< Miyambo 1 >
1 Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
Přísloví Šalomouna syna Davidova, krále Izraelského,
2 Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
Ku poznání moudrosti a cvičení, k vyrozumívání řečem rozumnosti,
3 kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
K dosažení vycvičení v opatrnosti, spravedlnosti, soudu a toho, což pravého jest,
4 Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
Aby dána byla hloupým důmyslnost, mládenečku umění a prozřetelnost.
5 Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
Když poslouchati bude moudrý, přibude mu umění, a rozumný bude vtipnější,
6 kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
K srozumění podobenství, a výmluvnosti řeči moudrých a pohádkám jejich.
7 Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
Bázeň Hospodinova jest počátek umění, moudrostí a cvičením pohrdají blázni.
8 Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
Poslouchej, synu můj, cvičení otce svého, a neopouštěj naučení matky své.
9 Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
Neboť to přidá příjemnosti hlavě tvé, a bude zlatým řetězem hrdlu tvému.
10 Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
Synu můj, jestliže by tě namlouvali hříšníci, nepřivoluj.
11 Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
Jestliže by řekli: Poď s námi, úklady čiňme krvi, skryjeme se proti nevinnému bez ostýchání se;
12 tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol )
Sehltíme je jako hrob za živa, a v cele jako ty, jenž sstupují do jámy; (Sheol )
13 Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
Všelijakého drahého zboží dosáhneme, naplníme domy své loupeží;
14 Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
Vrz los svůj mezi nás, měšec jeden budeme míti všickni:
15 Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
Synu můj, nevycházej na cestu s nimi, zdrž nohu svou od stezky jejich;
16 Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
Nebo nohy jejich ke zlému běží, a pospíchají k vylévání krve.
17 Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
Jistě, že jakož nadarmo roztažena bývá sít před očima jakéhokoli ptactva,
18 Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
Tak tito proti krvi své ukládají, skrývají se proti dušem svým.
19 Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
Takovéť jsou cesty každého dychtícího po zisku, duši pána svého uchvacuje.
20 Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
Moudrost vně volá, na ulicech vydává hlas svůj.
21 ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
V největším hluku volá, u vrat brány, v městě, a výmluvnosti své vypravuje, řka:
22 “Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
Až dokud hloupí milovati budete hloupost, a posměvači posměch sobě libovati, a blázni nenáviděti umění?
23 Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
Obraťtež se k domlouvání mému. Hle, vynáším vám ducha svého, a v známost vám uvodím slova svá.
24 Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
Poněvadž jsem volala, a odpírali jste; vztahovala jsem ruku svou, a nebyl, kdo by pozoroval,
25 Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
Anobrž strhli jste se všeliké rady mé, a trestání mého jste neoblíbili:
26 Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
Pročež i já v bídě vaší smáti se budu, posmívati se budu, když přijde to, čehož se bojíte,
27 Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
Když přijde jako hrozné zpuštění to, čehož se bojíte, a bída vaše jako bouře nastane, když přijde na vás trápení a ssoužení.
28 “Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
Tehdy volati budou ke mně, a nevyslyším; ráno hledati mne budou, a nenaleznou mne.
29 Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
Proto že nenáviděli umění, a bázně Hospodinovy nevyvolili,
30 popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
Aniž povolili radě mé, ale pohrdali všelikým domlouváním mým.
31 Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
Protož jísti budou ovoce skutků svých, a radami svými nasyceni budou.
32 Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
Nebo pokoj hloupých zmorduje je, a štěstí bláznů zahubí je.
33 Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”
Ale kdož mne poslouchá, bydliti bude bezpečně, pokoj maje před strachem zlých věcí.