< Filemoni 1 >

1 Kuchokera kwa Paulo, amene ndili mʼndende chifukwa cha Khristu Yesu ndi Timoteyo mʼbale wathu. Kulembera Filemoni, bwenzi lathu lokondedwa ndi mtumiki mnzathu.
Paul, the prisoner of Jesus Christ, and brother Timothy, to Philemon the beloved also our fellow-laborer,
2 Kwa Apiya mlongo wathu, Arkipo msilikali mnzathu, ndiponso mpingo umene umasonkhana mʼnyumba mwanu.
and to sister Apphia, and Archippus our fellow-soldier, and the church in your house.
3 Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale ndi inu.
Grace to you and peace from God our Father and the Lord Jesus Christ.
4 Ine ndimayamika Mulungu wanga nthawi zonse ndikakukumbukira iwe mʼmapemphero anga.
I give thanks to my God always, making mention of you in my prayers,
5 Pakuti ndamva za chikondi chako, za chikhulupiriro chako mwa Ambuye Yesu ndiponso za chikondi chako pa oyera mtima onse.
hearing about your divine love, and the faith which you have toward the Lord Jesus, and all the saints;
6 Ine ndikupemphera kuti mgwirizano wako ndi ife mʼchikhulupiriro ukhale opindulitsa pozamitsa nzeru zako zozindikira zinthu zilizonse zabwino zimene timagawana chifukwa cha Khristu.
in order that the fellowship of your faith may be efficient in the perfect knowledge of every good thing which is in you toward Christ.
7 Mʼbale, chikondi chako chandipatsa chimwemwe chachikulu ndi chilimbikitso, chifukwa umatsitsimutsa mitima ya anthu a Ambuye.
For I had much joy and consolation over your divine love, because the affections of the saints have been refreshed by you, O brother.
8 Tsopano ngakhale kuti mwa Khristu nditha kulimba mtima ndi kulamulira kuti uchite zimene uyenera kuchita,
Therefore, having much boldness in Christ to command you to that which is appropriate,
9 komabe ndikupempha mwachikondi. Ine Paulo, munthu wokalamba, ndipo tsopano ndili mʼndende chifukwa cha Khristu Yesu,
on account of the divine love, I the more exhort you, being such as Paul the aged, and now also the prisoner of Jesus Christ.
10 ndikukupempha chifukwa cha mwana wanga Onesimo, amene ndamubala ndili mu unyolo.
I exhort you concerning my son, whom I begat in my bonds, Onesimus,
11 Anali wopanda phindu kwa iwe, koma tsopano wasanduka wa phindu kwa iwe ndi kwa inenso.
him at one time unprofitable to you, but now profitable both to you and to me: whom I have sent back to you,
12 Ine ndikumutumizanso kwa iwe tsopano, koma potero ndikukhala ngati ndikutumiza mtima wanga weniweni.
him, that is my own heart.
13 Ndikanakonda ndikanakhala naye kuno kuti iyeyo azinditumikira mʼmalo mwako pamene ndili mu unyolo chifukwa cha Uthenga Wabwino.
Whom I did wish to have with me, in order that he might minister unto me in your stead in the bonds of the gospel:
14 Koma sindikufuna kuchita kanthu osakufunsa, nʼcholinga chakuti chilichonse chabwino ungandichitire chikhale mwakufuna kwako osati mokakamiza.
but without your consent I did not wish to do anything; in order that your good might not be by constraint, but by the free will:
15 Mwina chifukwa chimene unasiyana naye kwa kanthawi ndi chakuti ukhale nayenso nthawi zonse. (aiōnios g166)
for on this account he suddenly departed from you for an hour, that you might have him back forever; (aiōnios g166)
16 Osati ngati kapolo, koma woposa kapolo, ngati mʼbale wokondedwa. Iyeyu ndi wokondedwa kwambiri kwa ine koma kwa iweyo ndi wokondedwa koposa, ngati munthu komanso ngati mʼbale mwa Ambuye.
no longer as a slave, but more than a slave, a brother beloved, especially to me, and much more to you, both in the flesh and in the Lord:
17 Tsono ngati umati ndine mnzako, umulandire iyeyu monga momwe ukanandilandirira ineyo.
if then you have me a comrade, receive him as myself.
18 Ngati anakulakwira kapena kukongola kanthu kalikonse, ndidzalipira ineyo.
If he has wronged you as to anything, or owes you anything, charge this to me.
19 Ine, Paulo ndikulemba zimenezi ndi dzanja langa. Ine ndidzalipira. Nʼkosafunika kukukumbutsa kuti iweyo ngongole yako kwa ine ndi moyo wakowo.
I Paul have written with my own hand, I will pay it: not that I may say to you that you even owe yourself to me.
20 Mʼbale, ndikufuna kuti ndipindule nawe mwa Ambuye; tsono tsitsimutsa mtima wanga mwa Khristu.
Yea, brother, let me rejoice over you in the Lord: refresh my heart in Christ.
21 Ine ndili ndi chitsimikizo cha kumvera kwako pamene ndikukulembera kalatayi. Ndikulemba ndikudziwa kuti udzachita ngakhale kuposa zimene ndakupemphazi.
Having confidence in your obedience I have written to you, knowing that you will do even more than those things which I say.
22 Chinthu chinanso ndi ichi: undikonzere malo, chifukwa ndikukhulupirira kuti Mulungu adzamvera mapemphero anu ndi kundibwezera kwa inu.
And at the same time also prepare for me a lodging: for I hope that through your prayers I will be consigned unto you.
23 Epafra, wamʼndende mnzanga chifukwa cha Khristu Yesu akupereka moni.
Epaphras, my fellow-soldier in Christ Jesus;
24 Atumiki anzanga awa, Marko, Aristariko, Dema ndi Luka, akuperekanso moni.
Mark, Aristarchus, Demas, Luke, my fellow-workers, salute you.
25 Chisomo cha Ambuye Yesu Khristu chikhale ndi mzimu wako.
The grace of the Lord Jesus Christ be with your spirit.

< Filemoni 1 >