< Miyambo 1 >
1 Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
Les Proverbes de Salomon, fils de David, et Roi d'Israël.
2 Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
Pour connaître la sagesse et l'instruction, pour entendre les discours d'intelligence;
3 kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
Pour recevoir une leçon de bon sens, de justice, de jugement et d'équité.
4 Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
Pour donner du discernement aux simples, et de la connaissance et de l'adresse aux jeunes gens.
5 Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
Le sage écoutera, et deviendra mieux appris, et l'homme intelligent acquerra de la prudence;
6 kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
Afin d'entendre les discours sentencieux, et ce qui est élégamment dit; les paroles des sages, et leurs énigmes.
7 Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
La crainte de l'Eternel est la principale science; [mais] les fous méprisent la sagesse et l'instruction.
8 Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
Mon fils, écoute l'instruction de ton père, et n'abandonne point l'enseignement de ta mère.
9 Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
Car ce seront des grâces enfilées ensemble autour de ta tête, et des colliers autour de ton cou.
10 Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
Mon fils, si les pécheurs te veulent attirer, ne t'y accorde point.
11 Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
S'ils disent: Viens avec nous, dressons des embûches pour tuer; épions secrètement l'innocent, quoiqu'il ne nous en ait point donné de sujet;
12 tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol )
Engloutissons-les tout vifs, comme le sépulcre; et tout entiers, comme ceux qui descendent en la fosse; (Sheol )
13 Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
Nous trouverons toute sorte de biens précieux, nous remplirons nos maisons de butin;
14 Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
Tu y auras ton lot parmi nous, il n'y aura qu'une bourse pour nous tous.
15 Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
Mon fils, ne te mets point en chemin avec eux; retire ton pied de leur sentier.
16 Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
Parce que leurs pieds courent au mal, et se hâtent pour répandre le sang.
17 Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
Car [comme] c'est sans sujet que le rets est étendu devant les yeux de tout ce qui a des ailes;
18 Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
Ainsi ceux-ci dressent des embûches contre le sang de ceux-là, et épient secrètement leurs vies.
19 Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
Tel est le train de tout homme convoiteux de gain [déshonnête], lequel enlèvera la vie de ceux qui y sont adonnés.
20 Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
La souveraine Sapience crie hautement au dehors, elle fait retentir sa voix dans les rues.
21 ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
Elle crie dans les carrefours, là où on fait le plus de bruit, aux entrées des portes, elle prononce ses paroles par la ville:
22 “Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
Sots, [dit-elle], jusques à quand aimerez-vous la sottise? Et jusqu'à quand les moqueurs prendront-ils plaisir à la moquerie, et les fous auront-ils en haine la science?
23 Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
Etant repris par moi, convertissez-vous; voici, je vous donnerai de mon Esprit en abondance, et je vous ferai connaître mes paroles.
24 Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
Parce que j'ai crié, et que vous avez refusé [d'ouïr]; parce que j'ai étendu ma main, et qu'il n'y a eu personne qui y prit garde;
25 Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
Et parce que vous avez rejeté tout mon conseil, et que vous n'avez point agréé que je vous reprisse;
26 Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
Aussi je me rirai de votre calamité, je me moquerai quand votre effroi surviendra.
27 Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
Quand votre effroi surviendra comme une ruine, et que votre calamité viendra comme un tourbillon; quand la détresse et l'angoisse viendront sur vous;
28 “Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
Alors on criera vers moi, mais je ne répondrai point; on me cherchera de grand matin, mais on ne me trouvera point.
29 Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
Parce qu'ils auront haï la science, et qu'ils n'auront point choisi la crainte de l'Eternel.
30 popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
Ils n'ont point aimé mon conseil; ils ont dédaigné toutes mes répréhensions.
31 Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
Qu'ils mangent donc le fruit de leur voie, et qu'ils se rassasient de leurs conseils.
32 Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
Car l'aise des sots les tue, et la prospérité des fous les perd.
33 Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”
Mais celui qui m'écoutera, habitera en sûreté, et sera à son aise sans être effrayé d'aucun mal.