< Numeri 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai, mu tenti ya msonkhano, pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, mʼchaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, kuti,
و در روز اول ماه دوم از سال دوم از بیرون آمدن ایشان از زمین مصر، خداوند دربیابان سینا در خیمه اجتماع موسی را خطاب کرده، گفت:۱
2 “Werengani Aisraeli onse mʼmafuko awo ndi mʼmabanja awo, lemba dzina la munthu wamwamuna aliyense, mmodzimmodzi.
«حساب تمامی جماعت بنی‌اسرائیل را برحسب قبایل و خاندان آبای ایشان، به شماره اسم های همه ذکوران موافق سرهای ایشان بگیرید.۲
3 Iwe ndi Aaroni mwawerenge mwa magulu awo mu Israeli, amuna onse a zaka makumi awiri zakubadwa ndi opitirirapo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali.
از بیست ساله و زیاده، هر‌که از اسرائیل به جنگ بیرون می‌رود، تو وهارون ایشان را برحسب افواج ایشان بشمارید.۳
4 Munthu mmodzi wochokera ku fuko lililonse yemwe ndi mtsogoleri wa banja lake, ndiye akuthandizeni pa ntchitoyi.
و همراه شما یک نفر از هر سبط باشد که هر یک رئیس خاندان آبایش باشد.۴
5 Mayina a anthu amene akuthandizeniwo ndi awa: Elizuri mwana wa Sedeuri, kuchokera ku fuko la Rubeni,
و اسم های کسانی که با شما باید بایستند، این است: از روبین، الیصوربن شدیئور.۵
6 Selumieli mwana wa Zurisadai, kuchokera ku fuko la Simeoni,
و از شمعون، شلومیئیل بن صوریشدای.۶
7 Naasoni mwana wa Aminadabu, kuchokera ku fuko la Yuda,
و از یهودا، نحشون بن عمیناداب.۷
8 Netanieli mwana wa Zuwara, kuchokera ku fuko la Isakara,
و از یساکار، نتنائیل بن صوغر.۸
9 Eliabu mwana wa Heloni, kuchokera ku fuko la Zebuloni,
و از زبولون، الیاب بن حیلون.۹
10 Mwa ana a Yosefe: kuchokera ku fuko la Efereimu, Elisama mwana wa Amihudi; kuchokera ku fuko la Manase, Gamalieli mwana wa Pedazuri;
و از بنی یوسف: از افرایم، الیشمع بن عمیهود. و از منسی، جملیئیل بن فدهصور.۱۰
11 Abidani mwana wa Gideoni, kuchokera ku fuko la Benjamini,
از بنیامین، ابیدان بن جدعونی.۱۱
12 Ahiyezeri mwana wa Amisadai, kuchokera ku fuko la Dani,
و از دان، اخیعزر بن عمیشدای.۱۲
13 Pagieli mwana wa Okirani, kuchokera ku fuko la Aseri,
و از اشیر، فجعیئیل بن عکران.۱۳
14 Eliyasafu mwana wa Deuweli, kuchokera ku fuko la Gadi,
و از جاد، الیاساف بن دعوئیل.۱۴
15 Ahira mwana wa Enani, kuchokera ku fuko la Nafutali.”
و از نفتالی، اخیرع بن عینان.»۱۵
16 Amenewa ndi anthu amene anasankhidwa kuchokera mʼmagulu mwawo, eni mbumba a mafuko a makolo awo. Iwowa anali atsogoleri a mafuko a Israeli.
اینانند دعوت‌شدگان جماعت و سروران اسباط آبای ایشان، و روسای هزاره های اسرائیل.۱۶
17 Mose ndi Aaroni anatenga anthu amene mayina awo anaperekedwa,
و موسی و هارون این کسان را که به نام، معین شدند، گرفتند.۱۷
18 ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, anasonkhanitsa anthu onse pamodzi. Anthuwo anafotokoza za makolo awo mwa mafuko awo ndi mabanja awo. Ndipo mayina a amuna onse amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo analembedwa, mmodzimmodzi
و در روز اول ماه دوم، تمامی جماعت را جمع کرده، نسب نامه های ایشان را برحسب قبایل و خاندان آبای ایشان، به شماره اسم‌ها از بیست ساله و بالاتر موافق سرهای ایشان خواندند.۱۸
19 monga momwe Yehova analamulira Mose. Motero iyeyo anawawerenga mʼchipululu cha Sinai:
چنانکه خداوندموسی را امر فرموده بود، ایشان را در بیابان سینابشمرد.۱۹
20 Kuchokera mwa ana a Rubeni, mwana wamwamuna woyamba wa Israeli: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali, anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
و اما انساب بنی روبین نخست زاده اسرائیل، برحسب قبایل و خاندان آبای ایشان، موافق نامها و سرهای ایشان این بود: هر ذکور ازبیست ساله و بالاتر، جمیع کسانی که برای جنگ بیرون می‌رفتند.۲۰
21 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Rubeni chinali 46,500.
شمرده شدگان ایشان از سبطروبین، چهل و شش هزار و پانصد نفر بودند.۲۱
22 Kuchokera mwa zidzukulu za Simeoni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
و انساب بنی شمعون برحسب قبایل وخاندان آبای ایشان، کسانی که از ایشان شمرده شدند، موافق شماره اسم‌ها و سرهای ایشان این بود: هر ذکور از بیست ساله و بالاتر، هر‌که برای جنگ بیرون می‌رفت.۲۲
23 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Simeoni chinali 59,300.
شمرده شدگان ایشان ازسبط شمعون، پنجاه و نه هزار و سیصد نفر بودند.۲۳
24 Kuchokera mwa zidzukulu za Gadi: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
و انساب بنی جاد برحسب قبایل و خاندان آبای ایشان، موافق شماره اسم‌ها، از بیست ساله وبالاتر، هر‌که برای جنگ بیرون می‌رفت.۲۴
25 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Gadi chinali 45, 650.
شمرده شدگان ایشان از سبط جاد، چهل و پنج هزار و ششصد و پنجاه نفر بودند.۲۵
26 Kuchokera mwa zidzukulu za Yuda: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
و انساب بنی یهودا برحسب قبایل وخاندان آبای ایشان، موافق شماره اسم‌ها ازبیست ساله و بالاتر، هر‌که برای جنگ بیرون می‌رفت.۲۶
27 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Yuda chinali 74, 600.
شمرده شدگان ایشان از سبط یهودا، هفتاد و چهار هزار و شش صد نفر بودند.۲۷
28 Kuchokera mwa zidzukulu za Isakara: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
و انساب بنی یساکار برحسب قبایل وخاندان آبای ایشان، موافق شماره اسم‌ها ازبیست ساله و بالاتر، هر‌که برای جنگ بیرون می‌رفت.۲۸
29 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Isakara chinali 54,400.
شمرده شدگان ایشان از سبط یساکار، پنجاه و چهار هزار و چهارصد نفر بودند.۲۹
30 Kuchokera mwa zidzukulu za Zebuloni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
و انساب بنی زبولون برحسب قبایل وخاندان آبای ایشان، موافق شماره اسم‌ها ازبیست ساله و بالاتر، هر‌که برای جنگ بیرون می‌رفت.۳۰
31 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Zebuloni chinali 57,400.
شمرده شدگان ایشان از سبط زبولون پنجاه و هفت هزار و چهارصد نفر بودند.۳۱
32 Kuchokera mwa ana aamuna a Yosefe: Kuchokera mwa zidzukulu za Efereimu: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
و انساب بنی یوسف از بنی افرایم برحسب قبایل و خاندان آبای ایشان، موافق شماره اسم هااز بیست ساله و بالاتر، هر‌که برای جنگ بیرون می‌رفت.۳۲
33 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Efereimu chinali 40,500.
شمرده شدگان ایشان از سبط افرایم، چهل هزار و پانصد نفر بودند.۳۳
34 Kuchokera mwa zidzukulu za Manase: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
و انساب بنی منسی برحسب قبایل وخاندان آبای ایشان، موافق شماره اسم‌ها، ازبیست ساله و بالاتر، هر‌که برای جنگ بیرون می‌رفت.۳۴
35 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Manase chinali 32,200.
شمرده شدگان ایشان از سبط منسی، سی و دو هزار و دویست نفر بودند.۳۵
36 Kuchokera mwa zidzukulu za Benjamini: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
و انساب بنی بنیامین برحسب قبایل وخاندان آبای ایشان، موافق شماره اسم‌ها، ازبیست ساله بالاتر، هر‌که برای جنگ بیرون می‌رفت.۳۶
37 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Benjamini chinali 35,400.
شمرده شدگان ایشان از سبط بنیامین، سی و پنج هزار و چهارصد نفر بودند.۳۷
38 Kuchokera mwa zidzukulu za Dani: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
و انساب بنی دان برحسب قبایل و خاندان آبای ایشان، موافق شماره اسم‌ها از بیست ساله وبالاتر، هر‌که برای جنگ می‌رفت.۳۸
39 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Dani chinali 62,700.
شمرده شدگان ایشان از سبط دان، شصت و دو هزار و هفتصد نفر بودند.۳۹
40 Kuchokera mwa zidzukulu za Aseri: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
و انساب بنی اشیر برحسب قبایل و خاندان آبای ایشان، موافق شماره اسم‌ها از بیست ساله وبالاتر، هر‌که برای جنگ بیرون می‌رفت.۴۰
41 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Aseri chinali 41,500.
شمرده شدگان ایشان از سبط اشیر، چهل ویک هزار و پانصد نفر بودند.۴۱
42 Kuchokera mwa zidzukulu za Nafutali: Aamuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
و انساب بنی نفتالی برحسب قبایل وخاندان آبای ایشان، موافق شماره اسم‌ها ازبیست ساله و بالاتر، هر‌که برای جنگ بیرون می‌رفت.۴۲
43 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Nafutali chinali 53,400.
شمرده شدگان ایشان از سبط نفتالی، پنجاه و سه هزار و پانصد نفر بودند.۴۳
44 Amenewa ndiwo anthu amene Mose ndi Aaroni anawawerenga mothandizidwa ndi atsogoleri khumi ndi awiri a Israeli, aliyense kuyimira fuko lake.
اینانند شمرده شدگانی که موسی و هارون با دوازده نفر از سروران اسرائیل، که یک نفر برای هر خاندان آبای ایشان بود، شمردند.۴۴
45 Aisraeli onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli anawawerenga monga mwa mabanja awo.
و تمامی شمرده شدگان بنی‌اسرائیل برحسب خاندان آبای ایشان، از بیست ساله و بالاتر، هر کس از اسرائیل که برای جنگ بیرون می‌رفت.۴۵
46 Chiwerengero cha anthu onse pamodzi chinali 603,550.
همه شمرده شدگان، ششصد و سه هزار و پانصد وپنجاه نفر بودند.۴۶
47 Koma mabanja a fuko la Levi okha sanawawerenge pamodzi ndi ena.
اما لاویان برحسب سبط آبای ایشان در میان آنها شمرده نشدند.۴۷
48 Pakuti Yehova anawuza Mose kuti,
زیرا خداوند موسی را خطاب کرده، گفت:۴۸
49 “Usawerenge fuko la Levi kapena kuliphatikiza mʼkawundula wa Aisraeli.
«اما سبط لاوی را مشمار و حساب ایشان را درمیان بنی‌اسرائیل مگیر.۴۹
50 Koma uyike Aleviwo kuti aziyangʼanira tenti yanga yopatulika, zipangizo zake ndi zonse zili mʼmenemo. Azinyamula tentiyo pamodzi ndi zipangizo zake zonse; azisamalira ndi kumanga misasa mozungulira tentiyo.
لیکن لاویان را برمسکن شهادت و تمامی اسبابش و بر هرچه علاقه به آن دارد بگمار، و ایشان مسکن و تمامی اسبابش را بردارند، و ایشان آن را خدمت نمایندو به اطراف مسکن خیمه زنند.۵۰
51 Pamene akusamutsa tentiyo, Alevi ndiwo aziyitsitsa, akafuna kuyimanganso, Alevi ndiwo aziyimiritsa. Wina aliyense amene adzayandikire tentiyo adzaphedwa.
و چون مسکن روانه شود لاویان آن را پایین بیاورند، و چون مسکن افراشته شود لاویان آن را برپا نمایند، وغریبی که نزدیک آن آید، کشته شود.۵۱
52 Aisraeli azimanga matenti awo mʼmagulumagulu, munthu aliyense ku gulu lake pansi pa mbendera yake.
و بنی‌اسرائیل هر کس در محله خود و هر کس نزدعلم خویش برحسب افواج خود، خیمه زنند.۵۲
53 Alevi nawonso, azimanga matenti awo mozungulira tenti yopatulika kuti chilango chisagwere Aisraeli onse. Ndipo Alevi aziyangʼanira ndi kusamalira tenti yopatulikayo.”
و لاویان به اطراف مسکن شهادت خیمه زنند، مبادا غضب بر جماعت بنی‌اسرائیل بشود، ولاویان شعائر مسکن شهادت را نگاه دارند.»۵۳
54 Choncho Aisraeli anachita monga Yehova analamulira Mose.
پس بنی‌اسرائیل چنین کردند، و برحسب آنچه خداوند موسی را امر فرموده بود، به عمل آوردند.۵۴

< Numeri 1 >