< Obadiya 1 >
1 Masomphenya a Obadiya. Ambuye Yehova akunena kwa Edomu kuti, Tamva uthenga wochokera kwa Yehova: Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu kukanena kuti, “Konzekani, tiyeni tikachite nkhondo ndi Edomu.”
Vision d’Abdias. Voici ce que dit le Seigneur Dieu à Edom: [Nous avons entendu une nouvelle venant du Seigneur; et il a envoyé un messager vers les nations: Levez-vous, et levons-nous ensemble contre lui pour le combat].
2 “Taona, ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina; udzanyozedwa kwambiri.
Voici que je t’ai placé très petit parmi les nations, tu es fort méprisable.
3 Kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa, iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe ndipo umamanga nyumba zako pa mapiri ataliatali, iwe amene umanena mu mtima mwako kuti, ‘Ndani anganditsitse pansi?’
L’orgueil de ton cœur t’a élevé, toi habitant dans les fentes des rochers, exaltant ton trône; toi qui dis dans ton cœur: Qui me fera descendre à terre?
4 Koma ngakhale umawuluka ngati chiwombankhanga ndi kumanga chisa chako pakati pa nyenyezi, ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,” akutero Yehova.
Si tu t’élèves comme l’aigle, et que parmi les astres tu poses ton nid, je t’en ferai descendre, dit le Seigneur.
5 “Anthu akuba akanabwera kwa iwe, kapena anthu olanda zinthu akanafika usiku, aa, tsoka lanji limene likukudikira iwe! Kodi akanangotengako zimene akuzifuna zokha? Ngati anthu othyola mphesa akanafika, kodi akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha?
Si des voleurs, si des brigands étaient entrés chez toi durant la nuit, comment aurais-tu gardé le silence? N’auraient-ils pas volé ce qui leur suffisait? Si des vendangeurs étaient entrés chez toi, est-ce qu’ils ne t’auraient pas laissé au moins une grappe de raisin?
6 Koma Esau adzalandidwa zinthu zonse, chuma chake chobisika chidzabedwa!
Comment les ennemis ont-ils fouillé Esaü, fureté dans ce qu’il avait de caché?
7 Anthu onse ogwirizana nawo adzakupirikitsira kumalire; abwenzi ako adzakunyenga ndi kukugonjetsa; amene amadya chakudya chako adzakutchera msampha, koma iwe sudzazindikira zimenezi.”
Ils t’ont éconduit jusqu’à la frontière; tous tes alliés se sont joués de toi; les hommes qui vivaient en paix avec toi ont prévalu contre toi; ceux qui mangent ton pain dresseront des embûches sous tes pas; il n’y a pas de prudence en lui.
8 Yehova akunena kuti, “Tsiku limenelo, kodi sindidzawononga anthu onse anzeru a ku Edomu, anthu odziwa zinthu mʼmapiri a Esau?
N’est-ce pas en ce jour-là, dit le Seigneur, que je perdrai les sages de l’Idumée et bannirai la prudence de la montagne d’Esaü?
9 Ankhondo ako, iwe Temani, adzachita mantha, ndipo aliyense amene ali mʼphiri la Esau adzaphedwa pa nkhondo.
Et ils craindront, tes braves du midi, que l’homme de la montagne d’Esaü ne périsse.
10 Chifukwa cha nkhanza zimene unachitira mʼbale wako Yakobo, udzakhala wamanyazi; adzakuwononga mpaka muyaya.
À cause de tes meurtres et à cause de ton iniquité contre Jacob ton frère, la confusion te couvrira, et tu périras pour jamais.
11 Pamene adani ankamulanda chuma chake pamene alendo analowa pa zipata zake ndi kuchita maere pa Yerusalemu, pa tsikulo iwe unali ngati mmodzi wa iwo.
Au jour que tu t’élevais contre lui, quand des ennemis se rendaient maîtres de son armée, et que des étrangers entraient dans ses portes, et que sur Jérusalem ils jetaient le sort, toi aussi tu étais comme l’un d’entre eux.
12 Iwe sunayenera kunyoza mʼbale wako pa nthawi ya tsoka lake, kapena kunyogodola Ayuda chifukwa cha chiwonongeko chawo, kapena kuwaseka pa nthawi ya mavuto awo.
Et tu ne mépriseras pas ton frère en son jour malheureux, au jour de son exil, et tu ne te réjouiras pas sur les fils de Juda au jour de leur ruine; et tu ne parleras pas orgueilleusement au jour de l’angoisse.
13 Iwe sunayenera kudutsa pa zipata za anthu anga pa nthawi ya masautso awo, kapena kuwanyogodola pa tsiku la tsoka lawo, kapena kulanda chuma chawo pa nthawi ya masautso awo.
Et tu n’entreras pas dans la porte de mon peuple au jour de leur ruine; et tu ne les mépriseras pas, toi non plus, au milieu de ses maux, au jour de sa désolation; et tu ne seras pas envoyé contre son armée au jour de sa désolation.
14 Sunayenera kudikirira pamphambano ya misewu kuti uphe Ayuda othawa, kapena kuwapereka kwa adani awo Ayuda opulumuka pa nthawi ya mavuto awo.”
Et tu ne te tiendras pas dans les carrefours, afin de tuer ceux qui fuiront, et tu n’enfermeras pas les restes de ses habitants au jour de la tribulation.
15 “Tsiku la Yehova layandikira limene adzaweruza mitundu yonse ya anthu. Adzakuchitira zomwe unawachitira ena; zochita zako zidzakubwerera wekha.
Parce que le jour du Seigneur est près d’éclater sur toutes les nations; comme tu as fait, il te sera fait; ce que tu leur as fait, il le fera retomber sur ta tête.
16 Iwe unamwa pa phiri langa loyera, koteronso mitundu ina yonse idzamwa kosalekeza; iwo adzamwa ndi kudzandira ndipo adzayiwalika pa mbiri ya dziko lapansi.
Car comme vous avez bu sur ma montagne sainte, toutes les nations boiront sans discontinuer; et elles boiront, elles avaleront, et elles seront comme si elles n’étaient point.
17 Koma pa Phiri la Ziyoni padzakhala chipulumutso; phirilo lidzakhala lopatulika, ndipo nyumba ya Yakobo idzalandira cholowa chake.
Mais sur la montagne de Sion sera le salut et elle sera sainte: la maison de Jacob possédera ceux qui l’avaient possédée.
18 Nyumba ya Yakobo idzasanduka moto ndipo nyumba ya Yosefe idzasanduka lawi la moto; nyumba ya Esau idzasanduka chiputu, ndipo adzayitenthe pa moto ndi kuyipsereza. Sipadzakhala anthu opulumuka kuchokera mʼnyumba ya Esau.” Yehova wayankhula.
Et la maison de Jacob sera un feu, et la maison de Joseph une flamme, et la maison d’Esaü une paille; et ils l’embraseront, et ils la dévoreront, et il n’y aura pas de restes de la maison d’Esaü, parce que le Seigneur a parlé.
19 Anthu ochokera ku Negevi adzakhala ku mapiri a Esau, ndipo anthu ochokera mʼmbali mwa mapiri adzatenga dziko la Afilisti. Adzakhala mʼminda ya Efereimu ndi Samariya, ndipo Benjamini adzatenga Giliyadi.
Et ceux qui sont au midi hériteront de la montagne d’Esaü; et ceux qui sont dans les plaines assujettiront les Philistins; et ils posséderont la contrée d’Ephraïm et la contrée de Samarie, et Benjamin possédera Galaad.
20 Aisraeli amene ali ku ukapolo adzalandira dziko la Kanaani mpaka ku Zarefati; a ku Yerusalemu amene ali ku ukapolo ku Sefaradi adzalandira mizinda ya ku Negevi.
Et les exilés de cette armée des enfants d’Israël posséderont tous les lieux des Chananéens jusqu’à Sarepta; et les exilés de Jérusalem, qui sont sur le Bosphore, posséderont les cités du midi.
21 Opulumukawo adzapita ku Phiri la Ziyoni ndipo adzalamulira mapiri a Esau. Koma ufumuwo udzakhala wa Yehova.
Et les libérateurs monteront sur la montagne de Sion pour juger la montagne d’Esaü; et le règne sera au Seigneur.