< Obadiya 1 >

1 Masomphenya a Obadiya. Ambuye Yehova akunena kwa Edomu kuti, Tamva uthenga wochokera kwa Yehova: Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu kukanena kuti, “Konzekani, tiyeni tikachite nkhondo ndi Edomu.”
Obadias's Syn. Så siger den Herre HERREN til Edom: Fra HERREN har jeg hørt en Tidende: Et Bud er sendt ud blandt Folkene: Rejs jer til Kamp imod det!
2 “Taona, ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina; udzanyozedwa kwambiri.
Se, ringe har jeg gjort dig blandt Folkene, såre foragtet er du.
3 Kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa, iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe ndipo umamanga nyumba zako pa mapiri ataliatali, iwe amene umanena mu mtima mwako kuti, ‘Ndani anganditsitse pansi?’
Dit Hjertes Hovmod bedrog dig, du, som bor i Klippekløft, som troner i det høje og siger i Hjertet: "Hvo kan styrte mig til Jorden?"
4 Koma ngakhale umawuluka ngati chiwombankhanga ndi kumanga chisa chako pakati pa nyenyezi, ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,” akutero Yehova.
Bygger du end højt som Ørnen, er end din Rede blandt Stjerner, jeg styrter dig ned derfra, så lyder det fra HERREN.
5 “Anthu akuba akanabwera kwa iwe, kapena anthu olanda zinthu akanafika usiku, aa, tsoka lanji limene likukudikira iwe! Kodi akanangotengako zimene akuzifuna zokha? Ngati anthu othyola mphesa akanafika, kodi akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha?
Du skulde vel ikke have Tyve til Gæster, natlige Voldsmænd? Hvor er du lagt øde; de stjæler jo alt, hvad de lyster! Du skulde vel ikke have Høstmænd i Vingården? Efterslæt levner de ikke!
6 Koma Esau adzalandidwa zinthu zonse, chuma chake chobisika chidzabedwa!
Hvor blev dog Esau ransaget, hans Skatte opsporet!
7 Anthu onse ogwirizana nawo adzakupirikitsira kumalire; abwenzi ako adzakunyenga ndi kukugonjetsa; amene amadya chakudya chako adzakutchera msampha, koma iwe sudzazindikira zimenezi.”
Alle dine Forbundsfæller jog dig lige til Grænsen, dine gode Venner sveg dig, tog Magten fra dig; for at skræmme dig lagde de Fælder under din Fod.
8 Yehova akunena kuti, “Tsiku limenelo, kodi sindidzawononga anthu onse anzeru a ku Edomu, anthu odziwa zinthu mʼmapiri a Esau?
Visselig vil jeg på hin Dag, lyder det fra HERREN, udrydde de vise af Edom og Klogskab af Esaus Bjerge.
9 Ankhondo ako, iwe Temani, adzachita mantha, ndipo aliyense amene ali mʼphiri la Esau adzaphedwa pa nkhondo.
Da skal dine Helte lammes at Rædsel, o Teman, og hver en Mand ryddes ud at Esaus Bjerge.
10 Chifukwa cha nkhanza zimene unachitira mʼbale wako Yakobo, udzakhala wamanyazi; adzakuwononga mpaka muyaya.
For Drab og Vold mod din Broder Jakob skal du skjules af Skam; udryddes skal du for evigt,
11 Pamene adani ankamulanda chuma chake pamene alendo analowa pa zipata zake ndi kuchita maere pa Yerusalemu, pa tsikulo iwe unali ngati mmodzi wa iwo.
fordi du så til, da fremmede raned hans Gods og Udlændinge kom i bans Porte; da de lodded Jerusalem bort, var og du som en af dem.
12 Iwe sunayenera kunyoza mʼbale wako pa nthawi ya tsoka lake, kapena kunyogodola Ayuda chifukwa cha chiwonongeko chawo, kapena kuwaseka pa nthawi ya mavuto awo.
At nyde din Broders Dag, hans Vanhelds Dag, og glæde dig over Judæerne på Undergangens Dag! At opspærre Munden på Trængselens Dag,
13 Iwe sunayenera kudutsa pa zipata za anthu anga pa nthawi ya masautso awo, kapena kuwanyogodola pa tsiku la tsoka lawo, kapena kulanda chuma chawo pa nthawi ya masautso awo.
komme i mit Folks Port på Ulykkens Dag, være med til at nyde dets Kval på Ulykkens Dag, gribe efter dets Gods på Ulykkens Dag!
14 Sunayenera kudikirira pamphambano ya misewu kuti uphe Ayuda othawa, kapena kuwapereka kwa adani awo Ayuda opulumuka pa nthawi ya mavuto awo.”
At stå ved Dalenes Munding og dræbe de undslupne, prisgive dem, som slap bort, på Trængselens Dag!
15 “Tsiku la Yehova layandikira limene adzaweruza mitundu yonse ya anthu. Adzakuchitira zomwe unawachitira ena; zochita zako zidzakubwerera wekha.
Thi nær er HERRENs Dag over alle Folkene; som du har gjort, skal der gøres med dig, Gengæld kommer over dit Hoved.
16 Iwe unamwa pa phiri langa loyera, koteronso mitundu ina yonse idzamwa kosalekeza; iwo adzamwa ndi kudzandira ndipo adzayiwalika pa mbiri ya dziko lapansi.
Thi som I drak på mit hellige Bjerg, skal alle Folkene drikke uden Ophør; de skal drikke og rave og blive, som om de aldrig havde været til.
17 Koma pa Phiri la Ziyoni padzakhala chipulumutso; phirilo lidzakhala lopatulika, ndipo nyumba ya Yakobo idzalandira cholowa chake.
Men på Zions Bjerg skal der være Frelse, og det skal være en Helligdom, og Jakobs Hus skal tage sine Ejendomme i Eje.
18 Nyumba ya Yakobo idzasanduka moto ndipo nyumba ya Yosefe idzasanduka lawi la moto; nyumba ya Esau idzasanduka chiputu, ndipo adzayitenthe pa moto ndi kuyipsereza. Sipadzakhala anthu opulumuka kuchokera mʼnyumba ya Esau.” Yehova wayankhula.
Jakobs Hus skal blive en Ild og Josefs Hus en Lue, men Esaus Hus skal blive Strå, og de skal sætte Ild derpå og fortære det, og ingen af Esaus Hus skal undslippe, så sandt HERREN har talet.
19 Anthu ochokera ku Negevi adzakhala ku mapiri a Esau, ndipo anthu ochokera mʼmbali mwa mapiri adzatenga dziko la Afilisti. Adzakhala mʼminda ya Efereimu ndi Samariya, ndipo Benjamini adzatenga Giliyadi.
De skal tage Sydlandet i Eje sammen med Esaus Bjerge og Lavlandet sammen med Filisterne; deskal tage Efraims Mark i Eje sammen med Samarias Mark og Ammoniterne sammen med Gilead.
20 Aisraeli amene ali ku ukapolo adzalandira dziko la Kanaani mpaka ku Zarefati; a ku Yerusalemu amene ali ku ukapolo ku Sefaradi adzalandira mizinda ya ku Negevi.
Og de landflygtige i Hala og Habor skal tage Kana'anæernes Land i Eje indtil Zarepta, og de landflygtige fra Jerusalem, som er i Sefarad, skal tage Sydlandets Byer i Eje.
21 Opulumukawo adzapita ku Phiri la Ziyoni ndipo adzalamulira mapiri a Esau. Koma ufumuwo udzakhala wa Yehova.
Da drager Redningsmænd fra Zions Bjerg op for at holde Dom over Esaus Bjerge. Og så skal Riget være HERRENs.

< Obadiya 1 >