< Miyambo 10 >

1 Miyambo ya Solomoni: Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.
Ngeche mag Solomon: Wuowi mariek kelo mor ni wuon mare, to wuowi mofuwo miyo min mare chuny lit.
2 Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
Mwandu moyudi e yo marach onge gi ohala; to tim makare reso ji e tho.
3 Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala; koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.
Jehova Nyasaye ok we ngʼat makare obed gi kech, to oketho gombo mar joricho.
4 Wochita zinthu mwaulesi amasauka, koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.
Lwedo manyap miyo ngʼato bedo jachan, to lwedo ma jakinda kelo mwandu.
5 Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru, koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.
Ngʼat makayo cham e kinde oro en wuowi mariek, to ngʼat ma nindo kinde keyo en wuowi makwodo wich.
6 Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama, koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.
Gweth sidho kondo mar loch ewi ngʼat makare, to timbe mahundu opongʼ e dho ngʼat marach.
7 Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso, koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.
Paro miparogo ngʼat makare nobed gweth, to nying ngʼat marach nolal.
8 Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo, koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.
Ngʼat mariek e chunye rwako chike, to ngʼat mofuwo ma wachne ngʼeny dhi e kethruok.
9 Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka; koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.
Ngʼat mobidhore wuotho kaonge luoro, to ngʼatno maluwo yore mobam ibiro yudo mapiyo.
10 Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto, koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.
Ngʼat madiemo wangʼe giwuond kelo kuyo, to ngʼat mofuwo ma wachne ngʼeny dhi e kethruok.
11 Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo, koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.
Dho ngʼat makare en soko mar ngima, to timbe mahundu opongʼo dho ngʼat marach.
12 Udani umawutsa mikangano, koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.
Sigu kelo miero, to hera umo maricho duto.
13 Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu, koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.
Rieko iyudo e dho jogo mongʼeyo tiend wach, to luth en mar ngʼe ngʼatno maonge gi rieko mar ngʼado bura.
14 Anzeru amasunga chidziwitso koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.
Joma riek okano ngʼeyo, to dho joma ofuwo kelo kethruok.
15 Chuma cha munthu wolemera ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.
Mwandu mar jomoko e ohinga mochiel motegno ma gigengʼorego, to dhier e kethruok mar jochan.
16 Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama, koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.
Pok joma kare kelonegi ngima, to mwandu ma joricho yudo kelonegi kum.
17 Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo, koma wonyoza chidzudzulo amasochera.
Ngʼat mawinjo weche mirieyego wuotho e yo madhiyo e ngima, to ngʼat motamore kethone tero ji mamoko e yor lal.
18 Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama, ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.
Ngʼatno mapando sigu manie chunye, dhoge nigi miriambo, to ngʼatno ma jakwoth ofuwo.
19 Mawu akachuluka zolakwa sizisowa, koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.
Ka weche ngʼeny, to richo ok nyal bare ma ok obetie, to ngʼat marito lewe oriek.
20 Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri, koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.
Lew ngʼat makare en fedha mowal, to chuny ngʼat marach nigi ohala matin.
21 Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri; koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.
Dho ngʼat makare konyo ji mangʼeny, to ngʼat mofuwo tho nikech rem mar ngʼeyo ngʼado bura.
22 Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma, ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.
Gweth mar Jehova Nyasaye kelo mwandu, kendo ok omed chandruok kuome.
23 Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa, koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.
Ngʼat mofuwo yudo mor e timbe maricho, to ngʼat man-gi winjo bedo mamor kuom rieko.
24 Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira; chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.
Gima ngʼat marach oluoro biro loye; to gima ngʼat makare dwaro ibiro miye.
25 Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa, koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.
Ka auka mager ofuto, to joricho otieko; to joma kare chungo motegno nyaka chiengʼ.
26 Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso, ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.
Mana kaka kong awayo machamo lak kendo ka iro malungo wenge, e kaka jasamuoyo ni jogo moore.
27 Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo; koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.
Luoro Jehova Nyasaye miyo idak amingʼa, to higni mar ngʼat marach ingʼado bedo machwok.
28 Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe, koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.
Geno mar joma kare en mor, to geno mar joricho nolal nono.
29 Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino, koma wochita zoyipa adzawonongeka.
Yor Jehova Nyasaye e kar pondo ni joma kare, to en kethruok ni jogo matimo richo.
30 Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.
Joma kare ok nopudh ngangʼ, to joricho ok nodongʼ e piny.
31 Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru, koma lilime lokhota lidzadulidwa.
Dho joma kare kelo rieko, to lep mar richo nongʼad oko.
32 Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula, koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.
Lew joma kare ongʼeyo gima owinjore, to dho joricho wacho mana gik mochido.

< Miyambo 10 >