< Numeri 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai, mu tenti ya msonkhano, pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, mʼchaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, kuti,
Och Herren talade med Mose, i Sinai öken, uti vittnesbördsens tabernakel, på första dagen, i den andra månadenom, i de andra årena, sedan de voro gångne utur Egypti land, och sade:
2 “Werengani Aisraeli onse mʼmafuko awo ndi mʼmabanja awo, lemba dzina la munthu wamwamuna aliyense, mmodzimmodzi.
Tager en summo af hela Israels barnas menighet, efter deras slägter, och deras fäders hus och namn, allt det som mankön är, ifrå hufvud till hufvud;
3 Iwe ndi Aaroni mwawerenge mwa magulu awo mu Israeli, amuna onse a zaka makumi awiri zakubadwa ndi opitirirapo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali.
Ifrå tjugu år och derutöfver, allt det som doger till att draga i här i Israel. Och I skolen tälja dem efter deras härar, du och Aaron;
4 Munthu mmodzi wochokera ku fuko lililonse yemwe ndi mtsogoleri wa banja lake, ndiye akuthandizeni pa ntchitoyi.
Och skolen taga till eder af hvarjo slägtene en höfvitsman öfver hans faders hus.
5 Mayina a anthu amene akuthandizeniwo ndi awa: Elizuri mwana wa Sedeuri, kuchokera ku fuko la Rubeni,
Desse äro namnen af de höfvitsmän, som med eder stå skola. Af Ruben: Elizur, Sedeurs son.
6 Selumieli mwana wa Zurisadai, kuchokera ku fuko la Simeoni,
Af Simeon: Selumiel, ZuriSadai son.
7 Naasoni mwana wa Aminadabu, kuchokera ku fuko la Yuda,
Af Juda: Nahesson, Amminadabs son.
8 Netanieli mwana wa Zuwara, kuchokera ku fuko la Isakara,
Af Isaschar: Nethaneel, Zuars son.
9 Eliabu mwana wa Heloni, kuchokera ku fuko la Zebuloni,
Af Sebulon: Eliab, Helons son.
10 Mwa ana a Yosefe: kuchokera ku fuko la Efereimu, Elisama mwana wa Amihudi; kuchokera ku fuko la Manase, Gamalieli mwana wa Pedazuri;
Af Josephs barn: Af Ephraim, Elisama, Ammihuds son: Af Manasse, Gamliel, Pedahzurs son.
11 Abidani mwana wa Gideoni, kuchokera ku fuko la Benjamini,
Af BenJamin: Abidan, Gideoni son.
12 Ahiyezeri mwana wa Amisadai, kuchokera ku fuko la Dani,
Af Dan: Ahieser, Ammi Sadai son.
13 Pagieli mwana wa Okirani, kuchokera ku fuko la Aseri,
Af Asser: Pagiel, Ochrans son.
14 Eliyasafu mwana wa Deuweli, kuchokera ku fuko la Gadi,
Af Gad: Eliasaph, Deguels son.
15 Ahira mwana wa Enani, kuchokera ku fuko la Nafutali.”
Af Naphthali: Ahira, Enans son.
16 Amenewa ndi anthu amene anasankhidwa kuchokera mʼmagulu mwawo, eni mbumba a mafuko a makolo awo. Iwowa anali atsogoleri a mafuko a Israeli.
Desse äro de namnkunnigaste i menighetene, höfvitsmän i deras fäders slägter, som voro hufvud och Förstar i Israel.
17 Mose ndi Aaroni anatenga anthu amene mayina awo anaperekedwa,
Och Mose och Aaron togo dem till sig, såsom de vid namn uppräknade voro;
18 ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, anasonkhanitsa anthu onse pamodzi. Anthuwo anafotokoza za makolo awo mwa mafuko awo ndi mabanja awo. Ndipo mayina a amuna onse amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo analembedwa, mmodzimmodzi
Och församlade desslikes hela menighetena på första dagen i den andra månadenom, och räknade dem efter deras börd, efter deras slägter och fäders hus och namn, ifrå tjugu år och derutöfver, ifrå hufvud till hufvud;
19 monga momwe Yehova analamulira Mose. Motero iyeyo anawawerenga mʼchipululu cha Sinai:
Såsom Herren hade budit Mose; och talde dem uti Sinai öken.
20 Kuchokera mwa ana a Rubeni, mwana wamwamuna woyamba wa Israeli: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali, anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Rubens barn, som var den förste Israels son, efter deras börd, slägter, deras fäders hus och namn, ifrå hufvud till hufvud, allt det mankön var, ifrå tjugu år och derutöfver, och de som dogde till att draga i här,
21 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Rubeni chinali 46,500.
De vordo räknade intill Rubens slägte, sex och fyratio tusend, och femhundrad.
22 Kuchokera mwa zidzukulu za Simeoni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Simeons barn, efter deras börd, slägter, deras fäders hus och namn, ifrå hufvud till hufvud, allt det som mankön var, ifrå tjugu år och derutöfver, och i här draga dogde,
23 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Simeoni chinali 59,300.
Vordo talde intill Simeons slägte, nio och femtio tusend, och trehundrad.
24 Kuchokera mwa zidzukulu za Gadi: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Gads barn, efter deras börd, slägter, deras fäders hus och namn, ifrå tjugu år och derutöfver, allt det som i här draga dogde,
25 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Gadi chinali 45, 650.
Vordo talde intill Gads slägte, fem och fyratio tusend, sexhundrad och femtio.
26 Kuchokera mwa zidzukulu za Yuda: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Juda barn, efter deras börd, slägter, deras fäders hus och namn, ifrå tjugu år och derutöfver, allt det i här draga dogde,
27 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Yuda chinali 74, 600.
Vordo talde intill Juda slägte, fyra och sjutio tusend, och sexhundrad.
28 Kuchokera mwa zidzukulu za Isakara: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Isaschars barn, efter deras börd, slägter, deras fäders hus och namn, ifrå tjugu år och derutöfver, allt det i här draga dogde,
29 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Isakara chinali 54,400.
Vordo talde intill Isaschars slägte, fyra och femtio tusend, och fyrahundrad.
30 Kuchokera mwa zidzukulu za Zebuloni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Sebulons barn, efter deras börd, slägter, deras fäders hus och namn, ifrå tjugu år och derutöfver, allt det i här draga dogde,
31 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Zebuloni chinali 57,400.
Vordo talde intill Sebulons slägte, sju och femtio tusend, och fyrahundrad.
32 Kuchokera mwa ana aamuna a Yosefe: Kuchokera mwa zidzukulu za Efereimu: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Josephs barn, af Ephraim, efter deras börd, slägter, deras fäders hus och namn, ifrå tjugu år och derutöfver, allt det i här draga dogde,
33 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Efereimu chinali 40,500.
Vordo talde intill Ephraims slägte, fyratiotusend, och femhundrad.
34 Kuchokera mwa zidzukulu za Manase: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Manasse barn, efter deras börd, slägter, deras fäders hus och namn, ifrå tjugu år och derutöfver, allt det i här draga dogde,
35 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Manase chinali 32,200.
Vordo talde intill Manasse slägte, tu och tretio tusend, och tuhundrad.
36 Kuchokera mwa zidzukulu za Benjamini: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
BenJamins barn, efter deras börd, slägter, deras fäders hus och namn, ifrå tjugu år och derutöfver, allt det i här draga dogde,
37 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Benjamini chinali 35,400.
Vordo talde intill BenJamins slägte, fem och tretio tusend, och fyrahundrad.
38 Kuchokera mwa zidzukulu za Dani: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Dans barn, efter deras börd, slägter, deras fäders hus och namn, ifrå tjugu år och derutöfver, allt det i här draga dogde,
39 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Dani chinali 62,700.
Vordo talde intill Dans slägte, tu och sextio tusend, och sjuhundrad.
40 Kuchokera mwa zidzukulu za Aseri: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Assers barn, efter deras börd, slägter, deras fäders hus och namn, ifrå tjugu år och derutöfver, allt det i här draga dogde.
41 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Aseri chinali 41,500.
Vordo talde intill Assers slägte, ett och fyratio tusend, och femhundrad.
42 Kuchokera mwa zidzukulu za Nafutali: Aamuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Naphthali barn, efter deras börd, slägter, deras fäders hus och namn, ifrå tjugu år och derutöfver, allt det i här draga dogde,
43 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Nafutali chinali 53,400.
Vordo talde intill Naphthali slägte, tre och femtio tusend, och fyrahundrad.
44 Amenewa ndiwo anthu amene Mose ndi Aaroni anawawerenga mothandizidwa ndi atsogoleri khumi ndi awiri a Israeli, aliyense kuyimira fuko lake.
Desse äro de som Mose och Aaron, samt med de tolf Israels Förstar, talde, af hvilkom ju en var öfver hvart af deras fäders hus.
45 Aisraeli onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli anawawerenga monga mwa mabanja awo.
Och summan af Israels barn, efter deras fäders hus, ifrå tjugu år och derutöfver, det i här draga dogde i Israel,
46 Chiwerengero cha anthu onse pamodzi chinali 603,550.
Var sex resor hundradetusend, och tretusen, femhundrade och femtio.
47 Koma mabanja a fuko la Levi okha sanawawerenge pamodzi ndi ena.
Men de Leviter, efter deras fäders slägter, vordo intet räknade ibland med.
48 Pakuti Yehova anawuza Mose kuti,
Och Herren talade med Mose, och sade:
49 “Usawerenge fuko la Levi kapena kuliphatikiza mʼkawundula wa Aisraeli.
Levi slägt skall du intet räkna, eller taga någon summo af dem, ibland Israels barn.
50 Koma uyike Aleviwo kuti aziyangʼanira tenti yanga yopatulika, zipangizo zake ndi zonse zili mʼmenemo. Azinyamula tentiyo pamodzi ndi zipangizo zake zonse; azisamalira ndi kumanga misasa mozungulira tentiyo.
Men du skall skicka dem till vittnesbördsens tabernakel, och till all dess tyg, och allt det dertill hörer; och de skola bära tabernaklet, och all dess tyg, och skola det sköta, och lägra sig omkring tabernaklet.
51 Pamene akusamutsa tentiyo, Alevi ndiwo aziyitsitsa, akafuna kuyimanganso, Alevi ndiwo aziyimiritsa. Wina aliyense amene adzayandikire tentiyo adzaphedwa.
Och när man resa skall, då skola de Leviter taga tabernaklet neder; och när hären skall lägra sig, skola de slå tabernaklet upp. Om någor främmande nalkas dertill, han skall dö.
52 Aisraeli azimanga matenti awo mʼmagulumagulu, munthu aliyense ku gulu lake pansi pa mbendera yake.
Israels barn skola lägra sig hvar i sitt lägre, och vid sins härs baner.
53 Alevi nawonso, azimanga matenti awo mozungulira tenti yopatulika kuti chilango chisagwere Aisraeli onse. Ndipo Alevi aziyangʼanira ndi kusamalira tenti yopatulikayo.”
Men Leviterna skola lägra sig omkring vittnesbördsens tabernakel, på det icke skall komma en vrede öfver menighetena af Israels barn. Derföre skola de Leviter vakt hålla vid vittnesbördsens tabernakel.
54 Choncho Aisraeli anachita monga Yehova analamulira Mose.
Och Israels barn gjorde allt det Herren Mose budit hade.

< Numeri 1 >