< Obadiya 1 >
1 Masomphenya a Obadiya. Ambuye Yehova akunena kwa Edomu kuti, Tamva uthenga wochokera kwa Yehova: Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu kukanena kuti, “Konzekani, tiyeni tikachite nkhondo ndi Edomu.”
La vision d'Abdias. Ainsi a dit le Seigneur l'Eternel touchant Edom: Nous avons ouï une publication de par l'Eternel, et un Envoyé a été dépêché parmi les nations, [et elles ont dit]: Courage levons-nous contre lui pour le combattre.
2 “Taona, ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina; udzanyozedwa kwambiri.
Voici, je te rendrai petit entre les nations, tu seras fort méprisé.
3 Kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa, iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe ndipo umamanga nyumba zako pa mapiri ataliatali, iwe amene umanena mu mtima mwako kuti, ‘Ndani anganditsitse pansi?’
L'orgueil de ton cœur t'a séduit, toi qui habites dans les fentes des rochers, qui sont ta haute demeure, et qui dis en ton cœur: Qui est-ce qui me renversera par terre?
4 Koma ngakhale umawuluka ngati chiwombankhanga ndi kumanga chisa chako pakati pa nyenyezi, ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,” akutero Yehova.
Quand tu aurais élevé ton nid comme l'aigle, et quand même tu l'aurais mis entre les étoiles, je te jetterai de là par terre, dit l'Eternel.
5 “Anthu akuba akanabwera kwa iwe, kapena anthu olanda zinthu akanafika usiku, aa, tsoka lanji limene likukudikira iwe! Kodi akanangotengako zimene akuzifuna zokha? Ngati anthu othyola mphesa akanafika, kodi akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha?
Sont-ce des larrons qui sont entrés chez toi, ou des voleurs de nuit? Comment [donc] as-tu été rasé? N'eussent-ils pas dérobé jusqu'à ce qu'ils en eussent eu assez? Si des vendangeurs fussent entrés chez toi, n'eussent-ils pas laissé quelque grappillage?
6 Koma Esau adzalandidwa zinthu zonse, chuma chake chobisika chidzabedwa!
Comment a été fouillé Esaü? Comment ont été examinés ses lieux secrets?
7 Anthu onse ogwirizana nawo adzakupirikitsira kumalire; abwenzi ako adzakunyenga ndi kukugonjetsa; amene amadya chakudya chako adzakutchera msampha, koma iwe sudzazindikira zimenezi.”
Tous tes alliés t'ont conduit jusqu'à la frontière; ceux qui étaient en paix avec toi t'ont trompé, et ont eu le dessus sur toi; ceux [qui mangeaient] ton pain t'ont donné le coup par-dessous, sans qu'on l'aperçût.
8 Yehova akunena kuti, “Tsiku limenelo, kodi sindidzawononga anthu onse anzeru a ku Edomu, anthu odziwa zinthu mʼmapiri a Esau?
Ne sera-ce pas en ce temps-là, dit l'Eternel, que je ferai périr les sages au milieu d'Edom, et la prudence dans la montagne d'Esaü?
9 Ankhondo ako, iwe Temani, adzachita mantha, ndipo aliyense amene ali mʼphiri la Esau adzaphedwa pa nkhondo.
Tes hommes forts seront aussi étonnés, ô Téman! afin que les hommes soient retranchés de la montagne d'Esaü, à force de les [y] tuer.
10 Chifukwa cha nkhanza zimene unachitira mʼbale wako Yakobo, udzakhala wamanyazi; adzakuwononga mpaka muyaya.
La honte te couvrira, et tu seras retranché pour jamais, à cause de la violence [faite] à ton frère Jacob.
11 Pamene adani ankamulanda chuma chake pamene alendo analowa pa zipata zake ndi kuchita maere pa Yerusalemu, pa tsikulo iwe unali ngati mmodzi wa iwo.
Lorsque tu te tenais vis-à-vis quand les étrangers menaient son armée en captivité, et que les forains entraient dans ses portes, et qu'ils jetaient le sort sur Jérusalem, tu étais aussi comme l'un d'eux.
12 Iwe sunayenera kunyoza mʼbale wako pa nthawi ya tsoka lake, kapena kunyogodola Ayuda chifukwa cha chiwonongeko chawo, kapena kuwaseka pa nthawi ya mavuto awo.
Mais tu ne devais pas prendre plaisir à voir la journée de ton frère quand il a été livré aux étrangers, et tu ne devais pas te réjouir sur les enfants de Juda au jour qu'ils ont été détruits, et tu ne [les] devais pas braver au jour de la détresse.
13 Iwe sunayenera kudutsa pa zipata za anthu anga pa nthawi ya masautso awo, kapena kuwanyogodola pa tsiku la tsoka lawo, kapena kulanda chuma chawo pa nthawi ya masautso awo.
Et tu ne devais pas entrer dans la porte de mon peuple au jour de sa calamité, et tu ne devais pas prendre plaisir, toi, dis-je, à voir son mal au jour de sa calamité, et [tes mains] ne se devaient pas avancer sur son bien, au jour de sa calamité.
14 Sunayenera kudikirira pamphambano ya misewu kuti uphe Ayuda othawa, kapena kuwapereka kwa adani awo Ayuda opulumuka pa nthawi ya mavuto awo.”
Et tu ne te devais pas tenir sur les passages, pour exterminer ses réchappés; ni livrer ceux qui étaient restés, au jour de la détresse.
15 “Tsiku la Yehova layandikira limene adzaweruza mitundu yonse ya anthu. Adzakuchitira zomwe unawachitira ena; zochita zako zidzakubwerera wekha.
Car la journée de l'Eternel est proche sur toutes les nations; comme tu as fait, il te sera ainsi fait; ta récompense retournera sur ta tête.
16 Iwe unamwa pa phiri langa loyera, koteronso mitundu ina yonse idzamwa kosalekeza; iwo adzamwa ndi kudzandira ndipo adzayiwalika pa mbiri ya dziko lapansi.
Car comme vous avez bu sur la montagne de ma sainteté [la coupe de ma fureur], ainsi toutes les nations [la] boiront sans interruption; oui, elles [la] boiront, et [l']avaleront, et elles seront comme si elles n'avaient point été.
17 Koma pa Phiri la Ziyoni padzakhala chipulumutso; phirilo lidzakhala lopatulika, ndipo nyumba ya Yakobo idzalandira cholowa chake.
Mais il y aura des réchappés sur la montagne de Sion, et elle sera sainte, et la maison de Jacob possédera ses possessions.
18 Nyumba ya Yakobo idzasanduka moto ndipo nyumba ya Yosefe idzasanduka lawi la moto; nyumba ya Esau idzasanduka chiputu, ndipo adzayitenthe pa moto ndi kuyipsereza. Sipadzakhala anthu opulumuka kuchokera mʼnyumba ya Esau.” Yehova wayankhula.
Et la maison de Jacob sera un feu, et la maison de Joseph une flamme, et la maison d'Esaü du chaume; ils s'allumeront parmi eux, et les consumeront; et il n'y aura rien de reste dans la maison d'Esaü; car l'Eternel a parlé.
19 Anthu ochokera ku Negevi adzakhala ku mapiri a Esau, ndipo anthu ochokera mʼmbali mwa mapiri adzatenga dziko la Afilisti. Adzakhala mʼminda ya Efereimu ndi Samariya, ndipo Benjamini adzatenga Giliyadi.
Ils posséderont le Midi, [savoir] la montagne d'Esaü; et la campagne, [savoir] les Philistins, et ils posséderont le territoire d'Ephraïm, et le territoire de Samarie; et Benjamin [possédera] Galaad.
20 Aisraeli amene ali ku ukapolo adzalandira dziko la Kanaani mpaka ku Zarefati; a ku Yerusalemu amene ali ku ukapolo ku Sefaradi adzalandira mizinda ya ku Negevi.
Et ces bandes des enfants d'Israël qui auront été transportés, [posséderont] ce qui était des Cananéens, jusqu'à Sarepta; et ceux de Jérusalem qui auront été transportés, [posséderont] ce qui [est] jusqu'à Sépharad, ils le posséderont avec les villes du Midi.
21 Opulumukawo adzapita ku Phiri la Ziyoni ndipo adzalamulira mapiri a Esau. Koma ufumuwo udzakhala wa Yehova.
Car les libérateurs monteront en la montagne de Sion, pour juger la montagne d'Esaü; et le Royaume sera à l'Eternel.