< Miyambo 1 >
1 Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
Paraboles de Salomon, fils de David et roi d’Israël,
2 Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
Utiles pour connaître la sagesse et la discipline,
3 kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
Pour comprendre les paroles de la prudence, pour recevoir l’instruction de la doctrine, la justice, et le jugement et l’équité,
4 Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
Afin que soit donnée aux tout petits la finesse, à l’adolescent la science et l’intelligence.
5 Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
Le sage, en écoutant, sera plus sage, et l’intelligent possédera les moyens de gouverner.
6 kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
Il découvrira le proverbe et l’interprétation, les paroles des sages et leurs énigmes.
7 Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
La crainte du Seigneur est le principe de la sagesse. La sagesse et la doctrine, les insensés les méprisent.
8 Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
Écoute, mon fils, la discipline de ton père, et ne rejette pas la loi de ta mère,
9 Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
Afin que soit ajouté un agrément à ta tête, et un collier à ton cou.
10 Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
Mon fils, si des pécheurs veulent l’attirer, n’y acquiesce pas.
11 Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
S’ils disent: Viens avec nous, dressons des embûches au sang, cachons des pièges à l’innocent qui ne l’a pas mérité;
12 tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol )
Comme l’enfer, engloutissons-le vivant et entier, comme celui qui descend dans la fosse. (Sheol )
13 Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
Nous trouverons toutes sortes de biens précieux: nous remplirons nos maisons de dépouilles.
14 Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
Mets ta part avec nous, qu’une seule bourse soit pour nous tous.
15 Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
Mon fils, ne marche pas avec eux, écarte ton pied de leurs sentiers.
16 Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
Car leurs pieds courent au mal, et ils se hâtent afin de verser le sang.
17 Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
Mais en vain l’on jette le filet devant les yeux des oiseaux.
18 Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
Eux aussi à leur propre sang dressent des embûches, et
19 Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
Ainsi sont les sentiers de tout avare, ils ravissent lame de tous ceux qui possèdent.
20 Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
La sagesse prêche dehors; dans les places publiques elle élève sa voix;
21 ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
À la tête des foules elle crie, aux portes de la ville elle profère ses paroles disant:
22 “Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
Jusques à quand, tout petits enfants, aimerez-vous l’enfance, et les insensés désireront-ils ce qui leur est pernicieux, et les imprudents haïront-ils la science?
23 Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
Convertissez-vous à mes remontrances: voici que je vous révélerai mon esprit, et que je vous ferai comprendre mes paroles.
24 Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
Parce que j’ai appelé, et que vous avez refusé de m’entendre; que j’ai tendu ma main, et qu’il n’y a eu personne qui m’ait regardé;
25 Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
Que vous avez méprisé tous mes conseils, et négligé mes réprimandes:
26 Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
Moi aussi, à votre mort, je rirai et je me moquerai, lorsque ce que vous craigniez vous sera arrivé.
27 Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
Lorsqu’une calamité arrivera tout d’un coup, et que la mort, comme une tempête, fondra violemment sur vous; quand, viendront sur vous la tribulation et l’angoisse:
28 “Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
Alors ils m’invoqueront, et je ne les exaucerai pas; dès le matin ils se lèveront, et ils ne me trouveront pas;
29 Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
Parce qu’ils ont haï la discipline, et qu’ils n’ont pas reçu la crainte du Seigneur,
30 popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
Qu’ils n’ont pas acquiescé à mes conseils, qu’ils ont déprécié toutes mes remontrances.
31 Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
Aussi ils mangeront les fruits de leurs voies, et ils seront rassasiés de leurs conseils.
32 Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
L’égarement des tout petits les tuera; et la prospérité des insensés les perdra.
33 Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”
Mais celui qui m’écoute reposera sans terreur et jouira de l’abondance, la crainte des maux ayant été enlevée.