< Afilipi 4 >
1 Tsono abale anga, ndimakukondani ndipo ndikukulakalakani. Ndinu chimwemwe changa ndi chipewa cha ulemerero wanga. Abwenzi okondedwa, chilimikani choncho mwa Ambuye.
Therefore, my brethren dearly beloved and longed for, my joy and crown, so stand fast in the Lord, my dearly beloved.
2 Ndikudandaulira Euodiya ndi Suntuke kuti akhale ndi mtima umodzi mwa Ambuye.
I beseech Euodias, and beseech Syntyche, that they be of the same mind in the Lord.
3 Inde, ndikupempha iwe mnzanga pa ntchitoyi, thandiza amayiwa amene ndagwira nawo ntchito ya Uthenga Wabwino pamodzi ndi Klementonso ndi ena onse antchito anzanga amene mayina awo ali mʼbuku lamoyo.
And I entreat thee also, true yokefellow, help those women who laboured with me in the gospel, with Clement also, and with other my fellowlabourers, whose names are in the book of life.
4 Nthawi zonse muzikondwa mwa Ambuye. Ndikubwerezanso; muzikondwa!
Rejoice in the Lord always: and again I say, Rejoice.
5 Kufatsa kwanu kuzioneka pamaso pa anthu onse. Ambuye anu ali pafupi.
Let your moderation be known to all men. The Lord is at hand.
6 Musade nkhawa ndi kanthu kalikonse, koma pa china chilichonse, mwa pemphero ndi chidandaulo pamodzi ndi chiyamiko, perekani zopempha zanu kwa Mulungu.
Be anxious for nothing; but in every thing by prayer and supplication with thanksgiving let your requests be made known to God.
7 Ndipo mtendere wa Mulungu, umene upambana nzeru zonse udzasunga bwino mitima yanu ndi maganizo anu mwa Khristu Yesu.
And the peace of God, which passeth all understanding, shall keep your hearts and minds through Christ Jesus.
8 Potsiriza, abale, muziyika mtima wanu pa zinthu zilizonse zabwino ndi zotamandika monga, zinthu zoona, zinthu zolemekezeka, zinthu zolungama, zinthu zoyera, zinthu zokongola ndi zinthu zosiririka.
Finally, brethren, whatever things are true, whatever things are honest, whatever things are just, whatever things are pure, whatever things are lovely, whatever things are of good report; if there is any virtue, and if there is any praise, think on these things.
9 Muzichita chilichonse chimene mwaphunzira kapena kulandira kapena kumva kuchokera kwa ine kapena mwaona mwa ine. Ndipo Mulungu wamtendere adzakhala nanu.
Those things, which ye have both learned, and received, and heard, and seen in me, do: and the God of peace shall be with you.
10 Ndikukondwa kwambiri mwa Ambuye kuti patapita nthawi tsopano mwayambanso kuonetsa kuti mumandiganizira. Zoonadi, mwakhala mukundikumbukira, koma munalibe mpata woti muonetsere zimenezi.
But I rejoiced in the Lord greatly, that now at the last your care of me hath flourished again; in which ye were also concerned, but ye lacked opportunity.
11 Sindikunena izi chifukwa choti ndikusowa thandizo, poti ine ndaphunzira kukhala wokwaniritsidwa ndi zimene ndili nazo.
Not that I speak in respect of want: for I have learned, in whatever state I am, with that to be content.
12 Ndimadziwa kusauka nʼkutani, ndipo ndimadziwa kulemera nʼkutani. Ndaphunzira chinsinsi chokhala wokhutitsidwa mwa njira ina iliyonse, kaya nʼkudya bwino kapena kukhala ndi njala, kaya kukhala ndi chuma kapena umphawi.
I know both how to be abased, and I know how to abound: every where and in all things I am instructed both to be full and to be hungry, both to abound and to suffer need.
13 Ndikhoza kuchita zonse kudzera mwa Iye amene amandipatsa mphamvu.
I can do all things through Christ who strengtheneth me.
14 Komatu munachita bwino kundithandiza mʼmavuto anga.
However ye have done well, that ye did share with my affliction.
15 Ndipo inu Afilipi mukudziwa kuti masiku oyambirira olalikira Uthenga Wabwino, nditachoka ku Makedoniya, panalibe mpingo ndi umodzi omwe umene unagwirizana nane pa nkhani yopereka ndi kulandira, kupatula inu.
Now ye Philippians know also, that in the beginning of the gospel, when I departed from Macedonia, no church shared with me as concerning giving and receiving, but ye only.
16 Pakuti ngakhale pamene ndinali ku Tesalonika, munanditumizira kangapo zondithandiza pa zosowa zanga.
For even in Thessalonica ye sent once and again to my necessity.
17 Osati ndikufuna mphatso zanu, koma ndikufuna kuti pa zimene muli nazo pawonjezerekepo phindu.
Not because I desire a gift: but I desire fruit that may abound to your account.
18 Ndalandira zonse ndipo ndili nazo zokwanira zoposa zosowa zanga popeza ndalandira kwa Epafrodito mphatso zochuluka zimene munatumiza. Ndizo zopereka za fungo labwino, nsembe zolandiridwa zokondweretsa Mulungu.
But I have all, and abound: I am full, having received from Epaphroditus the things which were sent from you, an odour of a sweet smell, a sacrifice acceptable, wellpleasing to God.
19 Ndipo Mulungu wanga adzakwaniritsa zosowa zanu monga mwa chuma chake chaulemerero mwa Khristu Yesu.
But my God shall supply all your need according to his riches in glory by Christ Jesus.
20 Kwa Mulungu ndi Atate athu, kukhale ulemerero mpaka muyaya. Ameni. (aiōn )
Now to God and our Father be glory for ever and ever. Amen. (aiōn )
21 Perekani moni kwa oyera mtima onse mwa Khristu Yesu. Abale amene ali ndi ine akupereka moni wawo.
Greet every saint in Christ Jesus. The brethren who are with me greet you.
22 Oyera mtima onse akupereka moni, makamaka iwo a ku nyumba ya Kaisara.
All the saints greet you, chiefly they that are of Caesar’s household.
23 Chisomo cha Ambuye Yesu Khristu chikhale ndi mzimu wanu. Ameni.
The grace of our Lord Jesus Christ be with you all. Amen. To the Philippians written from Rome, by Epaphroditus.