< Afilipi 1 >
1 Paulo ndi Timoteyo, atumiki a Khristu Yesu. Kulembera anthu onse oyera mtima a ku Filipi amene ali mwa Khristu Yesu, pamodzi ndi oyangʼanira ndi atumiki awo.
An Paulo gi Timotheo ma wasumb Kristo Yesu, Wandikonu un jomaler duto mag Kristo Yesu man Filipi, kaachiel gi jokwadh jo-Kristo duto gi jokonygi:
2 Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale kwa inu.
Ngʼwono kod kwe mar Nyasaye Wuonwa kod Ruoth Yesu Kristo, obed kodu.
3 Ndimayamika Mulungu wanga nthawi zonse ndikakumbukira inu.
Adwokone Nyasacha erokamano seche duto ma aparoue.
4 Mʼmapemphero anga onse opempherera inu, nthawi zonse ndimapemphera ndi chimwemwe
Kinde duto ka alemonu, to alemonu gi mor,
5 chifukwa mwakhala mukundithandiza polalikira Uthenga Wabwino kuyambira tsiku loyamba mpaka tsopano.
nikech riwruok maru kodwa e tij lando Injili chakre odiechiengʼ mokwongo nyaka koroni,
6 Sindikukayika konse kuti Iye amene anayamba ntchito yabwino mwa inu adzayipitiriza ndi kuyimaliza mpaka pa tsiku la kubweranso kwa Khristu Yesu.
omiyo koro an gichir malongʼo ni Jal mane ochako tich maberno e chunyu biro dhi kode nyime nyaka chop orum e odiechieng Kristo Yesu.
7 Kwa ine ndi bwino kuti ndiziganiza zotere za nonsenu, popeza ndimakukondani, ngakhale ndikhale mʼndende, kapena pamene ndikuteteza ndi kukhazikitsa Uthenga Wabwino, inu nonse mumagawana nane chisomo cha Mulungu.
En gima kare mondo apar kamano kuomu uduto nikech agenou e chunya; kata ka an e twech kata ka asiro adiera mar Injili kendo ajiwe to un uduto usebedo koda e achiel kuom ngʼwono mar Nyasaye.
8 Mulungu angandichitire umboni kuti ndimakulakalakani ndi chikondi cha Khristu Yesu.
Nyasaye owuon nyalo timo nenda kaka chunya gombou duto ka an-gi hera matut mar Kristo Yesu.
9 Ndipo pemphero langa ndi lakuti chikondi chanu chipitirire kukulirakulira pa chidziwitso ndi kuzama mʼmaganizo,
Kendo ma e lamona mondo herau omedre mathoth ahinya kuom rieko kod ngʼeyo,
10 kuti mukhoza kuzindikira chabwino koposa zonse ndi chiti kuti muthe kukhala wopanda chodetsa ndi wopanda chilema kufikira tsiku la Khristu.
kendo mondo ubed gi rieko mar yiero mana timo gima ber kende. Kamano ngimau nobed maler kendo maonge bura, nyaka chop odiechieng Kristo.
11 Ndipo moyo wanu udzakhala odzazidwa ndi chipatso cha chilungamo chimene chimachokera mwa Yesu Khristu. Pakuti zimenezi zidzapereka ulemerero ndi matamando kwa Mulungu.
Ngimau nopongʼ gi olemo mag timbe makare maa kuom Yesu Kristo mondo Nyasaye oyud duongʼ kod pak.
12 Tsopano abale, ndikufuna mudziwe kuti chimene chandichitikira ine chathandiza kwambiri kupititsa patsogolo Uthenga Wabwino.
Jowetena, koro adwaro ni ungʼe, ni gik mosetimorena osemiyo Injili omedo landore.
13 Chotsatira chake nʼchakuti zadziwika bwino lomwe kwa onse amene ali ku nyumba yaufumu kuti ine ndili mʼmaunyolo chifukwa cha Khristu.
Kuom mano, koro osengʼere malongʼo ne askeche dala ruoth duto, kod ji mamoko duto ni otweya nikech Kristo.
14 Moti chifukwa cha maunyolo angawa, abale ambiri alimbikitsidwa kuyankhula Mawu a Mulungu molimbika ndi mopanda mantha.
Bedona e twech osemiyo jowete mathoth odoko thuondi kuom Ruoth, mi giyalo Wach Nyasaye gi chir maonge luoro.
15 Nʼzoonadi kuti ena amalalikira Khristu chifukwa cha kaduka ndi mikangano, koma ena chifukwa cha zolinga zabwino.
En adier ni jomoko lando wach Kristo ka gin-gi ich lit kod miero, to jomoko to lande ka chunygi ni kare.
16 Olalikira ndi zolinga zabwinowa amachita izi mwachikondi, podziwa kuti ine ndili muno chifukwa cha kuteteza Uthenga Wabwino.
Joma lando Injili gi chuny makarego lendo gihera, ka gingʼeyo ni oketa e twech mondo aked matek ni Injili.
17 Ena aja amalalikira Khristu modzikonda osati moona mtima namaganiza kuti kutero kubweretsa mavuto pamene ndili mʼmaunyolo.
Joma lando Kristo ka gin-gi ich lit gi miero to timo kamano mondo oyud duongʼ, ka giparo niginyalo medona chandruok ka pod an e od twech.
18 Nanga kodi zimenezo zili ndi ntchito? Chofunika ndi chakuti Khristu alalikidwe, kaya ndi mwachinyengo kapena moona. Ndipo ndikukondwera chifukwa cha chimenechi. Ndithu, ndidzapitirira kukondwera,
To onge wach! Gima duongʼ en ni wach Kristo ilando e yore duto; kata gi chuny marach, kata maber, kendo mano medo miya mor moloyo. Ee, kendo pod abiro medo bedo mamor,
19 pakuti ndikudziwa kuti chifukwa cha mapemphero anu ndi thandizo lochokera kwa Mzimu wa Yesu Khristu, zimene zandionekera zidzathandiza kuti ndimasulidwe.
nikech angʼeyo ni kuom lemo mulemonago kod kony ma ayudo kuom Roho mar Yesu Kristo, gik mosetimorenago ema bende biro kelona resruok.
20 Ndili ndi chiyembekezo chonse kuti sindidzachita manyazi ndi pangʼono pomwe, koma ndidzakhala ndi chilimbikitso chokwanira kuti monga mwa nthawi zonse, tsopano Khristu adzakwezedwa mʼthupi langa kaya ndi mʼmoyo kapena mu imfa.
Dwarona maduongʼ kod genona en ni ok anane wichkuot, to ni abiro bedo gi teko moromo mondo Kristo osik ka yudo duongʼ e ringra kaka pile, bed ni angima kata atho.
21 Pakuti kwa ine kukhala moyo ndi Khristu ndipo kufa ndi phindu.
Nikech an aneno ni ka angima, to angima nikech Kristo, to ka atho to en ohala.
22 Ngati nditi ndipitirire kukhala ndi moyo mʼthupi ndiye kuti kwa ine ndi kugwira ntchito yopindulitsa. Kodi ndisankhe chiyani? Sindikudziwa.
Kane anyalo medo bedo mangima e ringruok, to mano nyiso ni abiro medo tiyo tich makelo ohala. To koro dayier angʼo? Ok angʼeyo gima dayier!
23 Ndathinidwa ndi zinthu ziwirizi: Ndikulakalaka kunyamuka kuti ndikakhale ndi Khristu, chimene ndi chinthu chabwino kwambiri.
Yiero otama e kind gik mabeyo ariyogi: Chunya gombo ni atho mondo adhi abed gi Kristo, kendo mano en gima ber moloyo,
24 Komanso nʼkofunika kwambiri kuti ndikhalebe mʼthupi chifukwa cha inu.
to daher moloyo mondo amed bedo mangima e ringruok nikech un.
25 Ndili ndi chitsimikizo, ndikudziwa kuti ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzapitirira nanu kuti nonse mupite mʼtsogolo ndi kukhala ndi chimwemwe mu chikhulupiriro
Nikech chunya nigi ratiro chutho ni pod onego akonyu, kendo angʼeyo chutho ni pod abiro bet kodu duto mondo ami umed geroru kendo ubed mamor e yie maru,
26 kuti pokhala nanunso, kudzitamandira kwanu mwa Khristu Yesu kudzasefukire chifukwa cha ine.
mondo omi bedona kodu kendo omedu mor moloyo kuom Kristo Yesu nikech an.
27 Chilichonse chimene chingachitike, chachikulu nʼchakuti mukhale moyo ofanana ndi Uthenga Wabwino wa Khristu. Tsono ngati ndingabwere kudzakuonani kapena kumangomva za inu ndili kutali, ndidzadziwa kuti mwayima mwamphamvu mwa Mzimu mmodzi, kulimbika pamodzi ngati munthu mmodzi chifukwa cha chikhulupiriro cha Uthenga Wabwino
To kata obedo ni angʼo motimore, to usik kudak e kit ngimau mapile mowinjore gi Injili mar Kristo. Kata ka abiro nenou, kata ka ok abiro, to adwaro winjo ni uchungʼ motegno gi chuny achiel kendo gi paro achiel mondo ukedni adiera mar Injili,
28 osachita mantha ndi pangʼono pomwe ndi amene akutsutsana nanu. Ichi ndi chizindikiro kwa iwo kuti adzawonongedwa, koma inu mudzapulumutsidwa ndi Mulungu.
ma ok obwogu e yo moro amora, gi joma kwedou. Mano biro bedonegi ranyisi ni ibiro tiekgi, to un ibiro resu kendo Nyasaye ema biro timo mano.
29 Pakuti inu mwapatsidwa mwayi osati ongokhulupirira Khristu kokha, koma wakumva zowawa mʼmalo mwa Khristu.
Nikech dhial museyudo kuom Kristo ok en mana mondo uyie kuome kende, to oseluongu bende mondo une masiche nikech en,
30 Inunso mukudutsa mʼzowawa zomwe zija munaona ndikudutsamo inenso ndipo pano mukumva kuti ndikukumana nazobe.
nikech ukedo lweny nogo mane unena kakedo e kinde mokalo, kendo ma pod uwinjo ni akedo.