< Afilipi 1 >

1 Paulo ndi Timoteyo, atumiki a Khristu Yesu. Kulembera anthu onse oyera mtima a ku Filipi amene ali mwa Khristu Yesu, pamodzi ndi oyangʼanira ndi atumiki awo.
Krstos Iyesus guuts wottsuwots P'awlosnat T'imitiyosoke, Flp'isyos kitotse beyiru Krstos Iyesusn S'ayn wotts jamwotssh, Ik' maa eenashwotsnat diyak'oniyotsnsh.
2 Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale kwa inu.
Nonih Ik'oknat no doonzo Krstos Iyesusoki s'aatonat jeenon itsh wotowe.
3 Ndimayamika Mulungu wanga nthawi zonse ndikakumbukira inu.
Iti tgawi taawo jam aawo Izar Izeweri udirwe,
4 Mʼmapemphero anga onse opempherera inu, nthawi zonse ndimapemphera ndi chimwemwe
It jamets jangoshowere Ik'o tk'oni taawu jamo Ik' tk'ono gene'on s'eenke.
5 chifukwa mwakhala mukundithandiza polalikira Uthenga Wabwino kuyambira tsiku loyamba mpaka tsopano.
Shints aawortson dek't b́tutson andish b́borfetsosh dooshishiyo nabfetsr t fino tep'iruwotsi it wottsotse Ik'o udiruwe,
6 Sindikukayika konse kuti Iye amene anayamba ntchito yabwino mwa inu adzayipitiriza ndi kuyimaliza mpaka pa tsiku la kubweranso kwa Khristu Yesu.
Fini sheengo ititse dek't tuutso Izar Izewer, Krstos Iyesus angshosh aanar b́ weet aawots s'uwomaants b́betsituwok'osh arikon danfee.
7 Kwa ine ndi bwino kuti ndiziganiza zotere za nonsenu, popeza ndimakukondani, ngakhale ndikhale mʼndende, kapena pamene ndikuteteza ndi kukhazikitsa Uthenga Wabwino, inu nonse mumagawana nane chisomo cha Mulungu.
And tipimootse tbeyanoronat ttpeftsere shin doo shishi fini aroosh mooyr bínowere kup'iyosh Ik'o b́ s'aaton b́imts gowosh it únetswor biyatse kayituwotsi it wottsotse it jam aawo t nibots itne. Manshowere it jangosh taash shiyeyiruwo arikee.
8 Mulungu angandichitire umboni kuti ndimakulakalakani ndi chikondi cha Khristu Yesu.
Krstos Iyesus shunon it únetsnoor awuk'o tgawiruwok'owosh tgawo Ik'oniye.
9 Ndipo pemphero langa ndi lakuti chikondi chanu chipitirire kukulirakulira pa chidziwitso ndi kuzama mʼmaganizo,
It shuno danonat t'iwintson s'eenk wotarr eenfere bíametwok'o Ik'o k'oniruwe.
10 kuti mukhoza kuzindikira chabwino koposa zonse ndi chiti kuti muthe kukhala wopanda chodetsa ndi wopanda chilema kufikira tsiku la Khristu.
Manuwere k'ants keewo p'ec'ar danr Krstos aanar b́weet aawots s'ayinwotsnat eeg eego boatse daatserawuwotsi wotarr it datsetuwok'oye.
11 Ndipo moyo wanu udzakhala odzazidwa ndi chipatso cha chilungamo chimene chimachokera mwa Yesu Khristu. Pakuti zimenezi zidzapereka ulemerero ndi matamando kwa Mulungu.
Mank'oon it beyon Iyesus Krstosoke daatset kaawi shuwon s'eentso wotaarr Ik'osh mangonat udon datsiyituwotsi wotitute.
12 Tsopano abale, ndikufuna mudziwe kuti chimene chandichitikira ine chathandiza kwambiri kupititsa patsogolo Uthenga Wabwino.
Tieshuwotso! tiats bodts keewu jamo dooshishiyo iki b́gawnetwok'o b́wooshtsok'o danitdek'o shunfee.
13 Chotsatira chake nʼchakuti zadziwika bwino lomwe kwa onse amene ali ku nyumba yaufumu kuti ine ndili mʼmaunyolo chifukwa cha Khristu.
Taa ttipe Krstos jangosh b́wottsok'owo Ron datsi nugúsi maa kotiruwotsnat manoke fa'a ash jametswots danfnee.
14 Moti chifukwa cha maunyolo angawa, abale ambiri alimbikitsidwa kuyankhula Mawu a Mulungu molimbika ndi mopanda mantha.
Taa ttipetsatse tuutson amants eshu eshwotsitse ayuwots iki bogshdek't doonozo amantsuwotsi woternee, mansh Ik'o aap'tso shatalon shishiyosh shintsoniyere iki bogts ááwu shuuk'o daatsrne.
15 Nʼzoonadi kuti ena amalalikira Khristu chifukwa cha kaduka ndi mikangano, koma ena chifukwa cha zolinga zabwino.
Wotówa eré ik ikuwots Krstosi bo nabír okooronat nokoreyi shayirone, k'oshuwotsmó Krstosi bo nabir níb s'aayinone.
16 Olalikira ndi zolinga zabwinowa amachita izi mwachikondi, podziwa kuti ine ndili muno chifukwa cha kuteteza Uthenga Wabwino.
Hanots Krstosi bo nabir bo took shunatse tuutsone, boowere taa doo shishiyosh tdetsts mooshatse tuutson hanoke juwetso twottsok'o bodantsoshe.
17 Ena aja amalalikira Khristu modzikonda osati moona mtima namaganiza kuti kutero kubweretsa mavuto pamene ndili mʼmaunyolo.
Ekewotsmó Krstos jango k'uuridek't nabiruwots maac' s'ayinon b́woterawon botook shunonat ttipeyatse iki bogts kic'o tiats doosh gawttiniye.
18 Nanga kodi zimenezo zili ndi ntchito? Chofunika ndi chakuti Khristu alalikidwe, kaya ndi mwachinyengo kapena moona. Ndipo ndikukondwera chifukwa cha chimenechi. Ndithu, ndidzapitirira kukondwera,
Han wotowa ekeewi wotowa taa geneeúwe tgeeneúwiti, ariyon wotowa arikon wotowa jam werindon Krstosi nabetuwe.
19 pakuti ndikudziwa kuti chifukwa cha mapemphero anu ndi thandizo lochokera kwa Mzimu wa Yesu Khristu, zimene zandionekera zidzathandiza kuti ndimasulidwe.
K'osho taan gene'úshiruwo it Ik'o itk'onirwonat Iyesus Krstos shayiri tep'oon s'ayinr tkeshetwok'o tdantsotsne.
20 Ndili ndi chiyembekezo chonse kuti sindidzachita manyazi ndi pangʼono pomwe, koma ndidzakhala ndi chilimbikitso chokwanira kuti monga mwa nthawi zonse, tsopano Khristu adzakwezedwa mʼthupi langa kaya ndi mʼmoyo kapena mu imfa.
B́ jamon tjitserawok'o jangatniye tkotiri, ernmó úni aawo tk'aliruwok'onat hambets kashon t beyal wee t k'iriyal Krstos tiatsotse mangituwe etaat ááwushuk'on keewiruwe.
21 Pakuti kwa ine kukhala moyo ndi Khristu ndipo kufa ndi phindu.
Mansha taash beya eto Krstosn beewoniye, k'ira etoonwere oot'o biitse daatset keewe.
22 Ngati nditi ndipitirire kukhala ndi moyo mʼthupi ndiye kuti kwa ine ndi kugwira ntchito yopindulitsa. Kodi ndisankhe chiyani? Sindikudziwa.
Ernmó t atsi metsanaton dabr t beyetka wotink'e shuu daatsitfino finere etee, b́wotiyaloru dabr beyonat k'irotse ááwi galtdek'etwok'owo danatse.
23 Ndathinidwa ndi zinthu ziwirizi: Ndikulakalaka kunyamuka kuti ndikakhale ndi Khristu, chimene ndi chinthu chabwino kwambiri.
Git hasabiyanots dagots detsewtsere, hank'o beyanitse k'aleyar Krstosnton woto geefe, manuwere Krstosnton beyo taash ayidek't k'ank b́wottsotsne.
24 Komanso nʼkofunika kwambiri kuti ndikhalebe mʼthupi chifukwa cha inu.
K'osh weeron kashon t beyo itsh ayidek't geyike.
25 Ndili ndi chitsimikizo, ndikudziwa kuti ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzapitirira nanu kuti nonse mupite mʼtsogolo ndi kukhala ndi chimwemwe mu chikhulupiriro
Mansh arikeewetsk taane, taa k'irraniye oorar it imnetiyo eenr bíere imnetiyon geneúo it daatsish it jametsnton t teshetwok'o danfee.
26 kuti pokhala nanunso, kudzitamandira kwanu mwa Khristu Yesu kudzasefukire chifukwa cha ine.
Taa aani itok twoor t jangosh it detsts it'o Iyesus Krstosn ayituwe.
27 Chilichonse chimene chingachitike, chachikulu nʼchakuti mukhale moyo ofanana ndi Uthenga Wabwino wa Khristu. Tsono ngati ndingabwere kudzakuonani kapena kumangomva za inu ndili kutali, ndidzadziwa kuti mwayima mwamphamvu mwa Mzimu mmodzi, kulimbika pamodzi ngati munthu mmodzi chifukwa cha chikhulupiriro cha Uthenga Wabwino
Eshe jamoniyere bogo it beyotse Krstos doo shishiyo bíetirwok'on beewere, hanuwere taa wáár itn t s'ilalo wee itoke twokiyal ik níbon kup'at it ned'tsonat doo shishiyo ik wotat betsosh it kaartsok'o shishirwe.
28 osachita mantha ndi pangʼono pomwe ndi amene akutsutsana nanu. Ichi ndi chizindikiro kwa iwo kuti adzawonongedwa, koma inu mudzapulumutsidwa ndi Mulungu.
Itn k'efiruwotsi ik keewonoru shatk'ayere, it ááwu shuk'anwere boosh bot'afit milkt b́ wottsotse itshomó Ik'oke wotts it kashtsi milkte.
29 Pakuti inu mwapatsidwa mwayi osati ongokhulupirira Khristu kokha, koma wakumva zowawa mʼmalo mwa Khristu.
Krstosi aman mec'rosh b́ woterawo b́ jangoshowere gond bek'o it datsitwok'owe.
30 Inunso mukudutsa mʼzowawa zomwe zija munaona ndikudutsamo inenso ndipo pano mukumva kuti ndikukumana nazobe.
Eshe and itats bodiru gondbek'aan bali tiyats bodt teshtsoniye, andoor tiyats b́bodiru gond bek'o itshishirwoniye.

< Afilipi 1 >