< Numeri 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai, mu tenti ya msonkhano, pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, mʼchaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, kuti,
Adonai spoke to Moses [Drawn out] in the wilderness of Sinai [Thorn], in the Tent of Meeting, on the first day of the second month, in the second year after they had come out of the land of Egypt [Abode of slavery], saying,
2 “Werengani Aisraeli onse mʼmafuko awo ndi mʼmabanja awo, lemba dzina la munthu wamwamuna aliyense, mmodzimmodzi.
“Take a census of all the congregation of the children of Israel [God prevails], by their families, by their fathers’ houses, according to the number of the names, every male, one by one;
3 Iwe ndi Aaroni mwawerenge mwa magulu awo mu Israeli, amuna onse a zaka makumi awiri zakubadwa ndi opitirirapo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali.
from twenty years old and upward, all who are able to go out to war in Israel [God prevails]. You and Aaron [Light-bringer] shall count them by their divisions.
4 Munthu mmodzi wochokera ku fuko lililonse yemwe ndi mtsogoleri wa banja lake, ndiye akuthandizeni pa ntchitoyi.
With you there shall be a man of every tribe; everyone head of his fathers’ house.
5 Mayina a anthu amene akuthandizeniwo ndi awa: Elizuri mwana wa Sedeuri, kuchokera ku fuko la Rubeni,
These are the names of the men who shall stand with you: Of Reuben [See, a son!]: Elizur the son of Shedeur.
6 Selumieli mwana wa Zurisadai, kuchokera ku fuko la Simeoni,
Of Simeon [Hearing]: Shelumiel the son of Zurishaddai [My rock almighty].
7 Naasoni mwana wa Aminadabu, kuchokera ku fuko la Yuda,
Of Judah [Praised]: Nahshon the son of Amminadab.
8 Netanieli mwana wa Zuwara, kuchokera ku fuko la Isakara,
Of Issachar [Hire, Reward]: Nethanel the son of Zuar.
9 Eliabu mwana wa Heloni, kuchokera ku fuko la Zebuloni,
Of Zebulun [Living together]: Eliab the son of Helon.
10 Mwa ana a Yosefe: kuchokera ku fuko la Efereimu, Elisama mwana wa Amihudi; kuchokera ku fuko la Manase, Gamalieli mwana wa Pedazuri;
Of the children of Joseph [May he add]: Of Ephraim [Fruit]: Elishama the son of Ammihud. Of Manasseh [Causing to forget]: Gamaliel the son of Pedahzur.
11 Abidani mwana wa Gideoni, kuchokera ku fuko la Benjamini,
Of Benjamin [Son of right hand, Son of south]: Abidan the son of Gideoni.
12 Ahiyezeri mwana wa Amisadai, kuchokera ku fuko la Dani,
Of Dan [He judged]: Ahiezer the son of Ammishaddai.
13 Pagieli mwana wa Okirani, kuchokera ku fuko la Aseri,
Of Asher [Happy]: Pagiel the son of Ochran.
14 Eliyasafu mwana wa Deuweli, kuchokera ku fuko la Gadi,
Of Gad [Good fortune]: Eliasaph the son of Deuel.
15 Ahira mwana wa Enani, kuchokera ku fuko la Nafutali.”
Of Naphtali [My wrestling]: Ahira the son of Enan.”
16 Amenewa ndi anthu amene anasankhidwa kuchokera mʼmagulu mwawo, eni mbumba a mafuko a makolo awo. Iwowa anali atsogoleri a mafuko a Israeli.
These are those who were called of the congregation, the princes of the tribes of their fathers; they were the heads of the thousands of Israel [God prevails].
17 Mose ndi Aaroni anatenga anthu amene mayina awo anaperekedwa,
Moses [Drawn out] and Aaron [Light-bringer] took these men who are mentioned by name.
18 ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, anasonkhanitsa anthu onse pamodzi. Anthuwo anafotokoza za makolo awo mwa mafuko awo ndi mabanja awo. Ndipo mayina a amuna onse amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo analembedwa, mmodzimmodzi
They assembled all the congregation together on the first day of the second month; and they declared their ancestry by their families, by their fathers’ houses, according to the number of the names, from twenty years old and upward, one by one.
19 monga momwe Yehova analamulira Mose. Motero iyeyo anawawerenga mʼchipululu cha Sinai:
As Adonai enjoined Moses [Drawn out], so he counted them in the wilderness of Sinai [Thorn].
20 Kuchokera mwa ana a Rubeni, mwana wamwamuna woyamba wa Israeli: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali, anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
The children of Reuben [See, a son!], Israel [God prevails]’s firstborn, their generations, by their families, by their fathers’ houses, according to the number of the names, one by one, every male from twenty years old and upward, all who were able to go out to war;
21 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Rubeni chinali 46,500.
those who were counted of them, of the tribe of Reuben [See, a son!], were forty-six thousand five hundred.
22 Kuchokera mwa zidzukulu za Simeoni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the children of Simeon [Hearing], their generations, by their families, by their fathers’ houses, those who were counted of it, according to the number of the names, one by one, every male from twenty years old and upward, all who were able to go out to war;
23 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Simeoni chinali 59,300.
those who were counted of them, of the tribe of Simeon [Hearing], were fifty-nine thousand three hundred.
24 Kuchokera mwa zidzukulu za Gadi: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the children of Gad [Good fortune], their generations, by their families, by their fathers’ houses, according to the number of the names, from twenty years old and upward, all who were able to go out to war;
25 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Gadi chinali 45, 650.
those who were counted of them, of the tribe of Gad [Good fortune], were forty-five thousand six hundred fifty.
26 Kuchokera mwa zidzukulu za Yuda: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the children of Judah [Praised], their generations, by their families, by their fathers’ houses, according to the number of the names, from twenty years old and upward, all who were able to go out to war;
27 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Yuda chinali 74, 600.
those who were counted of them, of the tribe of Judah [Praised], were seventy-four thousand six hundred.
28 Kuchokera mwa zidzukulu za Isakara: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the children of Issachar [Hire, Reward], their generations, by their families, by their fathers’ houses, according to the number of the names, from twenty years old and upward, all who were able to go out to war;
29 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Isakara chinali 54,400.
those who were counted of them, of the tribe of Issachar [Hire, Reward], were fifty-four thousand four hundred.
30 Kuchokera mwa zidzukulu za Zebuloni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the children of Zebulun [Living together], their generations, by their families, by their fathers’ houses, according to the number of the names, from twenty years old and upward, all who were able to go out to war;
31 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Zebuloni chinali 57,400.
those who were counted of them, of the tribe of Zebulun [Living together], were fifty-seven thousand four hundred.
32 Kuchokera mwa ana aamuna a Yosefe: Kuchokera mwa zidzukulu za Efereimu: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the children of Joseph [May he add], of the children of Ephraim [Fruit], their generations, by their families, by their fathers’ houses, according to the number of the names, from twenty years old and upward, all who were able to go out to war;
33 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Efereimu chinali 40,500.
those who were counted of them, of the tribe of Ephraim [Fruit], were forty thousand five hundred.
34 Kuchokera mwa zidzukulu za Manase: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the children of Manasseh [Causing to forget], their generations, by their families, by their fathers’ houses, according to the number of the names, from twenty years old and upward, all who were able to go out to war;
35 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Manase chinali 32,200.
those who were counted of them, of the tribe of Manasseh [Causing to forget], were thirty-two thousand two hundred.
36 Kuchokera mwa zidzukulu za Benjamini: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the children of Benjamin [Son of right hand, Son of south], their generations, by their families, by their fathers’ houses, according to the number of the names, from twenty years old and upward, all who were able to go out to war;
37 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Benjamini chinali 35,400.
those who were counted of them, of the tribe of Benjamin [Son of right hand, Son of south], were thirty-five thousand four hundred.
38 Kuchokera mwa zidzukulu za Dani: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the children of Dan [He judged], their generations, by their families, by their fathers’ houses, according to the number of the names, from twenty years old and upward, all who were able to go out to war;
39 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Dani chinali 62,700.
those who were counted of them, of the tribe of Dan [He judged], were sixty-two thousand seven hundred.
40 Kuchokera mwa zidzukulu za Aseri: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the children of Asher [Happy], their generations, by their families, by their fathers’ houses, according to the number of the names, from twenty years old and upward, all who were able to go out to war;
41 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Aseri chinali 41,500.
those who were counted of them, of the tribe of Asher [Happy], were forty-one thousand five hundred.
42 Kuchokera mwa zidzukulu za Nafutali: Aamuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the children of Naphtali [My wrestling], their generations, by their families, by their fathers’ houses, according to the number of the names, from twenty years old and upward, all who were able to go out to war;
43 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Nafutali chinali 53,400.
those who were counted of them, of the tribe of Naphtali [My wrestling], were fifty-three thousand four hundred.
44 Amenewa ndiwo anthu amene Mose ndi Aaroni anawawerenga mothandizidwa ndi atsogoleri khumi ndi awiri a Israeli, aliyense kuyimira fuko lake.
These are those who were counted, whom Moses [Drawn out] and Aaron [Light-bringer] counted, and the princes of Israel [God prevails], being twelve men: they were each one for his fathers’ house.
45 Aisraeli onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli anawawerenga monga mwa mabanja awo.
So all those who were counted of the children of Israel [God prevails] by their fathers’ houses, from twenty years old and upward, all who were able to go out to war in Israel [God prevails];
46 Chiwerengero cha anthu onse pamodzi chinali 603,550.
even all those who were counted were six hundred three thousand five hundred fifty.
47 Koma mabanja a fuko la Levi okha sanawawerenge pamodzi ndi ena.
But the Levites [Descendants of United with] after the tribe of their fathers was not counted among them.
48 Pakuti Yehova anawuza Mose kuti,
For Adonai spoke to Moses [Drawn out], saying,
49 “Usawerenge fuko la Levi kapena kuliphatikiza mʼkawundula wa Aisraeli.
“Only the tribe of Levi [United with] you shall not count, neither shall you take a census of them among the children of Israel [God prevails];
50 Koma uyike Aleviwo kuti aziyangʼanira tenti yanga yopatulika, zipangizo zake ndi zonse zili mʼmenemo. Azinyamula tentiyo pamodzi ndi zipangizo zake zonse; azisamalira ndi kumanga misasa mozungulira tentiyo.
but appoint the Levites [Descendants of United with] over the Tabernacle of the Testimony, and over all its furnishings, and over all that belongs to it. They shall carry the tabernacle, and all its furnishings; and they shall take care of it, and shall encamp around it.
51 Pamene akusamutsa tentiyo, Alevi ndiwo aziyitsitsa, akafuna kuyimanganso, Alevi ndiwo aziyimiritsa. Wina aliyense amene adzayandikire tentiyo adzaphedwa.
When the tabernacle is to move, the Levites [Descendants of United with] shall take it down; and when the tabernacle is to be set up, the Levites [Descendants of United with] shall set it up. The stranger who comes near shall be put to death.
52 Aisraeli azimanga matenti awo mʼmagulumagulu, munthu aliyense ku gulu lake pansi pa mbendera yake.
The children of Israel [God prevails] shall pitch their tents, every man by his own camp, and every man by his own standard, according to their divisions.
53 Alevi nawonso, azimanga matenti awo mozungulira tenti yopatulika kuti chilango chisagwere Aisraeli onse. Ndipo Alevi aziyangʼanira ndi kusamalira tenti yopatulikayo.”
But the Levites [Descendants of United with] shall encamp around the Tabernacle of the Testimony, that there may be no wrath on the congregation of the children of Israel [God prevails]: and the Levites [Descendants of United with] shall be responsible for the Tabernacle of the Testimony.”
54 Choncho Aisraeli anachita monga Yehova analamulira Mose.
Thus the children of Israel [God prevails] did. According to all that Adonai enjoined Moses [Drawn out], so they did.

< Numeri 1 >