< Filemoni 1 >
1 Kuchokera kwa Paulo, amene ndili mʼndende chifukwa cha Khristu Yesu ndi Timoteyo mʼbale wathu. Kulembera Filemoni, bwenzi lathu lokondedwa ndi mtumiki mnzathu.
Paulus, Kristi Jesu Fange, og Broderen Timotheus til Filemon, vor elskede og Medarbejder,
2 Kwa Apiya mlongo wathu, Arkipo msilikali mnzathu, ndiponso mpingo umene umasonkhana mʼnyumba mwanu.
og til Søsteren Appia og Arkippus, vor Medstrider, og Menigheden i dit Hus;
3 Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale ndi inu.
Nåde være med eder og Fred fra Gud vor Fader og den Herre Jesus Kristus!
4 Ine ndimayamika Mulungu wanga nthawi zonse ndikakukumbukira iwe mʼmapemphero anga.
Jeg takker min Gud altid, når jeg kommer dig i Hu i mine Bønner,
5 Pakuti ndamva za chikondi chako, za chikhulupiriro chako mwa Ambuye Yesu ndiponso za chikondi chako pa oyera mtima onse.
efterdi jeg hører om din Kærlighed og den Tro, som du har til den Herre Jesus og til alle de hellige,
6 Ine ndikupemphera kuti mgwirizano wako ndi ife mʼchikhulupiriro ukhale opindulitsa pozamitsa nzeru zako zozindikira zinthu zilizonse zabwino zimene timagawana chifukwa cha Khristu.
for at din Delagtighed i Troen må blive virksom for Kristus i Erkendelse af alt det gode, som er i eder.
7 Mʼbale, chikondi chako chandipatsa chimwemwe chachikulu ndi chilimbikitso, chifukwa umatsitsimutsa mitima ya anthu a Ambuye.
Thi stor Glæde og Trøst har jeg fået af din Kærlighed, efterdi de helliges Hjerter ere blevne vederkvægede ved dig, Broder!
8 Tsopano ngakhale kuti mwa Khristu nditha kulimba mtima ndi kulamulira kuti uchite zimene uyenera kuchita,
Derfor, endskønt jeg kunde med stor Frimodighed i Kristus befale dig det, som er tilbørligt,
9 komabe ndikupempha mwachikondi. Ine Paulo, munthu wokalamba, ndipo tsopano ndili mʼndende chifukwa cha Khristu Yesu,
så beder jeg dig dog hellere for Kærlighedens Skyld, sådan som jeg er, som den gamle Paulus, og nu tilmed Kristi Jesu Fange;
10 ndikukupempha chifukwa cha mwana wanga Onesimo, amene ndamubala ndili mu unyolo.
jeg beder dig for mit Barn, som jeg har avlet i mine Lænker, Onesimus,
11 Anali wopanda phindu kwa iwe, koma tsopano wasanduka wa phindu kwa iwe ndi kwa inenso.
ham, som tilforn var dig unyttig, men nu er nyttig både for dig og for mig, ham, som jeg sender dig tilbage,
12 Ine ndikumutumizanso kwa iwe tsopano, koma potero ndikukhala ngati ndikutumiza mtima wanga weniweni.
ham, det er mit eget Hjerte.
13 Ndikanakonda ndikanakhala naye kuno kuti iyeyo azinditumikira mʼmalo mwako pamene ndili mu unyolo chifukwa cha Uthenga Wabwino.
Ham vilde jeg gerne beholde hos mig, for at han i dit Sted kunde tjene mig i Evangeliets Lænker.
14 Koma sindikufuna kuchita kanthu osakufunsa, nʼcholinga chakuti chilichonse chabwino ungandichitire chikhale mwakufuna kwako osati mokakamiza.
Men, uden dit Samtykke vilde jeg intet gøre, for at din Godhed ikke skulde være som af Tvang, men af fri Villie.
15 Mwina chifukwa chimene unasiyana naye kwa kanthawi ndi chakuti ukhale nayenso nthawi zonse. (aiōnios )
Thi måske blev han derfor skilt fra dig en liden Tid, for at du kunde få ham igen til evigt Eje, (aiōnios )
16 Osati ngati kapolo, koma woposa kapolo, ngati mʼbale wokondedwa. Iyeyu ndi wokondedwa kwambiri kwa ine koma kwa iweyo ndi wokondedwa koposa, ngati munthu komanso ngati mʼbale mwa Ambuye.
ikke mere som en Træl, men som mere end en Træl, som en elsket Broder, særlig for mig, men hvor meget mere for dig, både i Kødet og i Herren.
17 Tsono ngati umati ndine mnzako, umulandire iyeyu monga momwe ukanandilandirira ineyo.
Dersom da du anser mig for din Medbroder, så modtag ham som mig!
18 Ngati anakulakwira kapena kukongola kanthu kalikonse, ndidzalipira ineyo.
Men har han gjort dig nogen Uret eller er dig noget skyldig, da før mig det til Regning!
19 Ine, Paulo ndikulemba zimenezi ndi dzanja langa. Ine ndidzalipira. Nʼkosafunika kukukumbutsa kuti iweyo ngongole yako kwa ine ndi moyo wakowo.
Jeg, Paulus, skriver med min egen Hånd, jeg vil betale, for ikke at sige dig, at du desuden også skylder mig dig selv.
20 Mʼbale, ndikufuna kuti ndipindule nawe mwa Ambuye; tsono tsitsimutsa mtima wanga mwa Khristu.
Ja, Broder! lad mig få Gavn af dig i Herren, vederkvæg mit Hjerte i Kristus!
21 Ine ndili ndi chitsimikizo cha kumvera kwako pamene ndikukulembera kalatayi. Ndikulemba ndikudziwa kuti udzachita ngakhale kuposa zimene ndakupemphazi.
I Tillid til din Lydighed skriver jeg til dig, idet jeg ved, at du vil gøre endog mere end det, jeg siger.
22 Chinthu chinanso ndi ichi: undikonzere malo, chifukwa ndikukhulupirira kuti Mulungu adzamvera mapemphero anu ndi kundibwezera kwa inu.
Men med det samme bered også Herberge for mig; thi jeg håber, at jeg ved eders Bønner skal skænkes eder.
23 Epafra, wamʼndende mnzanga chifukwa cha Khristu Yesu akupereka moni.
Epafras, min medfangne i Kristus Jesus,
24 Atumiki anzanga awa, Marko, Aristariko, Dema ndi Luka, akuperekanso moni.
Markus, Aristarkus, Demas, Lukas, mine Medarbejdere, hilse dig.
25 Chisomo cha Ambuye Yesu Khristu chikhale ndi mzimu wako.
Vor Herres Jesu Kristi Nåde være med eders Ånd!