< Obadiya 1 >

1 Masomphenya a Obadiya. Ambuye Yehova akunena kwa Edomu kuti, Tamva uthenga wochokera kwa Yehova: Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu kukanena kuti, “Konzekani, tiyeni tikachite nkhondo ndi Edomu.”
La vision d'Abdias. Voici ce que dit le Seigneur Yahvé au sujet d'Édom. Nous avons entendu des nouvelles de Yahvé, et un ambassadeur est envoyé parmi les nations, disant: « Levez-vous, et levons-nous contre elle dans la bataille.
2 “Taona, ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina; udzanyozedwa kwambiri.
Voici, je t'ai rendu petit parmi les nations. Tu es grandement méprisée.
3 Kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa, iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe ndipo umamanga nyumba zako pa mapiri ataliatali, iwe amene umanena mu mtima mwako kuti, ‘Ndani anganditsitse pansi?’
L'orgueil de ton cœur t'a trompé, toi qui habites dans les fentes du rocher, dont la demeure est élevée, et qui dis en son cœur: Qui me fera descendre à terre?
4 Koma ngakhale umawuluka ngati chiwombankhanga ndi kumanga chisa chako pakati pa nyenyezi, ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,” akutero Yehova.
Tu as beau monter comme l'aigle, et ton nid est placé parmi les étoiles, je t'en ferai descendre, dit Yahvé.
5 “Anthu akuba akanabwera kwa iwe, kapena anthu olanda zinthu akanafika usiku, aa, tsoka lanji limene likukudikira iwe! Kodi akanangotengako zimene akuzifuna zokha? Ngati anthu othyola mphesa akanafika, kodi akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha?
« Si des voleurs venaient chez toi, si des brigands de nuit - oh, quel désastre t'attend - ne voleraient-ils pas seulement jusqu'à ce qu'ils en aient assez? Si des vendangeurs venaient chez toi, ne laisseraient-ils pas des raisins à glaner?
6 Koma Esau adzalandidwa zinthu zonse, chuma chake chobisika chidzabedwa!
Comme Esaü sera mis à sac! Comme on cherche ses trésors cachés!
7 Anthu onse ogwirizana nawo adzakupirikitsira kumalire; abwenzi ako adzakunyenga ndi kukugonjetsa; amene amadya chakudya chako adzakutchera msampha, koma iwe sudzazindikira zimenezi.”
Tous les hommes de ton alliance t'ont conduit sur ton chemin, jusqu'à la frontière. Les hommes qui étaient en paix avec toi t'ont trompé, et ont prévalu contre toi. Les amis qui mangent ton pain te tendent un piège. Il n'y a pas d'intelligence en lui. »
8 Yehova akunena kuti, “Tsiku limenelo, kodi sindidzawononga anthu onse anzeru a ku Edomu, anthu odziwa zinthu mʼmapiri a Esau?
« Ne détruirai-je pas en ce jour-là, dit Yahvé, les sages d'Édom et l'intelligence de la montagne d'Ésaü?
9 Ankhondo ako, iwe Temani, adzachita mantha, ndipo aliyense amene ali mʼphiri la Esau adzaphedwa pa nkhondo.
Tes vaillants hommes, Teman, seront consternés, au point que tous seront retranchés de la montagne d'Ésaü par le massacre.
10 Chifukwa cha nkhanza zimene unachitira mʼbale wako Yakobo, udzakhala wamanyazi; adzakuwononga mpaka muyaya.
A cause de la violence faite à ton frère Jacob, la honte te couvrira, et tu seras retranché pour toujours.
11 Pamene adani ankamulanda chuma chake pamene alendo analowa pa zipata zake ndi kuchita maere pa Yerusalemu, pa tsikulo iwe unali ngati mmodzi wa iwo.
Le jour où tu t'es tenu à l'écart, le jour où des étrangers ont emporté ses biens, où des étrangers sont entrés dans ses portes et ont tiré au sort Jérusalem, toi aussi tu as été comme l'un d'eux.
12 Iwe sunayenera kunyoza mʼbale wako pa nthawi ya tsoka lake, kapena kunyogodola Ayuda chifukwa cha chiwonongeko chawo, kapena kuwaseka pa nthawi ya mavuto awo.
Mais ne méprise pas ton frère au jour de son malheur, et ne te réjouis pas des fils de Juda au jour de leur ruine. Ne t'enorgueillis pas au jour de la détresse.
13 Iwe sunayenera kudutsa pa zipata za anthu anga pa nthawi ya masautso awo, kapena kuwanyogodola pa tsiku la tsoka lawo, kapena kulanda chuma chawo pa nthawi ya masautso awo.
N'entre pas dans la porte de mon peuple au jour de son malheur. Ne méprise pas leur détresse au jour de leur calamité, et ne t'empare pas de leurs biens au jour de leur calamité.
14 Sunayenera kudikirira pamphambano ya misewu kuti uphe Ayuda othawa, kapena kuwapereka kwa adani awo Ayuda opulumuka pa nthawi ya mavuto awo.”
Ne te tiens pas aux carrefours pour couper la route à ceux qui s'échappent. Ne livre pas ceux d'entre eux qui restent au jour de la détresse.
15 “Tsiku la Yehova layandikira limene adzaweruza mitundu yonse ya anthu. Adzakuchitira zomwe unawachitira ena; zochita zako zidzakubwerera wekha.
Car le jour de Yahvé est proche de toutes les nations! Ce que vous avez fait, il vous sera fait. Tes actes retomberont sur ta propre tête.
16 Iwe unamwa pa phiri langa loyera, koteronso mitundu ina yonse idzamwa kosalekeza; iwo adzamwa ndi kudzandira ndipo adzayiwalika pa mbiri ya dziko lapansi.
Car, comme vous avez bu sur ma montagne sainte, toutes les nations boiront sans cesse. Oui, elles boiront, elles avaleront, et elles seront comme si elles n'avaient pas été.
17 Koma pa Phiri la Ziyoni padzakhala chipulumutso; phirilo lidzakhala lopatulika, ndipo nyumba ya Yakobo idzalandira cholowa chake.
Mais sur la montagne de Sion, il y aura ceux qui échapperont, et elle sera sainte. La maison de Jacob possédera ses biens.
18 Nyumba ya Yakobo idzasanduka moto ndipo nyumba ya Yosefe idzasanduka lawi la moto; nyumba ya Esau idzasanduka chiputu, ndipo adzayitenthe pa moto ndi kuyipsereza. Sipadzakhala anthu opulumuka kuchokera mʼnyumba ya Esau.” Yehova wayankhula.
La maison de Jacob sera un feu, la maison de Joseph une flamme, et la maison d'Ésaü un chaume. Ils brûleront au milieu d'eux et les dévoreront. Il ne restera rien à la maison d'Ésaü. » En effet, Yahvé a parlé.
19 Anthu ochokera ku Negevi adzakhala ku mapiri a Esau, ndipo anthu ochokera mʼmbali mwa mapiri adzatenga dziko la Afilisti. Adzakhala mʼminda ya Efereimu ndi Samariya, ndipo Benjamini adzatenga Giliyadi.
Ceux du Sud posséderont la montagne d'Ésaü, et ceux de la plaine, les Philistins. Ils posséderont le champ d'Ephraïm et le champ de Samarie. Benjamin possédera Galaad.
20 Aisraeli amene ali ku ukapolo adzalandira dziko la Kanaani mpaka ku Zarefati; a ku Yerusalemu amene ali ku ukapolo ku Sefaradi adzalandira mizinda ya ku Negevi.
Les captifs de cette armée des enfants d'Israël, qui sont chez les Cananéens, posséderont jusqu'à Zarephath; et les captifs de Jérusalem, qui sont à Sépharad, posséderont les villes du Néguev.
21 Opulumukawo adzapita ku Phiri la Ziyoni ndipo adzalamulira mapiri a Esau. Koma ufumuwo udzakhala wa Yehova.
Des sauveurs monteront sur la montagne de Sion pour juger les montagnes d'Ésaü, et le royaume sera à Yahvé.

< Obadiya 1 >