< Miyambo 10 >

1 Miyambo ya Solomoni: Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.
Salomos ordsprog. Viis søn glæder sin fader, tåbelig søn er sin moders sorg.
2 Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
Gudløsheds skatte gavner intet, men retfærd redder fra død.
3 Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala; koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.
HERREN lader ej en retfærdig sulte, men gudløses attrå støder han fra sig.
4 Wochita zinthu mwaulesi amasauka, koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.
Doven hånd skaber fattigdom, flittiges hånd gør rig.
5 Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru, koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.
En klog søn samler om sommeren, en dårlig sover om høsten.
6 Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama, koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.
Velsignelse er for retfærdiges hoved, på uret gemmer gudløses mund.
7 Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso, koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.
Den retfærdiges minde velsignes, gudløses navn smuldrer hen.
8 Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo, koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.
Den vise tager mod påbud, den brovtende dåre styrtes.
9 Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka; koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.
Hvo lydefrit vandrer, vandrer trygt; men hvo der går krogveje, ham går det ilde.
10 Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto, koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.
Blinker man med øjet, volder man ondt, den brovtende dåre styrtes.
11 Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo, koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.
Den retfærdiges mund er en livsens kilde, på uret gemmer gudløses mund.
12 Udani umawutsa mikangano, koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.
Had vækker Splid, Kærlighed skjuler alle Synder.
13 Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu, koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.
På den kloges Læber fnder man Visdom, Stok er til Ryg på Mand uden Vid.
14 Anzeru amasunga chidziwitso koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.
De vise gemmer den indsigt, de har, Dårens Mund er truende Våde.
15 Chuma cha munthu wolemera ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.
Den riges Gods er hans faste Stad, Armod de ringes Våde.
16 Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama, koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.
Den retfærdiges Vinding tjener til Liv, den gudløses Indtægt til Synd.
17 Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo, koma wonyoza chidzudzulo amasochera.
At vogte på Tugt er Vej til Livet, vild farer den, som viser Revselse fra sig.
18 Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama, ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.
Retfærdige Læber tier om Had, en Tåbe er den, der udspreder Rygter.
19 Mawu akachuluka zolakwa sizisowa, koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.
Ved megen Tale undgås ej Brøde, klog er den, der vogter sin Mund.
20 Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri, koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.
Den retfærdiges Tunge er udsøgt Sølv, gudløses Hjerte er intet værd.
21 Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri; koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.
Den retfærdiges Læber nærer mange, Dårerne dør af Mangel på Vid.
22 Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma, ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.
HERRENs Velsignelse, den gør rig, Slid og Slæb lægger intet til.
23 Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa, koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.
For Tåben er Skændselsgerning en Leg, Visdom er Leg for Mand med Indsigt.
24 Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira; chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.
Hvad en gudløs frygter, kommer over hans Hoved, hvad retfærdige ønsker, bliver dem givet.
25 Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa, koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.
Når Storm farer frem, er den gudløse borte, den retfærdige står på evig Grund.
26 Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso, ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.
Som Eddike for Tænder og Røg for Øjne så er den lade for dem, der sender ham.
27 Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo; koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.
HERRENs Frygt lægger dage til, gudløses År kortes af.
28 Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe, koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.
Retfærdige har Glæde i Vente, gudløses Håb vil briste.
29 Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino, koma wochita zoyipa adzawonongeka.
For lydefri Vandel er HERREN et Værn, men en Rædsel for Udådsmænd.
30 Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.
Den retfærdige rokkes aldrig, ikke skal gudløse bo i Landet.
31 Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru, koma lilime lokhota lidzadulidwa.
Den retfærdiges Mund bærer Visdoms Frugt, den falske Tunge udryddes.
32 Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula, koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.
Den retfærdiges Læber søger yndest, gudløses Mund bærer Falskheds Frugt.

< Miyambo 10 >