< Afilipi 1 >
1 Paulo ndi Timoteyo, atumiki a Khristu Yesu. Kulembera anthu onse oyera mtima a ku Filipi amene ali mwa Khristu Yesu, pamodzi ndi oyangʼanira ndi atumiki awo.
PAUL and Timothy, servants of Jesus the Messiah, to all the saints that are in Jesus the Messiah at Philippi, with the elders and deacons.
2 Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale kwa inu.
Grace be with you, and peace from God our Father, and from our Lord Jesus the Messiah.
3 Ndimayamika Mulungu wanga nthawi zonse ndikakumbukira inu.
I thank my God at the constant recollection of you,
4 Mʼmapemphero anga onse opempherera inu, nthawi zonse ndimapemphera ndi chimwemwe
in all my prayers respecting you; and while I rejoice, I adore;
5 chifukwa mwakhala mukundithandiza polalikira Uthenga Wabwino kuyambira tsiku loyamba mpaka tsopano.
on account of your fellowship in the gospel, from the first day until now.
6 Sindikukayika konse kuti Iye amene anayamba ntchito yabwino mwa inu adzayipitiriza ndi kuyimaliza mpaka pa tsiku la kubweranso kwa Khristu Yesu.
Because I am confident of this, that he who hath begun the good works in you, will accomplish them until the day of our Lord Jesus the Messiah.
7 Kwa ine ndi bwino kuti ndiziganiza zotere za nonsenu, popeza ndimakukondani, ngakhale ndikhale mʼndende, kapena pamene ndikuteteza ndi kukhazikitsa Uthenga Wabwino, inu nonse mumagawana nane chisomo cha Mulungu.
For thus it is right for me to think of you all, because ye are permanently in my heart, and because, both in my bonds and in the vindication of the truth of the gospel, ye are my associates in grace.
8 Mulungu angandichitire umboni kuti ndimakulakalakani ndi chikondi cha Khristu Yesu.
For God is my witness, how I love you in the bowels of Jesus the Messiah.
9 Ndipo pemphero langa ndi lakuti chikondi chanu chipitirire kukulirakulira pa chidziwitso ndi kuzama mʼmaganizo,
And this I pray for, that your love may still increase and abound, in knowledge, and In all spiritual understanding:
10 kuti mukhoza kuzindikira chabwino koposa zonse ndi chiti kuti muthe kukhala wopanda chodetsa ndi wopanda chilema kufikira tsiku la Khristu.
so that ye may discern the things that are suitable; and may be pure and without offence, in the day of the Messiah,
11 Ndipo moyo wanu udzakhala odzazidwa ndi chipatso cha chilungamo chimene chimachokera mwa Yesu Khristu. Pakuti zimenezi zidzapereka ulemerero ndi matamando kwa Mulungu.
and be full of the fruits of righteousness which are by Jesus the Messiah, to the praise and glory of God.
12 Tsopano abale, ndikufuna mudziwe kuti chimene chandichitikira ine chathandiza kwambiri kupititsa patsogolo Uthenga Wabwino.
And I would that ye might know, my brethren, that the transaction in regard to me, hath eventuated rather for the furtherance of the gospel;
13 Chotsatira chake nʼchakuti zadziwika bwino lomwe kwa onse amene ali ku nyumba yaufumu kuti ine ndili mʼmaunyolo chifukwa cha Khristu.
so that my bonds, on account of the Messiah, are matter of notoriety in all the court, and to all others.
14 Moti chifukwa cha maunyolo angawa, abale ambiri alimbikitsidwa kuyankhula Mawu a Mulungu molimbika ndi mopanda mantha.
And many of the brethren in our Lord have become confident, on account of my bonds, and are more bold to speak the word of God without fear.
15 Nʼzoonadi kuti ena amalalikira Khristu chifukwa cha kaduka ndi mikangano, koma ena chifukwa cha zolinga zabwino.
And they herald it, some from envy and contention; but others with good will, and with love for the Messiah;
16 Olalikira ndi zolinga zabwinowa amachita izi mwachikondi, podziwa kuti ine ndili muno chifukwa cha kuteteza Uthenga Wabwino.
because they know that I am appointed for the vindication of the gospel.
17 Ena aja amalalikira Khristu modzikonda osati moona mtima namaganiza kuti kutero kubweretsa mavuto pamene ndili mʼmaunyolo.
And they who herald the Messiah in contention, do it not sincerely; but they hope to add pressure to my bonds.
18 Nanga kodi zimenezo zili ndi ntchito? Chofunika ndi chakuti Khristu alalikidwe, kaya ndi mwachinyengo kapena moona. Ndipo ndikukondwera chifukwa cha chimenechi. Ndithu, ndidzapitirira kukondwera,
And in this I have rejoiced, and do rejoice, that in every form, whether in pretence or in truth, the Messiah is heralded.
19 pakuti ndikudziwa kuti chifukwa cha mapemphero anu ndi thandizo lochokera kwa Mzimu wa Yesu Khristu, zimene zandionekera zidzathandiza kuti ndimasulidwe.
For I know, that these things will be found conducive to my life, through your prayers and the gift of the Spirit of Jesus the Messiah.
20 Ndili ndi chiyembekezo chonse kuti sindidzachita manyazi ndi pangʼono pomwe, koma ndidzakhala ndi chilimbikitso chokwanira kuti monga mwa nthawi zonse, tsopano Khristu adzakwezedwa mʼthupi langa kaya ndi mʼmoyo kapena mu imfa.
So that I hope and expect, that I shall in nothing be put to shame; but with uncovered face, as at all times, so now, the Messiah will be magnified in my body, whether by life or by death.
21 Pakuti kwa ine kukhala moyo ndi Khristu ndipo kufa ndi phindu.
For my life is, the Messiah; and if I die, it is gain to me.
22 Ngati nditi ndipitirire kukhala ndi moyo mʼthupi ndiye kuti kwa ine ndi kugwira ntchito yopindulitsa. Kodi ndisankhe chiyani? Sindikudziwa.
But if I have fruits of my labors in this life of the flesh, I know not what I shall choose.
23 Ndathinidwa ndi zinthu ziwirizi: Ndikulakalaka kunyamuka kuti ndikakhale ndi Khristu, chimene ndi chinthu chabwino kwambiri.
For the two press upon me: I desire to be liberated, that I may be with the Messiah; and this would be very advantageous to me.
24 Komanso nʼkofunika kwambiri kuti ndikhalebe mʼthupi chifukwa cha inu.
But also the business in regard to you, urges upon me to remain in the body.
25 Ndili ndi chitsimikizo, ndikudziwa kuti ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzapitirira nanu kuti nonse mupite mʼtsogolo ndi kukhala ndi chimwemwe mu chikhulupiriro
And this I confidently know, that I shall continue and remain, for your joy, and for the furtherance of your faith;
26 kuti pokhala nanunso, kudzitamandira kwanu mwa Khristu Yesu kudzasefukire chifukwa cha ine.
so that when I come again to you, your glorying, which is in Jesus the Messiah only, will abound through me.
27 Chilichonse chimene chingachitike, chachikulu nʼchakuti mukhale moyo ofanana ndi Uthenga Wabwino wa Khristu. Tsono ngati ndingabwere kudzakuonani kapena kumangomva za inu ndili kutali, ndidzadziwa kuti mwayima mwamphamvu mwa Mzimu mmodzi, kulimbika pamodzi ngati munthu mmodzi chifukwa cha chikhulupiriro cha Uthenga Wabwino
Let your conduct be as becometh the gospel of the Messiah; so that if I come I may see you, and if absent I may hear of you, that ye stand fast in one spirit and in one soul, and that ye strive together in the faith of the gospel.
28 osachita mantha ndi pangʼono pomwe ndi amene akutsutsana nanu. Ichi ndi chizindikiro kwa iwo kuti adzawonongedwa, koma inu mudzapulumutsidwa ndi Mulungu.
And in nothing be ye startled, by those who rise up against us; which is an indication of their destruction, and of life for you.
29 Pakuti inu mwapatsidwa mwayi osati ongokhulupirira Khristu kokha, koma wakumva zowawa mʼmalo mwa Khristu.
And this is given to you by God, that ye not only really believe in the Messiah, but also that ye suffer on his account;
30 Inunso mukudutsa mʼzowawa zomwe zija munaona ndikudutsamo inenso ndipo pano mukumva kuti ndikukumana nazobe.
and that ye endure conflict, as ye have seen in me, and now hear concerning me.