< Afilipi 1 >
1 Paulo ndi Timoteyo, atumiki a Khristu Yesu. Kulembera anthu onse oyera mtima a ku Filipi amene ali mwa Khristu Yesu, pamodzi ndi oyangʼanira ndi atumiki awo.
Παύλος και Τιμόθεος, δούλοι του Ιησού Χριστού, προς πάντας τους αγίους εν Χριστώ Ιησού τους όντας εν Φιλίπποις μετά των επισκόπων και διακόνων.
2 Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale kwa inu.
χάρις είη υμίν και ειρήνη από Θεού Πατρός ημών και Κυρίου Ιησού Χριστού.
3 Ndimayamika Mulungu wanga nthawi zonse ndikakumbukira inu.
Ευχαριστώ τον Θεόν μου οσάκις σας ενθυμούμαι,
4 Mʼmapemphero anga onse opempherera inu, nthawi zonse ndimapemphera ndi chimwemwe
πάντοτε εν πάση προσευχή μου υπέρ πάντων υμών δεόμενος μετά χαράς,
5 chifukwa mwakhala mukundithandiza polalikira Uthenga Wabwino kuyambira tsiku loyamba mpaka tsopano.
διά την εις το ευαγγέλιον κοινωνίαν σας από της πρώτης ημέρας μέχρι του νυν,
6 Sindikukayika konse kuti Iye amene anayamba ntchito yabwino mwa inu adzayipitiriza ndi kuyimaliza mpaka pa tsiku la kubweranso kwa Khristu Yesu.
βέβαιος ων εις αυτό τούτο, ότι εκείνος όστις ήρχισεν εις εσάς καλόν έργον θέλει επιτελέσει αυτό μέχρι της ημέρας του Ιησού Χριστού,
7 Kwa ine ndi bwino kuti ndiziganiza zotere za nonsenu, popeza ndimakukondani, ngakhale ndikhale mʼndende, kapena pamene ndikuteteza ndi kukhazikitsa Uthenga Wabwino, inu nonse mumagawana nane chisomo cha Mulungu.
καθώς είναι δίκαιον εις εμέ να φρονώ τούτο περί πάντων υμών, διότι σας έχω εν τη καρδία μου, και είσθε πάντες σεις και εις τα δεσμά μου και εις την απολογίαν και εις την βεβαίωσιν του ευαγγελίου συγκοινωνοί μου της χάριτος.
8 Mulungu angandichitire umboni kuti ndimakulakalakani ndi chikondi cha Khristu Yesu.
Διότι μάρτυς μου είναι ο Θεός, ότι σας επιποθώ πάντας με σπλάγχνα Ιησού Χριστού.
9 Ndipo pemphero langa ndi lakuti chikondi chanu chipitirire kukulirakulira pa chidziwitso ndi kuzama mʼmaganizo,
Και τούτο προσεύχομαι, να περισσεύση η αγάπη σας έτι μάλλον και μάλλον εις επίγνωσιν και εις πάσαν νόησιν,
10 kuti mukhoza kuzindikira chabwino koposa zonse ndi chiti kuti muthe kukhala wopanda chodetsa ndi wopanda chilema kufikira tsiku la Khristu.
διά να διακρίνητε τα διαφέροντα, ώστε να ήσθε ειλικρινείς και απρόσκοποι μέχρι της ημέρας του Χριστού,
11 Ndipo moyo wanu udzakhala odzazidwa ndi chipatso cha chilungamo chimene chimachokera mwa Yesu Khristu. Pakuti zimenezi zidzapereka ulemerero ndi matamando kwa Mulungu.
πλήρεις καρπών δικαιοσύνης των διά του Ιησού Χριστού εις δόξαν και έπαινον Θεού.
12 Tsopano abale, ndikufuna mudziwe kuti chimene chandichitikira ine chathandiza kwambiri kupititsa patsogolo Uthenga Wabwino.
Θέλω δε να εξεύρητε, αδελφοί, ότι τα συμβάντα εις εμέ συνέτρεξαν μάλλον εις πρόοδον του ευαγγελίου,
13 Chotsatira chake nʼchakuti zadziwika bwino lomwe kwa onse amene ali ku nyumba yaufumu kuti ine ndili mʼmaunyolo chifukwa cha Khristu.
ώστε τα διά τον Χριστόν δεσμά μου έγειναν φανερά εις όλον το πραιτώριον και εις πάντας τους λοιπούς,
14 Moti chifukwa cha maunyolo angawa, abale ambiri alimbikitsidwa kuyankhula Mawu a Mulungu molimbika ndi mopanda mantha.
και οι πλειότεροι των εν Κυρίω αδελφών πεποιθότες εις τα δεσμά μου τολμώσι περισσότερον να κηρύττωσιν αφόβως τον λόγον.
15 Nʼzoonadi kuti ena amalalikira Khristu chifukwa cha kaduka ndi mikangano, koma ena chifukwa cha zolinga zabwino.
Τινές μεν και διά φθόνον και έριδα, τινές δε και από καλής θελήσεως κηρύττουσι τον Χριστόν·
16 Olalikira ndi zolinga zabwinowa amachita izi mwachikondi, podziwa kuti ine ndili muno chifukwa cha kuteteza Uthenga Wabwino.
οι μεν κηρύττουσιν εξ αντιζηλίας τον Χριστόν, ουχί εν καθαρότητι, νομίζοντες ότι προσθέτουσι θλίψιν εις τα δεσμά μου·
17 Ena aja amalalikira Khristu modzikonda osati moona mtima namaganiza kuti kutero kubweretsa mavuto pamene ndili mʼmaunyolo.
οι δε εξ αγάπης, εξεύροντες ότι είμαι τεταγμένος εις απολογίαν του ευαγγελίου.
18 Nanga kodi zimenezo zili ndi ntchito? Chofunika ndi chakuti Khristu alalikidwe, kaya ndi mwachinyengo kapena moona. Ndipo ndikukondwera chifukwa cha chimenechi. Ndithu, ndidzapitirira kukondwera,
Τι λοιπόν πλην κατά πάντα τρόπον, είτε επί προφάσει είτε τη αληθεία, ο Χριστός κηρύττεται· και εις τούτο χαίρω αλλά και θέλω χαίρει.
19 pakuti ndikudziwa kuti chifukwa cha mapemphero anu ndi thandizo lochokera kwa Mzimu wa Yesu Khristu, zimene zandionekera zidzathandiza kuti ndimasulidwe.
Διότι εξεύρω ότι τούτο θέλει αποβή εις εμέ προς σωτηρίαν διά της δεήσεώς σας και διά της βοηθείας, του Πνεύματος του Ιησού Χριστού,
20 Ndili ndi chiyembekezo chonse kuti sindidzachita manyazi ndi pangʼono pomwe, koma ndidzakhala ndi chilimbikitso chokwanira kuti monga mwa nthawi zonse, tsopano Khristu adzakwezedwa mʼthupi langa kaya ndi mʼmoyo kapena mu imfa.
κατά την σταθεράν προσδοκίαν και ελπίδα μου ότι δεν θέλω αισχυνθή εις ουδέν, αλλά μετά πάσης παρρησίας ως πάντοτε και τώρα θέλει μεγαλυνθή ο Χριστός εν τω σώματί μου είτε διά ζωής είτε διά θανάτου.
21 Pakuti kwa ine kukhala moyo ndi Khristu ndipo kufa ndi phindu.
Διότι εις εμέ το ζην είναι ο Χριστός και το αποθανείν κέρδος.
22 Ngati nditi ndipitirire kukhala ndi moyo mʼthupi ndiye kuti kwa ine ndi kugwira ntchito yopindulitsa. Kodi ndisankhe chiyani? Sindikudziwa.
Αλλ' εάν το να ζω εν σαρκί τούτο συμβάλλη εις καρποφορίαν του έργου μου, και τι να εκλέξω δεν γνωρίζω.
23 Ndathinidwa ndi zinthu ziwirizi: Ndikulakalaka kunyamuka kuti ndikakhale ndi Khristu, chimene ndi chinthu chabwino kwambiri.
Διότι στενοχωρούμαι υπό των δύο, έχων μεν την επιθυμίαν να αναχωρήσω και να είμαι με τον Χριστόν· διότι είναι πολύ πλέον καλήτερον·
24 Komanso nʼkofunika kwambiri kuti ndikhalebe mʼthupi chifukwa cha inu.
το να μένω όμως εν τη σαρκί είναι αναγκαιότερον διά σας.
25 Ndili ndi chitsimikizo, ndikudziwa kuti ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzapitirira nanu kuti nonse mupite mʼtsogolo ndi kukhala ndi chimwemwe mu chikhulupiriro
Και τούτο εξεύρω εν πεποιθήσει ότι θέλω μείνει και συμπαραμείνει μετά πάντων υμών διά την εις την πίστιν προκοπήν σας και χαράν,
26 kuti pokhala nanunso, kudzitamandira kwanu mwa Khristu Yesu kudzasefukire chifukwa cha ine.
διά να περισσεύη δι' εμού το καύχημά σας εις τον Ιησούν Χριστόν διά της εμής πάλιν παρουσίας προς εσάς.
27 Chilichonse chimene chingachitike, chachikulu nʼchakuti mukhale moyo ofanana ndi Uthenga Wabwino wa Khristu. Tsono ngati ndingabwere kudzakuonani kapena kumangomva za inu ndili kutali, ndidzadziwa kuti mwayima mwamphamvu mwa Mzimu mmodzi, kulimbika pamodzi ngati munthu mmodzi chifukwa cha chikhulupiriro cha Uthenga Wabwino
Μόνον πολιτεύεσθε αξίως του ευαγγελίου του Χριστού, διά να ακούσω, είτε όταν έλθω και σας ίδω είτε ενώ είμαι απών, την κατάστασίν σας, ότι στέκεσθε εις εν πνεύμα, συναγωνιζόμενοι εν μιά ψυχή διά την πίστιν του ευαγγελίου,
28 osachita mantha ndi pangʼono pomwe ndi amene akutsutsana nanu. Ichi ndi chizindikiro kwa iwo kuti adzawonongedwa, koma inu mudzapulumutsidwa ndi Mulungu.
και μη φοβιζόμενοι εις ουδέν από των εναντίων, το οποίον εις αυτούς μεν είναι ένδειξις απωλείας, εις εσάς δε σωτηρίας, και τούτο από Θεού·
29 Pakuti inu mwapatsidwa mwayi osati ongokhulupirira Khristu kokha, koma wakumva zowawa mʼmalo mwa Khristu.
διότι εις εσάς εχαρίσθη το υπέρ Χριστού, ου μόνον το να πιστεύητε εις αυτόν, αλλά και το να πάσχητε υπέρ αυτού,
30 Inunso mukudutsa mʼzowawa zomwe zija munaona ndikudutsamo inenso ndipo pano mukumva kuti ndikukumana nazobe.
έχοντες τον αυτόν αγώνα, οποίον είδετε εν εμοί και τώρα ακούετε εν εμοί.