< Afilipi 1 >
1 Paulo ndi Timoteyo, atumiki a Khristu Yesu. Kulembera anthu onse oyera mtima a ku Filipi amene ali mwa Khristu Yesu, pamodzi ndi oyangʼanira ndi atumiki awo.
Yesus kiristoosa oothancha gidida Phawulosapene Xintoosape woossa keeththa cimatarane daqonistara issife Pilipisiyosa deren diza ammanizaytas Yesus kiristoosas dummatidaytas wursios,
2 Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale kwa inu.
Nu Aawa Xoossafe Goda Yesus kiristoosape kiyatethine saroteth intes gido.
3 Ndimayamika Mulungu wanga nthawi zonse ndikakumbukira inu.
Intena qopiza wursio galas tani ta Xoossa galatays.
4 Mʼmapemphero anga onse opempherera inu, nthawi zonse ndimapemphera ndi chimwemwe
Wurisio gallas inte gishshi ta woossiza wode ufayssan woossays.
5 chifukwa mwakhala mukundithandiza polalikira Uthenga Wabwino kuyambira tsiku loyamba mpaka tsopano.
Koyro gallasafe ha simmin ha7i gakanas mishiracho qaala oothon inte tanara deista.
6 Sindikukayika konse kuti Iye amene anayamba ntchito yabwino mwa inu adzayipitiriza ndi kuyimaliza mpaka pa tsiku la kubweranso kwa Khristu Yesu.
Intenan lo7o ootho doommmidayssi izi Yesus kiristoosay wursietha piridas yaana gakanas intena danda7issanayssa ta ammanays.
7 Kwa ine ndi bwino kuti ndiziganiza zotere za nonsenu, popeza ndimakukondani, ngakhale ndikhale mʼndende, kapena pamene ndikuteteza ndi kukhazikitsa Uthenga Wabwino, inu nonse mumagawana nane chisomo cha Mulungu.
Ta ha7i qasho keeththan dishinine ta qachistanapeka kase mishiracho qaala tuma naaganasine minithanas Xoossi taas ba kiyatethan immida maadon inte wurikka tanara issife oothidayta gidida gishshi inte wursio galas ta wozinape dhayekkista. Hessa gishshi ta inte gishshi qopanas taas besses.
8 Mulungu angandichitire umboni kuti ndimakulakalakani ndi chikondi cha Khristu Yesu.
T ainttena Yesus kiristoosa siiqon wossita amotizakkone Xooss taas marikako.
9 Ndipo pemphero langa ndi lakuti chikondi chanu chipitirire kukulirakulira pa chidziwitso ndi kuzama mʼmaganizo,
Inte siiqoy eratethaninne akkekan keehi darana mala ta woossays.
10 kuti mukhoza kuzindikira chabwino koposa zonse ndi chiti kuti muthe kukhala wopanda chodetsa ndi wopanda chilema kufikira tsiku la Khristu.
Hessika inte wursiofe adhdhizayssa shaaki erana malane Yesus kiristoosa yuusa galas gakanas inte geeshatane wothoy bayndayta gidana mala koyayiss.
11 Ndipo moyo wanu udzakhala odzazidwa ndi chipatso cha chilungamo chimene chimachokera mwa Yesu Khristu. Pakuti zimenezi zidzapereka ulemerero ndi matamando kwa Mulungu.
Xoossa bonchisizayssane galatissizayssa inte oothana mala Yesus kiristoosan beettiza geeshatetha ayfen inte wozinay kumo.
12 Tsopano abale, ndikufuna mudziwe kuti chimene chandichitikira ine chathandiza kwambiri kupititsa patsogolo Uthenga Wabwino.
Ha7ika ta ishato ta bolla gakida metoy mishiracho qaalay kasepe dari aakanas gididayssa inte erana mala ta koyays.
13 Chotsatira chake nʼchakuti zadziwika bwino lomwe kwa onse amene ali ku nyumba yaufumu kuti ine ndili mʼmaunyolo chifukwa cha Khristu.
Hessa gishshi ta qachetethay kiristoosa gishshi gididayssi kawo keeththa zabaynatasine hartasika eretides.
14 Moti chifukwa cha maunyolo angawa, abale ambiri alimbikitsidwa kuyankhula Mawu a Mulungu molimbika ndi mopanda mantha.
Ta qachetidayssa geedon ammanizayti Xoossa qaala babbontta xalatethan asas marikatanas minoteth demmida.
15 Nʼzoonadi kuti ena amalalikira Khristu chifukwa cha kaduka ndi mikangano, koma ena chifukwa cha zolinga zabwino.
Issi issi asati coo nu izape waanidoni geethanine hollotethan sabakettes. Baggayti qasse lo7o qofara Kiristoosa gishshi sabaketes.
16 Olalikira ndi zolinga zabwinowa amachita izi mwachikondi, podziwa kuti ine ndili muno chifukwa cha kuteteza Uthenga Wabwino.
Baggayti ta mishiracho qaala gishshi mootistana haan dizayssa eriza gishshi siiqon sabaketes.
17 Ena aja amalalikira Khristu modzikonda osati moona mtima namaganiza kuti kutero kubweretsa mavuto pamene ndili mʼmaunyolo.
Hankoyti qasse lo7o qofan gidontta tana gakida qashoza bolla hara waaye gathanasine ba iitta qofa polanas Kiristoosa sabaketes.
18 Nanga kodi zimenezo zili ndi ntchito? Chofunika ndi chakuti Khristu alalikidwe, kaya ndi mwachinyengo kapena moona. Ndipo ndikukondwera chifukwa cha chimenechi. Ndithu, ndidzapitirira kukondwera,
Heessa gidikone aya meto dizay! Waana ayfe yooy suuretethan gidin woykko milatoson gidinka awaraka kiristoosa sabakiza gishshi ta ufa7istayss. Qassekka ta ufa7istana.
19 pakuti ndikudziwa kuti chifukwa cha mapemphero anu ndi thandizo lochokera kwa Mzimu wa Yesu Khristu, zimene zandionekera zidzathandiza kuti ndimasulidwe.
Ta birshista atany inte woossanine Yesus kiristoosa ayana maadon gididayssa ta erayss.
20 Ndili ndi chiyembekezo chonse kuti sindidzachita manyazi ndi pangʼono pomwe, koma ndidzakhala ndi chilimbikitso chokwanira kuti monga mwa nthawi zonse, tsopano Khristu adzakwezedwa mʼthupi langa kaya ndi mʼmoyo kapena mu imfa.
Ta ay ogeraka yeellatontta mala mino ufayssine laamotay taas dees. Gido attin kaseka hachchika, ta hayqqinka paxa diin kiristoosay ta ashon bonchetanayssa ta xalatethan hasa7ayss.
21 Pakuti kwa ine kukhala moyo ndi Khristu ndipo kufa ndi phindu.
Taas duusu guusi kiristoosako. Hayqoyka taas go7ako.
22 Ngati nditi ndipitirire kukhala ndi moyo mʼthupi ndiye kuti kwa ine ndi kugwira ntchito yopindulitsa. Kodi ndisankhe chiyani? Sindikudziwa.
Gido attin hayssa tanni hayssa asho dusan guja dizakko ayfe immiza ootho othays gusukko. Ta awayssa dooranakone taas erettena.
23 Ndathinidwa ndi zinthu ziwirizi: Ndikulakalaka kunyamuka kuti ndikakhale ndi Khristu, chimene ndi chinthu chabwino kwambiri.
Ha nam77u Hanotan metotistadis. Ta baada kiristoosara daanas laamotayss. Hessi hara wursiofe keehi lo7oko.
24 Komanso nʼkofunika kwambiri kuti ndikhalebe mʼthupi chifukwa cha inu.
Gido attin taas ashon duusi intes keehi koshees.
25 Ndili ndi chitsimikizo, ndikudziwa kuti ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzapitirira nanu kuti nonse mupite mʼtsogolo ndi kukhala ndi chimwemwe mu chikhulupiriro
Hessan amanistada ta hayqoppe atada intenara deyin ntte diccanaysanne inte amanon ufa7istanaysa ta ammanetayss.
26 kuti pokhala nanunso, kudzitamandira kwanu mwa Khristu Yesu kudzasefukire chifukwa cha ine.
Ta he bada inte achan deyikko ta gedon intes Kirstosan diza ceqetethi darana.
27 Chilichonse chimene chingachitike, chachikulu nʼchakuti mukhale moyo ofanana ndi Uthenga Wabwino wa Khristu. Tsono ngati ndingabwere kudzakuonani kapena kumangomva za inu ndili kutali, ndidzadziwa kuti mwayima mwamphamvu mwa Mzimu mmodzi, kulimbika pamodzi ngati munthu mmodzi chifukwa cha chikhulupiriro cha Uthenga Wabwino
Kiristoosa mishiracho qaalas bessiza mala diite. Hessatho hanika ta intena hee baada be7idako woykko hahon daada inte gishshi ta siyizako inte mishiracho qaala ammanos issino oletishe issi ayanan inte minni eqnayssa ta erayss.
28 osachita mantha ndi pangʼono pomwe ndi amene akutsutsana nanu. Ichi ndi chizindikiro kwa iwo kuti adzawonongedwa, koma inu mudzapulumutsidwa ndi Mulungu.
Ay ogeraka intenara eqetizaytas hirigopite. Hessi istti dhayanasine inte atanayssas Xoossafe imettida malatako.
29 Pakuti inu mwapatsidwa mwayi osati ongokhulupirira Khristu kokha, koma wakumva zowawa mʼmalo mwa Khristu.
Inte kiristoosa ammanizayta xalala gidontta iza gishshi waaye ekizayta gidana mala hayssi Xoossa kiyatethi intes imettides.
30 Inunso mukudutsa mʼzowawa zomwe zija munaona ndikudutsamo inenso ndipo pano mukumva kuti ndikukumana nazobe.
Inte kase beyida mala ha7ika ta bolla dizayssa inte siyizayssa mala hessaththo intenaka waayison dees.