< Miyambo 1 >
1 Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
Pregovori Salomona, Davidovega sina, Izraelovega kralja,
2 Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
da bi spoznali modrost in poučevanje, da bi zaznali besede razumevanja,
3 kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
da bi sprejeli poučevanje modrosti, pravice, sodbe in nepristranskost;
4 Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
da bi dali premetenost preprostemu, mladeniču spoznanje in preudarnost.
5 Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
Moder človek bo slišal in bo povečal učenje in razumen človek se bo dokopal k modrim nasvetom,
6 kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
da bo razumel pregovor in razlago, besede modrih in njihove temne izreke.
7 Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
Strah Gospodov je začetek spoznanja, toda bedaki prezirajo modrost in poučevanje.
8 Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
Moj sin, prisluhni poučevanju svojega očeta in ne zapusti postave svoje matere,
9 Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
kajti ona bosta ornament milosti tvoji glavi in verižici okoli tvojega vratu.
10 Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
Moj sin, če te grešniki privabljajo, ne privoli.
11 Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
Če rečejo: »Pridi z nami, v zasedi prežimo na kri, brez razloga se tajno pritajimo za nedolžnega,
12 tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol )
požrimo jih žive kakor grob in cele, kakor tiste, ki gredo dol v jamo. (Sheol )
13 Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
Našli bomo vse dragoceno imetje, svoje hiše bomo napolnili z ukradenim blagom.
14 Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
Svoj žreb vrzi med nas, vsi imejmo eno mošnjo.«
15 Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
Moj sin, ne hodi z njimi na pot, svoje stopalo zadrži pred njihovo stezo,
16 Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
kajti njihova stopala tečejo k zlu in hitijo, da prelijejo kri.
17 Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
Zagotovo je zaman razprostrta mreža v očeh katerekoli ptice.
18 Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
In oni prežijo v zasedi na svojo lastno kri, tajno se pritajijo za svoja lastna življenja.
19 Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
Takšne so poti vsakega, ki je pohlepen dobička, ki odvzema življenje svojim lastnikom.
20 Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
Modrost kliče zunaj, svoj glas izreka na ulicah,
21 ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
kliče na glavnem kraju vrveža, v odprtinah velikih vrat, v mestu izreka svoje besede, rekoč:
22 “Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
»Doklej boste, vi topi, ljubili topost? In se posmehljivci razveseljevali v svojem posmehovanju in bedaki sovražili spoznanje?
23 Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
Obrnite se na moj opomin. Glejte, na vas bom izlila svojega duha, razglašala vam bom svoje besede.
24 Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
Ker sem klicala, pa ste odklonili, iztegovala sem svojo roko, pa noben človek ni upošteval,
25 Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
temveč ste zaničevali vse moje svetovanje in niste hoteli mojega opomina,
26 Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
se bom tudi jaz smejala ob vaši katastrofi, zasmehovala bom, ko pride vaš strah,
27 Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
ko prihaja vaš strah kakor opustošenje in vaše uničenje kakor vrtinčast veter, ko nad vas prihajata tegoba in tesnoba.
28 “Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
Tedaj se bodo obračali name, toda ne bom jim odgovorila, iskali me bodo zgodaj, toda ne bodo me našli,
29 Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
ker so sovražili spoznanje in niso izbrali strahu Gospodovega.
30 popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
Ničesar niso hoteli od mojega nasveta. Prezirali so vsak moj opomin.
31 Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
Zato bodo jedli od sadu svoje lastne poti in napolnjeni bodo s svojimi lastnimi naklepi.
32 Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
Kajti odvračanje od preprostosti jih bo ubilo in uspevanje bedakov jih bo uničilo.
33 Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”
Toda kdorkoli me posluša, bo varno prebival in bo miren pred strahom zla.«