedness; but a man of understanding hath wisdom.
24 Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira; chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.
The fear of a wicked [man], it shall come upon him; but the desire of the righteous shall be granted.
25 Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa, koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.
As a whirlwind passeth, so is the wicked no [more]; but the righteous is an everlasting foundation.
26 Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso, ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.
As vinegar to the teeth, and as smoke to the eyes, so is the sluggard to them that send him.
27 Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo; koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.
The fear of Jehovah prolongeth days; but the years of the wicked shall be shortened.
28 Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe, koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.
The hope of the righteous is joy; but the expectation of the wicked shall perish.
29 Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino, koma wochita zoyipa adzawonongeka.
The way of Jehovah is strength to the perfect [man], but destruction to the workers of iniquity.
30 Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.
The righteous [man] shall never be moved; but the wicked shall not inhabit the land.
31 Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru, koma lilime lokhota lidzadulidwa.
The mouth of a righteous [man] putteth forth wisdom; but the froward tongue shall be cut out.
32 Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula, koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.
The lips of a righteous [man] know what is acceptable; but the mouth of the wicked is frowardness.

< Miyambo 10 >