< Afilipi 2 >
1 Ngati muli ndi chilimbikitso chilichonse chifukwa cholumikizana ndi Khristu, ngati muli ndi chitonthozo chifukwa cha chikondi chake, ngati muli ndi mtima umodzi mwa Mzimu, ndipo ngati mumakomerana mtima ndi kuchitirana chifundo,
Če obstaja torej kakršnakoli tolažba v Kristusu, če kakršnakoli tolažba ljubezni, če kakršnakoli družba Duha, če kakršnakoli čustva in usmiljenja,
2 tsono tsirizani chimwemwe changa pokhala amaganizo ofanana, achikondi chimodzimodzi, amodzi mu mzimu ndi acholinga chimodzinso.
izpolnite moje veselje, da ste istih misli in imate isto ljubezen, da ste soglasni, enega mišljenja.
3 Musachite kalikonse ndi mtima odzikonda chabe kapena odzitukumula chabe. Koma khalani odzichepetsa ndipo aliyense aziona mnzake ngati womuposa iyeyo.
Naj se nič ne stori zaradi prepira ali ošabnosti, temveč naj vsak v skromnosti mišljenja bolj upošteva drugega kakor sebe.
4 Musamangofuna zokomera inu nokha koma aliyense azifuna zokomeranso ena.
Ne glejte vsakdo na svoje stvari, temveč vsakdo tudi na stvari drugih.
5 Pa ubale wanu wina ndi mnzake, mukhale ndi mtima wofanana ndi wa Khristu Yesu:
V vas naj bo to mišljenje, ki je bilo tudi v Kristusu Jezusu,
6 Iyeyu, pokhala Mulungu ndithu, sanatenge kufanana ndi Mulungu kukhala chinthu choyenera kuchigwiritsa.
ki je, četudi v Božji podobi, mislil, da ni rop, da bi bil enak z Bogom;
7 Koma anadzichepetsa kotheratu nakhala ndi khalidwe ngati la kapolo ndi kukhala munthu ngati anthu ena onse.
temveč je samega sebe naredil brez slôvesa in si privzel obliko služabnika in bil narejen po človeški podobnosti;
8 Ndipo pokhala munthu choncho anadzichepetsa yekha ndipo anamvera mpaka imfa yake, imfa yake ya pamtanda!
in po videzu zaznan kakor moški, je samega sebe ponižal in postal pokoren do smrti, celó smrti na križu.
9 Choncho Mulungu anamukweza Iye kukhala wapamwamba kwambiri, ndipo anamupatsa dzina loposa dzina lina lililonse
Zatorej ga je Bog tudi visoko povišal in mu dal ime, ki je nad vsakim imenom,
10 kuti pakumva dzina la Yesu, bondo lililonse limugwadire, kumwamba ndi pa dziko lapansi ndi pansi pa dziko,
da naj bi ob imenu Jezus pokleknilo vsako koleno, od stvari na nebu in stvari na zemlji ter stvari pod zemljo;
11 ndipo lilime lililonse livomereze kuti Yesu Khristu ndi Ambuye kuchitira ulemu Mulungu Atate.
ter da bi vsak jezik priznal, da je Jezus Kristus Gospod, v slavo Boga Očeta.
12 Tsono, abwenzi anga okondedwa, monga mwakhala omvera nthawi zonse, osati pamene ndinali nanu pokha, koma tsopano koposa pamene ndili kutali. Pitirizani kugwira ntchito ya chipulumutso chanu mwa mantha ndi kunjenjemera,
Zatorej, moji ljubljeni, kakor ste vedno ubogali, ne kakor samo v moji prisotnosti, temveč veliko bolj zdaj, v moji odsotnosti, s strahom in trepetom uresničite svojo lastno rešitev duše.
13 pakuti ndi Mulungu amene amagwira ntchito mwa inu kuti mufune ndi kuchita zimene zimamukondweretsa Iyeyo.
Kajti Bog je, ki deluje v vas oboje, da hočete in da delate iz njegovega dobrega zadovoljstva.
14 Muzichita zonse mosawiringula kapena mosatsutsapo,
Vse stvari delajte brez mrmranj in razpravljanj,
15 kuti mukhale wopanda cholakwa ndi angwiro, ana a Mulungu wopanda cholakwika mu mʼbado uno wachinyengo ndi wosocheretsa. Mukatero mudzawala pakati pawo ngati nyenyezi zakumwamba
da boste lahko brez krivde in neškodljivi Božji sinovi, brez oštevanja v sredi sprijenega in sprevrženega naroda, med katerim sijete kakor luči na svetu;
16 powawuza mawu amoyo. Ndipo ine ndidzatha kunyadira pa tsiku la Khristu kuti sindinathamange kapena kugwira ntchito pachabe.
držeč se besede življenja, da se bom na Kristusov dan lahko veselil, da nisem zaman tekel niti [se nisem] zaman trudil.
17 Koma ngakhale ndikuthiridwa ngati nsembe ya chakumwa yoperekedwa pa nsembe ndi pa utumiki wochokera mʼchikhulupiriro chanu, ndine wokondwa ndi wosangalala pamodzi ndi inu nonse.
Da, in če bi bil darovan na žrtev in službo vaše vere, se radostim in se z vami vsemi veselim.
18 Chomwechonso, inu khalani okondwa ndi osangalala nane pamodzi.
Zaradi istega razloga se tudi vi veselite in razveseljujte z menoj.
19 Ngati Ambuye Yesu alola, ndikukhulupirira kuti ndidzamutuma Timoteyo msanga kwanuko, kuti mwina ndingadzasangalale ndikadzamva za moyo wanu.
Toda zaupam v Gospoda Jezusa, da v kratkem pošljem k vam Timóteja, da bom tudi jaz, ko izvem vaše stanje, lahko dobro potolažen.
20 Ndilibenso wina monga iyeyu amene ali ndi chidwi chenicheni pa za moyo wanu.
Kajti nimam nobenega človeka istih misli, ki bo naravno skrbel za vaše stanje.
21 Pakuti aliyense amangofuna zokomera iye yekha osati zokomera Yesu Khristu.
Kajti vsi iščejo svoje lastno, ne [pa] stvari, ki so Jezusa Kristusa.
22 Koma inu mukudziwa kuti Timoteyo wadzionetsa yekha, chifukwa watumikira ndi ine pa ntchito ya Uthenga Wabwino monga mwana ndi abambo ake.
Vendar poznate dokaz o njem, da je z menoj služil v evangeliju kakor sin z očetom.
23 Choncho ndikuyembekezera kumutuma msanga ndikangodziwa mmene zinthu zanga ziyendere.
Njega se torej nadejam poslati tako kmalu, kot bom videl, kako bo z menoj.
24 Ndipo ndikukhulupirira kuti Ambuye akalola ine mwini ndidzafikanso kwanuko posachedwapa.
Toda zaupam v Gospoda, da bom kmalu prišel tudi sam.
25 Koma ndikuganiza kuti nʼkofunika kuti ndikutumizireni mʼbale wanga Epafrodito, mtumiki mnzanga ndi msilikali mnzanga, amenenso ndi mtumiki wanu amene munamutumiza kuti adzandithandize pa zosowa zanga.
Vendar se mi je zdelo potrebno poslati k vam Epafrodita, mojega brata in družabnika v trudu in soborca, toda vašega odposlanca in tega, ki je služil mojim potrebam.
26 Pakuti akukulakalakani nonsenu ndipo akusauka mu mtima chifukwa munamva kuti akudwala.
Kajti hrepenel je po vas vseh in bil poln potrtosti; zato ker ste slišali, da je bil bolan.
27 Zoonadi ankadwala ndipo anatsala pangʼono kumwalira. Koma Mulungu anamuchitira chifundo, ndipo sanangomuchitira chifundo iye yekhayu komanso ine, kuti chisoni changa chisachuluke.
Kajti zares je bil bolan, blizu smrti, toda Bog se ga je usmilil; in ne samo njega, ampak tudi mene, da ne bi imel bridkost na bridkost.
28 Choncho khumbo langa lofulumiza kumutumiza lakula, kuti pamene mumuonenso musangalale komanso kuti nkhawa yanga ichepe.
Poslal sem ga torej bolj hitro, da ko ga boste ponovno videli, se boste lahko razveselili in da bom jaz lahko manj žalosten.
29 Mulandireni mwa Ambuye ndi chimwemwe chachikulu, ndipo anthu onga iyeyu muziwachitira ulemu.
Sprejmite ga torej v Gospodu z vsem veseljem; in take imejte v časti;
30 Iyeyu anatsala pangʼono kufa chifukwa cha ntchito ya Khristu, anayika moyo pa chiswe kuti akwaniritse thandizo limene inu simukanatha.
ker je bil zaradi Kristusovega dela blizu smrti, ne oziraje se na svoje življenje, da dopolni pomanjkanje vašega služenja do mene.