< Obadiya 1 >

1 Masomphenya a Obadiya. Ambuye Yehova akunena kwa Edomu kuti, Tamva uthenga wochokera kwa Yehova: Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu kukanena kuti, “Konzekani, tiyeni tikachite nkhondo ndi Edomu.”
KA wanana a Obadia. Peneia ka Iehova ka Haku i olelo mai ai no Edoma; Ua lohe kakou i ka lohe ana mai Iehova mai, Ua hoounaia'ku ka elele iwaena o na lahuikanaka; E ku oukou iluna, a e ala ku e kakou ia ia i ke kaua.
2 “Taona, ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina; udzanyozedwa kwambiri.
Aia hoi, ua hoolilo au ia oe i mea uuku iwaena o na lahuikanaka; Ua lilo oe i mea hoowahawaha loa ia.
3 Kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa, iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe ndipo umamanga nyumba zako pa mapiri ataliatali, iwe amene umanena mu mtima mwako kuti, ‘Ndani anganditsitse pansi?’
Ua hoopunipuni ka haaheo o kou naau ia oe, E ka mea e noho ana ma na ana o ka pohaku, He wahi kiekie kou noho ana; E olelo ana ma kou naau, Na wai la au e lawe iho ilalo i ka honua?
4 Koma ngakhale umawuluka ngati chiwombankhanga ndi kumanga chisa chako pakati pa nyenyezi, ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,” akutero Yehova.
Ina e hookiekie oe ia oe iho e like me ka aeto, Ina e hoonoho i kou punana iwaena o na hoku, Malaila mai e lawe iho ai au ia oe ilalo, wahi a Iehova.
5 “Anthu akuba akanabwera kwa iwe, kapena anthu olanda zinthu akanafika usiku, aa, tsoka lanji limene likukudikira iwe! Kodi akanangotengako zimene akuzifuna zokha? Ngati anthu othyola mphesa akanafika, kodi akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha?
Ina i hele mai na aihue i ou la, ina he poe powa i ka po, (Nani kou lukuia!) aole anei lakou e aihue, a pau ko lakou makemake? Ina i hele mai na ohi waina i ou la, aole anei lakou e waiho aku i ke koena?
6 Koma Esau adzalandidwa zinthu zonse, chuma chake chobisika chidzabedwa!
Nani ka imiia o ka Esau! I huliia hoi kona mau wahi huna!
7 Anthu onse ogwirizana nawo adzakupirikitsira kumalire; abwenzi ako adzakunyenga ndi kukugonjetsa; amene amadya chakudya chako adzakutchera msampha, koma iwe sudzazindikira zimenezi.”
O na kanaka a pau o kau berita, ua hoouna aku lakou ia oe a i ka palena; O na kanaka e kuikahi ana me oe, ua wahahee lakou ia oe, a ua lanakila lakou maluna ou; O ka poe e ai ana i kau berena, ua waiho lakou i ka hei malalo iho ou; Aohe naauao iloko ona.
8 Yehova akunena kuti, “Tsiku limenelo, kodi sindidzawononga anthu onse anzeru a ku Edomu, anthu odziwa zinthu mʼmapiri a Esau?
Aole anei au e luku aku i ka poe ike, mai Edoma aku ia la, wahi a Iehova, A me ka naauao mai ka mauna o Esau aku?
9 Ankhondo ako, iwe Temani, adzachita mantha, ndipo aliyense amene ali mʼphiri la Esau adzaphedwa pa nkhondo.
A e weliweli kou poe kanaka ikaika, e Temana, I okiiak'u kela kanaka keia kanaka, mai ka mauna o Esau aku.
10 Chifukwa cha nkhanza zimene unachitira mʼbale wako Yakobo, udzakhala wamanyazi; adzakuwononga mpaka muyaya.
No ka luku ana a no ka hana ino i kou hoahanau ia Iakoba, e uhi mai ka hilahila ia oe, A e luku loa ia'ku oe.
11 Pamene adani ankamulanda chuma chake pamene alendo analowa pa zipata zake ndi kuchita maere pa Yerusalemu, pa tsikulo iwe unali ngati mmodzi wa iwo.
I ka la i ku ai oe ma kela aoao, I ka la i lawe pio aku ai na malihini i kona ikaika, A komo ko na aina e iloko o kona mau pukapa, A hailona lakou no Ierusalema, Ua like hoi oe me kekahi o lakou.
12 Iwe sunayenera kunyoza mʼbale wako pa nthawi ya tsoka lake, kapena kunyogodola Ayuda chifukwa cha chiwonongeko chawo, kapena kuwaseka pa nthawi ya mavuto awo.
Aole nae i pono kou nana ana i ka la o kou hoahanau, I ka la o kona malihini ana; Aole hoi he pono kou hauoli ana maluna o na mamo a Iuda, I ka la i lukuia'i lakou; Aole pono kau olelo hookiekie ana i ka wa i pilikia'i lakou.
13 Iwe sunayenera kudutsa pa zipata za anthu anga pa nthawi ya masautso awo, kapena kuwanyogodola pa tsiku la tsoka lawo, kapena kulanda chuma chawo pa nthawi ya masautso awo.
Aole pono kou komo ana iloko o ka puka o ko'u poe kanaka, i ka la o ko lakou make; Aohe pono kou nana ana i ko lakou poino i ka la i make ai lakou, A me kou kau ana i kou lima maluna o kona waiwai i ka la o kona lukuia ana.
14 Sunayenera kudikirira pamphambano ya misewu kuti uphe Ayuda othawa, kapena kuwapereka kwa adani awo Ayuda opulumuka pa nthawi ya mavuto awo.”
Aohe pono kou ku ana ma ka huina alanui e oki aku i kona poe i pakele; Aohe pono kou haawi lilo ana i kona poe i koe, i ka la pilikia.
15 “Tsiku la Yehova layandikira limene adzaweruza mitundu yonse ya anthu. Adzakuchitira zomwe unawachitira ena; zochita zako zidzakubwerera wekha.
No ka mea, ua kokoke mai ka la o Iehova maluna o na lahuikanaka a pau: Like me kau i hana aku ai, pela e hanaia mai ai oe: O kau hoopai ana, e hoihoiia mai ia maluna o kou poo.
16 Iwe unamwa pa phiri langa loyera, koteronso mitundu ina yonse idzamwa kosalekeza; iwo adzamwa ndi kudzandira ndipo adzayiwalika pa mbiri ya dziko lapansi.
No ka mea, like me oukou i inu ai maluna o ko'u mauna hoano, Pela e inu mau ai na lahuikanaka a pau; A e inu lakou, a e moni iho, A e like auanei lakou me na mea ole.
17 Koma pa Phiri la Ziyoni padzakhala chipulumutso; phirilo lidzakhala lopatulika, ndipo nyumba ya Yakobo idzalandira cholowa chake.
Aka, ma ka mauna o Ziona he mea e pakele ai, a he mea laa; A e loaa i ko ka hale o Iakoba ko lakou noho ana.
18 Nyumba ya Yakobo idzasanduka moto ndipo nyumba ya Yosefe idzasanduka lawi la moto; nyumba ya Esau idzasanduka chiputu, ndipo adzayitenthe pa moto ndi kuyipsereza. Sipadzakhala anthu opulumuka kuchokera mʼnyumba ya Esau.” Yehova wayankhula.
A lilo ko ka hale o Iakoba i ahi, A o ko ka hale o Iosepa i lapalapa; A o ko ka hale o Esau i opala, A e hoaa iwaena o lakou, a e hoopau ia lakou; Aohe mea e koe ana o ko ka hale o Esau; No ka mea, o Iehova ka i olelo mai.
19 Anthu ochokera ku Negevi adzakhala ku mapiri a Esau, ndipo anthu ochokera mʼmbali mwa mapiri adzatenga dziko la Afilisti. Adzakhala mʼminda ya Efereimu ndi Samariya, ndipo Benjamini adzatenga Giliyadi.
A e loaa i ko ke kukuluhema ka mauna o Esau, A i ko ka papu ko Pilisetia: A e lilo no lakou ka aina o Eperaima, a me ka aina o Samaria; A e lilo o Gileada no Beniamina.
20 Aisraeli amene ali ku ukapolo adzalandira dziko la Kanaani mpaka ku Zarefati; a ku Yerusalemu amene ali ku ukapolo ku Sefaradi adzalandira mizinda ya ku Negevi.
A o ka poe pio o keia poe kaua o na mamo a Iseraela, e lilo no lakou ko Kanaana a hiki i Zarepata; A o ka poe pio no Ierusalema ma Separada, e lilo no lakou na kulanakauhale o ke kukuluhema.
21 Opulumukawo adzapita ku Phiri la Ziyoni ndipo adzalamulira mapiri a Esau. Koma ufumuwo udzakhala wa Yehova.
A e pii mai na mea hoola ma ka mauna Ziona, e hoopai i ka mauna o Esau; A e lilo ke aupuni no Iehova.

< Obadiya 1 >