< Afilipi 1 >
1 Paulo ndi Timoteyo, atumiki a Khristu Yesu. Kulembera anthu onse oyera mtima a ku Filipi amene ali mwa Khristu Yesu, pamodzi ndi oyangʼanira ndi atumiki awo.
Paulus och Timoteus, Kristi Jesu tjänare, hälsa alla de heliga i Kristus Jesus som bo i Filippi, tillika med församlingsföreståndare och församlingstjänare.
2 Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale kwa inu.
Nåd vare med eder och frid ifrån Gud, vår Fader, och Herren Jesus Kristus.
3 Ndimayamika Mulungu wanga nthawi zonse ndikakumbukira inu.
Jag tackar min Gud, så ofta jag tänker på eder,
4 Mʼmapemphero anga onse opempherera inu, nthawi zonse ndimapemphera ndi chimwemwe
i det jag alltid i alla mina böner med glädje beder för eder alla.
5 chifukwa mwakhala mukundithandiza polalikira Uthenga Wabwino kuyambira tsiku loyamba mpaka tsopano.
Jag tackar honom för att I, allt ifrån första dagen intill nu, haven deltagit i arbetet för evangelium.
6 Sindikukayika konse kuti Iye amene anayamba ntchito yabwino mwa inu adzayipitiriza ndi kuyimaliza mpaka pa tsiku la kubweranso kwa Khristu Yesu.
Och jag har den tillförsikten, att han som i eder har begynt ett gott verk, han skall ock fullborda det, intill Kristi Jesu dag.
7 Kwa ine ndi bwino kuti ndiziganiza zotere za nonsenu, popeza ndimakukondani, ngakhale ndikhale mʼndende, kapena pamene ndikuteteza ndi kukhazikitsa Uthenga Wabwino, inu nonse mumagawana nane chisomo cha Mulungu.
Och det är ju rätt och tillbörligt att jag tänker så om eder alla, eftersom jag, både när jag ligger i bojor, och när jag försvarar och befäster evangelium, har eder i mitt hjärta såsom alla med mig delaktiga i nåden.
8 Mulungu angandichitire umboni kuti ndimakulakalakani ndi chikondi cha Khristu Yesu.
Ty Gud är mitt vittne, han vet huru jag längtar efter eder alla med Kristi Jesu kärlek.
9 Ndipo pemphero langa ndi lakuti chikondi chanu chipitirire kukulirakulira pa chidziwitso ndi kuzama mʼmaganizo,
Och därom beder jag, att eder kärlek må allt mer och mer överflöda av kunskap och förstånd i allt,
10 kuti mukhoza kuzindikira chabwino koposa zonse ndi chiti kuti muthe kukhala wopanda chodetsa ndi wopanda chilema kufikira tsiku la Khristu.
så att I kunnen döma om vad rättast är, på det att I mån bliva rena och för ingen till stötesten, i väntan på Kristi dag,
11 Ndipo moyo wanu udzakhala odzazidwa ndi chipatso cha chilungamo chimene chimachokera mwa Yesu Khristu. Pakuti zimenezi zidzapereka ulemerero ndi matamando kwa Mulungu.
och bliva rika på rättfärdighetens frukt, vilken kommer genom Jesus Kristus, Gud till ära och pris.
12 Tsopano abale, ndikufuna mudziwe kuti chimene chandichitikira ine chathandiza kwambiri kupititsa patsogolo Uthenga Wabwino.
Jag vill att I, mina bröder, skolen veta att det som har vederfarits mig snarare har länt till evangelii framgång.
13 Chotsatira chake nʼchakuti zadziwika bwino lomwe kwa onse amene ali ku nyumba yaufumu kuti ine ndili mʼmaunyolo chifukwa cha Khristu.
Det har nämligen så blivit uppenbart för alla i pretoriet och för alla andra, att det är i Kristus som jag bär mina bojor;
14 Moti chifukwa cha maunyolo angawa, abale ambiri alimbikitsidwa kuyankhula Mawu a Mulungu molimbika ndi mopanda mantha.
och de flesta av bröderna hava genom mina bojor blivit så frimodiga i Herren, att de med allt större dristighet våga oförskräckt förkunna Guds ord.
15 Nʼzoonadi kuti ena amalalikira Khristu chifukwa cha kaduka ndi mikangano, koma ena chifukwa cha zolinga zabwino.
Somliga finnas väl ock, som av avund och trätlystnad predika Kristus, men det finnes också andra som göra det av god vilja.
16 Olalikira ndi zolinga zabwinowa amachita izi mwachikondi, podziwa kuti ine ndili muno chifukwa cha kuteteza Uthenga Wabwino.
Dessa senare göra det av kärlek, eftersom de veta att jag är satt till att försvara evangelium.
17 Ena aja amalalikira Khristu modzikonda osati moona mtima namaganiza kuti kutero kubweretsa mavuto pamene ndili mʼmaunyolo.
De förra åter förkunna Kristus av genstridighet, icke med rent sinne, i tanke att de skola tillskynda mig ytterligare bedrövelse i mina bojor.
18 Nanga kodi zimenezo zili ndi ntchito? Chofunika ndi chakuti Khristu alalikidwe, kaya ndi mwachinyengo kapena moona. Ndipo ndikukondwera chifukwa cha chimenechi. Ndithu, ndidzapitirira kukondwera,
Vad mer? Kristus bliver dock på ena eller andra sättet förkunnad, det må nu ske för syns skull eller i uppriktighet; och däröver gläder jag mig. Ja, jag skall ock framgent få glädja mig;
19 pakuti ndikudziwa kuti chifukwa cha mapemphero anu ndi thandizo lochokera kwa Mzimu wa Yesu Khristu, zimene zandionekera zidzathandiza kuti ndimasulidwe.
ty jag vet att detta skall lända mig till frälsning, genom eder förbön och därigenom att Jesu Kristi Ande förlänas mig.
20 Ndili ndi chiyembekezo chonse kuti sindidzachita manyazi ndi pangʼono pomwe, koma ndidzakhala ndi chilimbikitso chokwanira kuti monga mwa nthawi zonse, tsopano Khristu adzakwezedwa mʼthupi langa kaya ndi mʼmoyo kapena mu imfa.
Det är nämligen min trängtan och mitt hopp att jag i intet skall komma på skam, utan att Kristus, nu såsom alltid, skall av mig med all frimodighet bliva förhärligad i min kropp, det må ske genom liv eller genom död.
21 Pakuti kwa ine kukhala moyo ndi Khristu ndipo kufa ndi phindu.
Ty att leva, det är för mig Kristus, och att dö, det är för mig en vinning.
22 Ngati nditi ndipitirire kukhala ndi moyo mʼthupi ndiye kuti kwa ine ndi kugwira ntchito yopindulitsa. Kodi ndisankhe chiyani? Sindikudziwa.
Men om det att leva i köttet för mig är att utföra ett arbete som bär frukt, vilketdera skall jag då välja? Det kan jag icke säga.
23 Ndathinidwa ndi zinthu ziwirizi: Ndikulakalaka kunyamuka kuti ndikakhale ndi Khristu, chimene ndi chinthu chabwino kwambiri.
Jag drages åt båda hållen. Ty väl åstundar jag att bryta upp och vara hos Kristus, vilket ju vore mycket bättre;
24 Komanso nʼkofunika kwambiri kuti ndikhalebe mʼthupi chifukwa cha inu.
men att jag lever kvar i köttet är för eder skull mer av nöden.
25 Ndili ndi chitsimikizo, ndikudziwa kuti ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzapitirira nanu kuti nonse mupite mʼtsogolo ndi kukhala ndi chimwemwe mu chikhulupiriro
Och då jag är förvissad härom, vet jag att jag skall leva kvar och förbliva hos eder alla, eder till förkovran och glädje i tron,
26 kuti pokhala nanunso, kudzitamandira kwanu mwa Khristu Yesu kudzasefukire chifukwa cha ine.
för att eder berömmelse skall överflöda i Kristus Jesus, i fråga om mig, därigenom att jag ännu en gång kommer till eder.
27 Chilichonse chimene chingachitike, chachikulu nʼchakuti mukhale moyo ofanana ndi Uthenga Wabwino wa Khristu. Tsono ngati ndingabwere kudzakuonani kapena kumangomva za inu ndili kutali, ndidzadziwa kuti mwayima mwamphamvu mwa Mzimu mmodzi, kulimbika pamodzi ngati munthu mmodzi chifukwa cha chikhulupiriro cha Uthenga Wabwino
Fören allenast en sådan vandel som är värdig Kristi evangelium, så att jag -- vare sig jag kommer och besöker eder, eller jag förbliver frånvarande -- får höra om eder att I stån fasta i en och samme Ande och endräktigt kämpen tillsammans för tron på evangelium,
28 osachita mantha ndi pangʼono pomwe ndi amene akutsutsana nanu. Ichi ndi chizindikiro kwa iwo kuti adzawonongedwa, koma inu mudzapulumutsidwa ndi Mulungu.
utan att i något stycke låta skrämma eder av motståndarna. Ty att I så skicken eder är för dem ett vittnesbörd om att de själva gå mot fördärvet, men att I skolen bliva frälsta, och detta av Gud.
29 Pakuti inu mwapatsidwa mwayi osati ongokhulupirira Khristu kokha, koma wakumva zowawa mʼmalo mwa Khristu.
Åt eder har ju förunnats icke allenast att tro på Kristus, utan ock att lida för hans skull,
30 Inunso mukudutsa mʼzowawa zomwe zija munaona ndikudutsamo inenso ndipo pano mukumva kuti ndikukumana nazobe.
i det att I haven samma kamp som I förr sågen mig hava och nu hören att jag har.