< Numeri 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai, mu tenti ya msonkhano, pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, mʼchaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, kuti,
Premye jou dezyèm mwa nan dezyèm lanne depi moun pèp Izrayèl yo te soti kite peyi Lejip la, antan yo te nan dezè Sinayi a, Seyè a pale ak Moyiz nan Tant Randevou a. Li di l' konsa:
2 “Werengani Aisraeli onse mʼmafuko awo ndi mʼmabanja awo, lemba dzina la munthu wamwamuna aliyense, mmodzimmodzi.
-Se pou ou menm ak Arawon, nou fè yon resansman pou konte tout moun nan pèp Izrayèl la, dapre fanmi yo, dapre branch fanmi yo. W'a pran non tout gason, yonn apre lòt.
3 Iwe ndi Aaroni mwawerenge mwa magulu awo mu Israeli, amuna onse a zaka makumi awiri zakubadwa ndi opitirirapo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali.
N'a konte tou sa ki gen ventan osinon ki pi gran, depi yo bon pou fè lagè. N'a fè resansman an dapre jan lame a òganize.
4 Munthu mmodzi wochokera ku fuko lililonse yemwe ndi mtsogoleri wa banja lake, ndiye akuthandizeni pa ntchitoyi.
N'a pran yon chèf nan chak branch fanmi, dapre zansèt yo, pou ede nou.
5 Mayina a anthu amene akuthandizeniwo ndi awa: Elizuri mwana wa Sedeuri, kuchokera ku fuko la Rubeni,
Men non moun ki va ede nou nan resansman an: Nan branch fanmi Woubenn lan, se va Elizou, pitit gason Chedeyou.
6 Selumieli mwana wa Zurisadai, kuchokera ku fuko la Simeoni,
Nan branch fanmi Simeyon an, se va Cheloumyèl, pitit gason Sourichadayi.
7 Naasoni mwana wa Aminadabu, kuchokera ku fuko la Yuda,
Nan branch fanmi Jida a, se va Nakchon, pitit gason Aminadab.
8 Netanieli mwana wa Zuwara, kuchokera ku fuko la Isakara,
Nan branch fanmi Isaka a, se va Netanèl, pitit gason Swa.
9 Eliabu mwana wa Heloni, kuchokera ku fuko la Zebuloni,
Nan branch fanmi Zabilon an, se va Eliyab, pitit gason Elon.
10 Mwa ana a Yosefe: kuchokera ku fuko la Efereimu, Elisama mwana wa Amihudi; kuchokera ku fuko la Manase, Gamalieli mwana wa Pedazuri;
Nan branch fanmi Efrayim, premye pitit gason Jozèf la, se va Elichama, pitit gason Amiyoud. Nan branch fanmi Manase, dezyèm pitit gason Jozèf la, se va Gamliyèl, pitit gason Pedachou.
11 Abidani mwana wa Gideoni, kuchokera ku fuko la Benjamini,
Nan branch fanmi Benjamen an, se va Abidan, pitit gason Gideyoni.
12 Ahiyezeri mwana wa Amisadai, kuchokera ku fuko la Dani,
Nan branch fanmi Dann lan, se va Ayezè, pitit gason Amichadayi.
13 Pagieli mwana wa Okirani, kuchokera ku fuko la Aseri,
Nan branch fanmi Asè a, se va Pagiyèl, pitit gason Okran.
14 Eliyasafu mwana wa Deuweli, kuchokera ku fuko la Gadi,
Nan branch fanmi Gad la, se va Elyasaf, pitit gason Dewèl.
15 Ahira mwana wa Enani, kuchokera ku fuko la Nafutali.”
Nan branch fanmi Neftali a, se va Ayira, pitit gason Enan.
16 Amenewa ndi anthu amene anasankhidwa kuchokera mʼmagulu mwawo, eni mbumba a mafuko a makolo awo. Iwowa anali atsogoleri a mafuko a Israeli.
Se moun sa yo yo te chwazi nan pèp la pou fè travay la. Se yo ki te chèf lakay yo, chèf branch fanmi zansèt yo.
17 Mose ndi Aaroni anatenga anthu amene mayina awo anaperekedwa,
Moyiz ak Arawon pran douz mesye Bondye te nonmen yo,
18 ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, anasonkhanitsa anthu onse pamodzi. Anthuwo anafotokoza za makolo awo mwa mafuko awo ndi mabanja awo. Ndipo mayina a amuna onse amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo analembedwa, mmodzimmodzi
yo reyini tout pèp la, premye jou dezyèm mwa a. Yo pran non tout moun dapre fanmi yo, dapre branch fanmi zansèt yo. Yo konte tout gason, yonn apre lòt, tou sa ki gen ventan osinon ki pi gran,
19 monga momwe Yehova analamulira Mose. Motero iyeyo anawawerenga mʼchipululu cha Sinai:
dapre lòd Seyè a te bay Moyiz la. Se nan dezè Sinayi a yo te fè resansman tout pèp la.
20 Kuchokera mwa ana a Rubeni, mwana wamwamuna woyamba wa Israeli: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali, anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Se konsa yo konte tout gason nan branch fanmi Woubenn, premye pitit Jakòb la, tou sa ki gen ventan ak tou sa ki pi gran epi ki bon pou fè lagè. Yo pran non yo yonn apre lòt, yo di pitit ki moun yo ye, dapre fanmi yo, dapre branch fanmi zansèt yo.
21 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Rubeni chinali 46,500.
Yo jwenn karannsimil senksan (46.500) gason pou branch fanmi Woubenn lan.
22 Kuchokera mwa zidzukulu za Simeoni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Yo fè menm bagay la tou pou tout lòt branch fanmi yo. Pou branch fanmi Simeyon an,
23 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Simeoni chinali 59,300.
yo jwenn senkantnèfmil twasan (59.300) gason.
24 Kuchokera mwa zidzukulu za Gadi: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Pou branch fanmi Gad la,
25 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Gadi chinali 45, 650.
yo jwenn karannsenkmil sisansenkant (45.650) gason.
26 Kuchokera mwa zidzukulu za Yuda: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Pou branch fanmi Jida a,
27 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Yuda chinali 74, 600.
yo jwenn swasannkatòzmil sisan (74.600) gason.
28 Kuchokera mwa zidzukulu za Isakara: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Pou branch fanmi Isaka a,
29 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Isakara chinali 54,400.
yo jwenn senkannkatmil katsan (54.400) gason.
30 Kuchokera mwa zidzukulu za Zebuloni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Pou branch fanmi Zabilon an,
31 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Zebuloni chinali 57,400.
yo jwenn senkannsètmil katsan (57.400) gason.
32 Kuchokera mwa ana aamuna a Yosefe: Kuchokera mwa zidzukulu za Efereimu: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Pou branch fanmi Efrayim, premye pitit gason Jozèf la,
33 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Efereimu chinali 40,500.
yo jwenn karantmil senksan (40.500) gason.
34 Kuchokera mwa zidzukulu za Manase: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Pou branch fanmi Manase, dezyèm pitit gason Jozèf la,
35 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Manase chinali 32,200.
yo jwenn tranndemil desan (32.200) gason.
36 Kuchokera mwa zidzukulu za Benjamini: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Pou branch fanmi Benjamen an,
37 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Benjamini chinali 35,400.
yo jwenn trannsenkmil katsan (35.400) gason.
38 Kuchokera mwa zidzukulu za Dani: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Pou branch fanmi Dann lan,
39 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Dani chinali 62,700.
yo jwenn swasanndemil sètsan (62.700) gason.
40 Kuchokera mwa zidzukulu za Aseri: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Pou branch fanmi Asè a,
41 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Aseri chinali 41,500.
yo jwenn karanteyenmil senksan (41.500) gason.
42 Kuchokera mwa zidzukulu za Nafutali: Aamuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Pou branch fanmi Neftali a,
43 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Nafutali chinali 53,400.
yo jwenn senkanntwamil katsan (53.400) gason.
44 Amenewa ndiwo anthu amene Mose ndi Aaroni anawawerenga mothandizidwa ndi atsogoleri khumi ndi awiri a Israeli, aliyense kuyimira fuko lake.
Se non tout moun sa yo Moyiz ak Arawon te pran lè sa a. Te gen douz chèf, yonn pou chak branch fanmi pèp Izrayèl la, ki t'ap ede yo nan travay la.
45 Aisraeli onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli anawawerenga monga mwa mabanja awo.
Pou tout branch fanmi yo ansanm,
46 Chiwerengero cha anthu onse pamodzi chinali 603,550.
yo jwenn sisantwamil senksansenkant (603.550) gason.
47 Koma mabanja a fuko la Levi okha sanawawerenge pamodzi ndi ena.
Men yo pa t' fè resansman branch fanmi Levi a ansanm ak lòt branch fanmi yo,
48 Pakuti Yehova anawuza Mose kuti,
paske Seyè a te di Moyiz konsa:
49 “Usawerenge fuko la Levi kapena kuliphatikiza mʼkawundula wa Aisraeli.
-Ou pa bezwen fè resansman branch fanmi Levi a. Ou pa bezwen konte moun fanmi Levi yo ansanm ak rès moun pèp Izrayèl yo.
50 Koma uyike Aleviwo kuti aziyangʼanira tenti yanga yopatulika, zipangizo zake ndi zonse zili mʼmenemo. Azinyamula tentiyo pamodzi ndi zipangizo zake zonse; azisamalira ndi kumanga misasa mozungulira tentiyo.
Men, w'a mete moun fanmi Levi yo reskonsab Tant Randevou a ak tou sa ki ladan l' ansanm ak tou sa ki pou li. Se yo ki pou pote l' ansanm ak tou sa ki ladan l'. Se yo ki pou sèvi ladan l' epi yo gen pou yo moute kay yo fè wonn Tant Randevou a.
51 Pamene akusamutsa tentiyo, Alevi ndiwo aziyitsitsa, akafuna kuyimanganso, Alevi ndiwo aziyimiritsa. Wina aliyense amene adzayandikire tentiyo adzaphedwa.
Lè pou Tant Bondye a deplase, se moun fanmi Levi yo ki va demoute l'. Lè yo rive kote pou yo rete a, se moun fanmi Levi yo ki va moute l' tou. Nenpòt lòt moun ki pa nan branch fanmi Levi a epi ki ta pwoche bò tant lan, se pou yo touye l'.
52 Aisraeli azimanga matenti awo mʼmagulumagulu, munthu aliyense ku gulu lake pansi pa mbendera yake.
Lòt moun pèp Izrayèl yo menm va moute tant yo apa, chak fanmi ansanm bò làbanyè yo, dapre pozisyon yo nan lame a.
53 Alevi nawonso, azimanga matenti awo mozungulira tenti yopatulika kuti chilango chisagwere Aisraeli onse. Ndipo Alevi aziyangʼanira ndi kusamalira tenti yopatulikayo.”
Men, moun fanmi Levi yo va moute kay yo fè wonn Tant Randevou a pou kòlè Bondye pa tonbe sou pèp Izrayèl la. Se yo menm tou ki la pou veye sou Tant Randevou a.
54 Choncho Aisraeli anachita monga Yehova analamulira Mose.
Moun pèp Izrayèl yo te fè tou sa Seyè a te bay Moyiz lòd fè a. Se konsa yo te fè l' vre.

< Numeri 1 >