< Afilipi 4 >

1 Tsono abale anga, ndimakukondani ndipo ndikukulakalakani. Ndinu chimwemwe changa ndi chipewa cha ulemerero wanga. Abwenzi okondedwa, chilimikani choncho mwa Ambuye.
Stůjte proto pevně ve spojení s Pánem, moji drazí bratři! Tak velmi po vás toužím, vždyť jste moje radost a má odměna.
2 Ndikudandaulira Euodiya ndi Suntuke kuti akhale ndi mtima umodzi mwa Ambuye.
Euodie a Syntyché, moc vás prosím, smiřte se zase a nehádejte se, jste přece křesťanky!
3 Inde, ndikupempha iwe mnzanga pa ntchitoyi, thandiza amayiwa amene ndagwira nawo ntchito ya Uthenga Wabwino pamodzi ndi Klementonso ndi ena onse antchito anzanga amene mayina awo ali mʼbuku lamoyo.
Syzygu, tebe prosím, pomoz jim v tom! Vždyť obě byly mými platnými pomocnicemi při šíření Kristova poselství, spolu s Klementem i ostatními, které Pán zapsal do Knihy života.
4 Nthawi zonse muzikondwa mwa Ambuye. Ndikubwerezanso; muzikondwa!
Radujte se a důvěřujte Pánu, radujte se zas a znovu.
5 Kufatsa kwanu kuzioneka pamaso pa anthu onse. Ambuye anu ali pafupi.
Ke všem buďte shovívaví a laskaví! Myslete na brzký Kristův návrat!
6 Musade nkhawa ndi kanthu kalikonse, koma pa china chilichonse, mwa pemphero ndi chidandaulo pamodzi ndi chiyamiko, perekani zopempha zanu kwa Mulungu.
Ničím se příliš netrapte, všechno svěřte v modlitbě Bohu: své prosby i díky za jejich vyslyšení.
7 Ndipo mtendere wa Mulungu, umene upambana nzeru zonse udzasunga bwino mitima yanu ndi maganizo anu mwa Khristu Yesu.
Uvidíte, že vás Bůh naplní klidem, jaký si nedovedete ani představit. Stačí jen důvěřovat Ježíši Kristu.
8 Potsiriza, abale, muziyika mtima wanu pa zinthu zilizonse zabwino ndi zotamandika monga, zinthu zoona, zinthu zolemekezeka, zinthu zolungama, zinthu zoyera, zinthu zokongola ndi zinthu zosiririka.
Než skončím, bratři, rád bych vám položil na srdce ještě jedno: podporujte všechno, co je pravdivé, dobré a správné, čisté, milé a chvályhodné, co má dobrou pověst a pokládá se za ctnost.
9 Muzichita chilichonse chimene mwaphunzira kapena kulandira kapena kumva kuchokera kwa ine kapena mwaona mwa ine. Ndipo Mulungu wamtendere adzakhala nanu.
Žijte tak, jak jsem vás učil a jak jste u mne slyšeli i viděli. A Bůh, dárce pokoje, bude s vámi.
10 Ndikukondwa kwambiri mwa Ambuye kuti patapita nthawi tsopano mwayambanso kuonetsa kuti mumandiganizira. Zoonadi, mwakhala mukundikumbukira, koma munalibe mpata woti muonetsere zimenezi.
Udělali jste mi, bratři, velikou radost a jsem za to Pánu vděčný, že jste mysleli na moje potřeby. Vím, že vám na mně záleželo i dřív, ale chyběla vám příležitost.
11 Sindikunena izi chifukwa choti ndikusowa thandizo, poti ine ndaphunzira kukhala wokwaniritsidwa ndi zimene ndili nazo.
Nestěžuji si na nedostatek, naučil jsem se být spokojen s tím, co právě mám.
12 Ndimadziwa kusauka nʼkutani, ndipo ndimadziwa kulemera nʼkutani. Ndaphunzira chinsinsi chokhala wokhutitsidwa mwa njira ina iliyonse, kaya nʼkudya bwino kapena kukhala ndi njala, kaya kukhala ndi chuma kapena umphawi.
Umím žít v odříkání i blahobytu, když se stůl prohýbá i když nemám co do úst.
13 Ndikhoza kuchita zonse kudzera mwa Iye amene amandipatsa mphamvu.
Ke všemu mám sílu, Kristus mi ji dává.
14 Komatu munachita bwino kundithandiza mʼmavuto anga.
Ale od vás je hezké, že jste mi pomohli svým darem.
15 Ndipo inu Afilipi mukudziwa kuti masiku oyambirira olalikira Uthenga Wabwino, nditachoka ku Makedoniya, panalibe mpingo ndi umodzi omwe umene unagwirizana nane pa nkhani yopereka ndi kulandira, kupatula inu.
Nemusím vám jistě připomínat, že ani tenkrát, když jsem se poprvé vypravoval z Makedonie hlásat Krista, byli jste jediní, kdo mi přispěli na mou cestu.
16 Pakuti ngakhale pamene ndinali ku Tesalonika, munanditumizira kangapo zondithandiza pa zosowa zanga.
Dokonce i do Tesaloniky jste mi dvakrát poslali, co jsem potřeboval.
17 Osati ndikufuna mphatso zanu, koma ndikufuna kuti pa zimene muli nazo pawonjezerekepo phindu.
Vašeho daru si vážím, ale ještě víc mne těší vědomí, jak každou takovou obětí se zvětšuje váš vklad u Boha.
18 Ndalandira zonse ndipo ndili nazo zokwanira zoposa zosowa zanga popeza ndalandira kwa Epafrodito mphatso zochuluka zimene munatumiza. Ndizo zopereka za fungo labwino, nsembe zolandiridwa zokondweretsa Mulungu.
Všechno jsem tedy v pořádku dostal a nic mi teď nechybí, když Epafroditus doručil vaši zásilku. Věřte, že tato vaše oběť je Bohu stejně milá jako mně.
19 Ndipo Mulungu wanga adzakwaniritsa zosowa zanu monga mwa chuma chake chaulemerero mwa Khristu Yesu.
Proto dá i vám, kteří patříte Ježíši Kristu, ze svého nevyčerpatelného bohatství všechno, co potřebujete.
20 Kwa Mulungu ndi Atate athu, kukhale ulemerero mpaka muyaya. Ameni. (aiōn g165)
Jemu, našemu Otci, sláva na věky! (aiōn g165)
21 Perekani moni kwa oyera mtima onse mwa Khristu Yesu. Abale amene ali ndi ine akupereka moni wawo.
P. S. Pozdravujte ode mne všechny křesťany u vás. Taky od těch, kteří tu bydlí se mnou, vás mám pozdravovat.
22 Oyera mtima onse akupereka moni, makamaka iwo a ku nyumba ya Kaisara.
I ostatní zdejší křesťané, zvlášť ti, co slouží v císařském paláci, vzkazují pozdrav.
23 Chisomo cha Ambuye Yesu Khristu chikhale ndi mzimu wanu. Ameni.
Přejeme vám všem milost Ježíše Krista, našeho Pána.

< Afilipi 4 >