< Afilipi 1 >
1 Paulo ndi Timoteyo, atumiki a Khristu Yesu. Kulembera anthu onse oyera mtima a ku Filipi amene ali mwa Khristu Yesu, pamodzi ndi oyangʼanira ndi atumiki awo.
Milí křesťané ve Filipech, přijměte pozdrav ode mne i Timotea. Vám všem, vašim správcům a pomocníkům přejeme milost a pokoj od našeho nebeského Otce a od Ježíše Krista, našeho Pána.
2 Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale kwa inu.
3 Ndimayamika Mulungu wanga nthawi zonse ndikakumbukira inu.
Kdykoliv si na vás vzpomenu, děkuji za vás všechny Bohu, že od chvíle, kdy jste poprvé slyšeli radostné poselství o Kristu, nepřestali jste mi pomáhat v jeho šíření. Za to jsem velmi vděčen.
4 Mʼmapemphero anga onse opempherera inu, nthawi zonse ndimapemphera ndi chimwemwe
5 chifukwa mwakhala mukundithandiza polalikira Uthenga Wabwino kuyambira tsiku loyamba mpaka tsopano.
6 Sindikukayika konse kuti Iye amene anayamba ntchito yabwino mwa inu adzayipitiriza ndi kuyimaliza mpaka pa tsiku la kubweranso kwa Khristu Yesu.
Nepochybuji, že když Bůh své dobré dílo u vás započal, dovede je až k slavnému konci v den Kristova návratu.
7 Kwa ine ndi bwino kuti ndiziganiza zotere za nonsenu, popeza ndimakukondani, ngakhale ndikhale mʼndende, kapena pamene ndikuteteza ndi kukhazikitsa Uthenga Wabwino, inu nonse mumagawana nane chisomo cha Mulungu.
Nemohu o vás smýšlet jinak; stali jste se mi zvlášť blízkými svou vnitřní účastí na všem, co jsem prožíval, ať už to bylo ve vězení nebo na svobodě, při obhajování pravdy o Kristu.
8 Mulungu angandichitire umboni kuti ndimakulakalakani ndi chikondi cha Khristu Yesu.
Bůh ví, jak po vás všech toužím. Láska, kterou mne naplňuje Ježíš, mne táhne k vám.
9 Ndipo pemphero langa ndi lakuti chikondi chanu chipitirire kukulirakulira pa chidziwitso ndi kuzama mʼmaganizo,
Prosím Boha, aby vás obdaroval poznáním a moudrostí a zdokonalil vás v lásce,
10 kuti mukhoza kuzindikira chabwino koposa zonse ndi chiti kuti muthe kukhala wopanda chodetsa ndi wopanda chilema kufikira tsiku la Khristu.
abyste vždy správně rozlišovali dobré od zlého a neposkvrnili se ničím špatným až do příchodu Ježíšova.
11 Ndipo moyo wanu udzakhala odzazidwa ndi chipatso cha chilungamo chimene chimachokera mwa Yesu Khristu. Pakuti zimenezi zidzapereka ulemerero ndi matamando kwa Mulungu.
Každý váš skutek ať svědčí o Kristově moci ve vás a oslavuje tak Boha.
12 Tsopano abale, ndikufuna mudziwe kuti chimene chandichitikira ine chathandiza kwambiri kupititsa patsogolo Uthenga Wabwino.
Chci vám sdělit, bratři, že moje uvěznění se stalo vynikající reklamou pro Kristovu věc.
13 Chotsatira chake nʼchakuti zadziwika bwino lomwe kwa onse amene ali ku nyumba yaufumu kuti ine ndili mʼmaunyolo chifukwa cha Khristu.
I ten poslední písař u soudu totiž ví, že mým jediným proviněním je má víra v Krista,
14 Moti chifukwa cha maunyolo angawa, abale ambiri alimbikitsidwa kuyankhula Mawu a Mulungu molimbika ndi mopanda mantha.
a zdá se, že ostatním bratřím to pomohlo zbavit se strachu, takže teď o Kristu hovoří daleko otevřeněji než dříve.
15 Nʼzoonadi kuti ena amalalikira Khristu chifukwa cha kaduka ndi mikangano, koma ena chifukwa cha zolinga zabwino.
Je sice pravda, že někteří to dělají jen ze závisti a ctižádosti, aby také získali pověst neohrožených kazatelů, a myslí si, že jim tady ve vězení budu závidět jejich úspěchy.
16 Olalikira ndi zolinga zabwinowa amachita izi mwachikondi, podziwa kuti ine ndili muno chifukwa cha kuteteza Uthenga Wabwino.
Ale jiní mluví o Kristu z lásky k němu a ve mně vidí obhájce jeho učení.
17 Ena aja amalalikira Khristu modzikonda osati moona mtima namaganiza kuti kutero kubweretsa mavuto pamene ndili mʼmaunyolo.
Ať však už rozhlašují Krista z pohnutek čistých nebo s postranními úmysly, jen když je hlásána zvěst o Kristu. Z toho se mohu vždy jen radovat.
18 Nanga kodi zimenezo zili ndi ntchito? Chofunika ndi chakuti Khristu alalikidwe, kaya ndi mwachinyengo kapena moona. Ndipo ndikukondwera chifukwa cha chimenechi. Ndithu, ndidzapitirira kukondwera,
Vím, že soudní přelíčení tak či onak povede k dobrému. To mi zaručují vaše modlitby i Duch svatý, který stojí při mně.
19 pakuti ndikudziwa kuti chifukwa cha mapemphero anu ndi thandizo lochokera kwa Mzimu wa Yesu Khristu, zimene zandionekera zidzathandiza kuti ndimasulidwe.
Proto doufám a těším se na to, že budu moci mluvit stejně směle, jak jsem to dělal dosud, a že z této pře vyjde Kristus vítězně, ať už sám vyváznu se zdravou kůží či nikoliv.
20 Ndili ndi chiyembekezo chonse kuti sindidzachita manyazi ndi pangʼono pomwe, koma ndidzakhala ndi chilimbikitso chokwanira kuti monga mwa nthawi zonse, tsopano Khristu adzakwezedwa mʼthupi langa kaya ndi mʼmoyo kapena mu imfa.
21 Pakuti kwa ine kukhala moyo ndi Khristu ndipo kufa ndi phindu.
Vždyť mým životem je Kristus, a proto i smrt mi bude ziskem.
22 Ngati nditi ndipitirire kukhala ndi moyo mʼthupi ndiye kuti kwa ine ndi kugwira ntchito yopindulitsa. Kodi ndisankhe chiyani? Sindikudziwa.
Zůstanu-li ovšem na živu, mohl bych ještě být užitečný lidem.
23 Ndathinidwa ndi zinthu ziwirizi: Ndikulakalaka kunyamuka kuti ndikakhale ndi Khristu, chimene ndi chinthu chabwino kwambiri.
Takže kdybych měl možnost volit, sám nevím, čemu bych dal přednost: zemřít a být s Kristem (to by mě přitahovalo nejvíc),
24 Komanso nʼkofunika kwambiri kuti ndikhalebe mʼthupi chifukwa cha inu.
anebo žít dál kvůli vám, což by bylo zase potřebnější.
25 Ndili ndi chitsimikizo, ndikudziwa kuti ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzapitirira nanu kuti nonse mupite mʼtsogolo ndi kukhala ndi chimwemwe mu chikhulupiriro
Ale nějak cítím, že mne ještě mezi vámi čeká práce, a tak se kloním k přesvědčení, že tentokrát tu ještě zůstanu,
26 kuti pokhala nanunso, kudzitamandira kwanu mwa Khristu Yesu kudzasefukire chifukwa cha ine.
abyste rostli v radostné víře a měli v mém vysvobození další důvod k oslavě Krista.
27 Chilichonse chimene chingachitike, chachikulu nʼchakuti mukhale moyo ofanana ndi Uthenga Wabwino wa Khristu. Tsono ngati ndingabwere kudzakuonani kapena kumangomva za inu ndili kutali, ndidzadziwa kuti mwayima mwamphamvu mwa Mzimu mmodzi, kulimbika pamodzi ngati munthu mmodzi chifukwa cha chikhulupiriro cha Uthenga Wabwino
Bez ohledu na můj příští osud myslete však na to, abyste žili tak, jak se sluší na Kristovy vyznavače. A ať už vás budu moci navštívit nebo o vás jen uslyším, chci se dovídat, že držíte pevně pohromadě, spojeni úsilím o šíření Kristova poselství
28 osachita mantha ndi pangʼono pomwe ndi amene akutsutsana nanu. Ichi ndi chizindikiro kwa iwo kuti adzawonongedwa, koma inu mudzapulumutsidwa ndi Mulungu.
přes všechny zuřivé útoky nepřítele. Ten v tom bude vidět předzvěst své záhuby, ale pro vás je to důkaz, že Bůh je s vámi a že vám dal věčný život.
29 Pakuti inu mwapatsidwa mwayi osati ongokhulupirira Khristu kokha, koma wakumva zowawa mʼmalo mwa Khristu.
Vždyť vám bylo dopřáno nejen v Krista uvěřit,
30 Inunso mukudutsa mʼzowawa zomwe zija munaona ndikudutsamo inenso ndipo pano mukumva kuti ndikukumana nazobe.
ale také pro něho trpět ve stejném boji, jaký vedu já.