< Miyambo 10 >
1 Miyambo ya Solomoni: Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.
Syn moudrý obveseluje otce, ale syn bláznivý zámutkem jest matce své.
2 Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
Neprospívají pokladové bezbožně nabytí, ale spravedlnost vytrhuje od smrti.
3 Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala; koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.
Nedopustí lačněti Hospodin duši spravedlivého, statek pak bezbožných rozptýlí.
4 Wochita zinthu mwaulesi amasauka, koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.
K nouzi přivodí ruka lstivá, ruka pak pracovitých zbohacuje.
5 Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru, koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.
Kdo shromažďuje v létě, jest syn rozumný; kdož vyspává ve žni, jest syn, kterýž hanbu činí.
6 Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama, koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.
Požehnání jest nad hlavou spravedlivého, ale ústa bezbožných přikrývají ukrutnost.
7 Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso, koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.
Památka spravedlivého požehnaná, ale jméno bezbožných smrdí.
8 Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo, koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.
Moudré srdce přijímá přikázaní, ale blázen od rtů svých padne.
9 Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka; koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.
Kdo chodí upřímě, chodí doufanlivě; kdož pak převrací cesty své, vyjeven bude.
10 Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto, koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.
Kdo mhourá okem, uvodí nesnáz; a kdož jest bláznivých rtů, padne.
11 Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo, koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.
Pramen života jsou ústa spravedlivého, ale ústa bezbožných přikrývají ukrutnost.
12 Udani umawutsa mikangano, koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.
Nenávist vzbuzuje sváry, ale láska přikrývá všecka přestoupení.
13 Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu, koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.
Ve rtech rozumného nalézá se moudrost, ale kyj na hřbetě blázna.
14 Anzeru amasunga chidziwitso koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.
Moudří skrývají umění, úst pak blázna blízké jest setření.
15 Chuma cha munthu wolemera ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.
Zboží bohatého jest město pevné jeho, ale nouze jest chudých setření.
16 Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama, koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.
Práce spravedlivého jest k životu, nábytek pak bezbožných jest k hříchu.
17 Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo, koma wonyoza chidzudzulo amasochera.
Stezkou života jde, kdož přijímá trestání; ale kdož pohrdá domlouváním, bloudí.
18 Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama, ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.
Kdož přikrývá nenávist rty lživými, i kdož uvodí v lehkost, ten blázen jest.
19 Mawu akachuluka zolakwa sizisowa, koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.
Mnohé mluvení nebývá bez hříchu, kdož pak zdržuje rty své, opatrný jest.
20 Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri, koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.
Stříbro výborné jest jazyk spravedlivého, ale srdce bezbožných za nic nestojí.
21 Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri; koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.
Rtové spravedlivého pasou mnohé, blázni pak pro bláznovství umírají.
22 Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma, ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.
Požehnání Hospodinovo zbohacuje, a to beze všeho trápení.
23 Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa, koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.
Za žert jest bláznu činiti nešlechetnost, ale muž rozumný moudrosti se drží.
24 Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira; chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.
Èeho se bojí bezbožný, to přichází na něj; ale čehož žádají spravedliví, dává Bůh.
25 Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa, koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.
Jakož pomíjí vichřice, tak nestane bezbožníka, spravedlivý pak jest základ stálý.
26 Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso, ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.
Jako ocet zubům, a jako dým očima, tak jest lenivý těm, kteříž jej posílají.
27 Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo; koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.
Bázeň Hospodinova přidává dnů, léta pak bezbožných ukrácena bývají.
28 Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe, koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.
Očekávání spravedlivých jest potěšení, naděje pak bezbožných zahyne.
29 Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino, koma wochita zoyipa adzawonongeka.
Silou jest upřímému cesta Hospodinova, a strachem těm, kteříž činí nepravost.
30 Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.
Spravedlivý na věky se nepohne, bezbožní pak nebudou bydliti v zemi.
31 Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru, koma lilime lokhota lidzadulidwa.
Ústa spravedlivého vynášejí moudrost, ale jazyk převrácený vyťat bude.
32 Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula, koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.
Rtové spravedlivého znají, což jest Bohu libého, ústa pak bezbožných převrácené věci.