< Numeri 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai, mu tenti ya msonkhano, pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, mʼchaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, kuti,
And Jehovah spoke to Moses in the wilderness of Sinai in the tent of meeting, on the first of the second month, in the second year after their departure from the land of Egypt, saying,
2 “Werengani Aisraeli onse mʼmafuko awo ndi mʼmabanja awo, lemba dzina la munthu wamwamuna aliyense, mmodzimmodzi.
Take the sum of the whole assembly of the children of Israel, after their families, according to their fathers' houses, by the number of the names, every male, according to their polls;
3 Iwe ndi Aaroni mwawerenge mwa magulu awo mu Israeli, amuna onse a zaka makumi awiri zakubadwa ndi opitirirapo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali.
from twenty years and upward, all that go forth to military service in Israel: ye shall number them according to their hosts, thou and Aaron.
4 Munthu mmodzi wochokera ku fuko lililonse yemwe ndi mtsogoleri wa banja lake, ndiye akuthandizeni pa ntchitoyi.
And with you there shall be a man for every tribe, a man who is the head of his father's house.
5 Mayina a anthu amene akuthandizeniwo ndi awa: Elizuri mwana wa Sedeuri, kuchokera ku fuko la Rubeni,
And these are the names of the men that shall stand with you: for Reuben, Elizur the son of Shedeur;
6 Selumieli mwana wa Zurisadai, kuchokera ku fuko la Simeoni,
for Simeon, Shelumiel the son of Zurishaddai;
7 Naasoni mwana wa Aminadabu, kuchokera ku fuko la Yuda,
for Judah, Nahshon the son of Amminadab;
8 Netanieli mwana wa Zuwara, kuchokera ku fuko la Isakara,
for Issachar, Nethaneel the son of Zuar;
9 Eliabu mwana wa Heloni, kuchokera ku fuko la Zebuloni,
for Zebulun, Eliab the son of Helon;
10 Mwa ana a Yosefe: kuchokera ku fuko la Efereimu, Elisama mwana wa Amihudi; kuchokera ku fuko la Manase, Gamalieli mwana wa Pedazuri;
for the children of Joseph: for Ephraim, Elishama the son of Ammihud; for Manasseh, Gamaliel the son of Pedahzur;
11 Abidani mwana wa Gideoni, kuchokera ku fuko la Benjamini,
for Benjamin, Abidan the son of Gideoni;
12 Ahiyezeri mwana wa Amisadai, kuchokera ku fuko la Dani,
for Dan, Ahiezer the son of Ammishaddai;
13 Pagieli mwana wa Okirani, kuchokera ku fuko la Aseri,
for Asher, Pagiel the son of Ocran;
14 Eliyasafu mwana wa Deuweli, kuchokera ku fuko la Gadi,
for Gad, Eliasaph the son of Deuel;
15 Ahira mwana wa Enani, kuchokera ku fuko la Nafutali.”
for Naphtali, Ahira the son of Enan.
16 Amenewa ndi anthu amene anasankhidwa kuchokera mʼmagulu mwawo, eni mbumba a mafuko a makolo awo. Iwowa anali atsogoleri a mafuko a Israeli.
These were those summoned of the assembly, princes of the tribes of their fathers, the heads of the thousands of Israel.
17 Mose ndi Aaroni anatenga anthu amene mayina awo anaperekedwa,
And Moses and Aaron took these men who are expressed by their names,
18 ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, anasonkhanitsa anthu onse pamodzi. Anthuwo anafotokoza za makolo awo mwa mafuko awo ndi mabanja awo. Ndipo mayina a amuna onse amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo analembedwa, mmodzimmodzi
and gathered the whole assembly together on the first of the second month. And they declared their pedigrees after their families, according to their fathers' houses, by the number of the names, from twenty years old and upward, according to their polls.
19 monga momwe Yehova analamulira Mose. Motero iyeyo anawawerenga mʼchipululu cha Sinai:
As Jehovah had commanded Moses, so he numbered them in the wilderness of Sinai.
20 Kuchokera mwa ana a Rubeni, mwana wamwamuna woyamba wa Israeli: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali, anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
And the sons of Reuben, Israel's eldest son, their generations, after their families, according to their fathers' houses, by the number of the names, according to their polls, every male from twenty years old and upward, all that went forth to military service:
21 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Rubeni chinali 46,500.
those that were numbered of them, of the tribe of Reuben, were forty-six thousand five hundred.
22 Kuchokera mwa zidzukulu za Simeoni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sons of Simeon: their generations, after their families, according to their fathers' houses, those that were numbered of them, by the number of the names, according to their polls, every male from twenty years old and upward, all that went forth to military service:
23 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Simeoni chinali 59,300.
those that were numbered of them, of the tribe of Simeon, were fifty-nine thousand three hundred.
24 Kuchokera mwa zidzukulu za Gadi: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sons of Gad: their generations, after their families, according to their fathers' houses, by the number of the names, from twenty years old and upward, all that went forth to military service:
25 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Gadi chinali 45, 650.
those that were numbered of them, of the tribe of Gad, were forty-five thousand six hundred and fifty.
26 Kuchokera mwa zidzukulu za Yuda: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sons of Judah: their generations, after their families, according to their fathers' houses, by the number of the names, from twenty years old and upward, all that went forth to military service:
27 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Yuda chinali 74, 600.
those that were numbered of them, of the tribe of Judah, were seventy-four thousand six hundred.
28 Kuchokera mwa zidzukulu za Isakara: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sons of Issachar: their generations, after their families, according to their fathers' houses, by the number of the names, from twenty years old and upward, all that went forth to military service:
29 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Isakara chinali 54,400.
those that were numbered of them, of the tribe of Issachar, were fifty-four thousand four hundred.
30 Kuchokera mwa zidzukulu za Zebuloni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sons of Zebulun: their generations, after their families, according to their fathers' houses, by the number of the names, from twenty years old and upward, all that went forth to military service:
31 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Zebuloni chinali 57,400.
those that were numbered of them, of the tribe of Zebulun, were fifty-seven thousand four hundred.
32 Kuchokera mwa ana aamuna a Yosefe: Kuchokera mwa zidzukulu za Efereimu: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sons of Joseph: of the children of Ephraim: their generations, after their families, according to their fathers' houses, by the number of the names, from twenty years old and upward, all that went forth to military service:
33 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Efereimu chinali 40,500.
those that were numbered of them, of the tribe of Ephraim, were forty thousand five hundred.
34 Kuchokera mwa zidzukulu za Manase: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the children of Manasseh: their generations, after their families, according to their fathers' houses, by the number of the names, from twenty years old and upward, all that went forth to military service:
35 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Manase chinali 32,200.
those that were numbered of them, of the tribe of Manasseh, were thirty-two thousand two hundred.
36 Kuchokera mwa zidzukulu za Benjamini: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sons of Benjamin: their generations, after their families, according to their fathers' houses, by the number of the names, from twenty years old and upward, all that went forth to military service:
37 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Benjamini chinali 35,400.
those that were numbered of them, of the tribe of Benjamin, were thirty-five thousand four hundred.
38 Kuchokera mwa zidzukulu za Dani: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sons of Dan: their generations, after their families, according to their fathers' houses, by the number of the names, from twenty years old and upward, all that went forth to military service:
39 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Dani chinali 62,700.
those that were numbered of them, of the tribe of Dan, were sixty-two thousand seven hundred.
40 Kuchokera mwa zidzukulu za Aseri: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sons of Asher: their generations, after their families, according to their fathers' houses, by the number of the names, from twenty years old and upward, all that went forth to military service:
41 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Aseri chinali 41,500.
those that were numbered of them, of the tribe of Asher, were forty-one thousand five hundred.
42 Kuchokera mwa zidzukulu za Nafutali: Aamuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sons of Naphtali: their generations, after their families, according to their fathers' houses, by the number of the names, from twenty years old and upward, all that went forth to military service:
43 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Nafutali chinali 53,400.
those that were numbered of them, of the tribe of Naphtali, were fifty-three thousand four hundred.
44 Amenewa ndiwo anthu amene Mose ndi Aaroni anawawerenga mothandizidwa ndi atsogoleri khumi ndi awiri a Israeli, aliyense kuyimira fuko lake.
These are those that were numbered, whom Moses and Aaron numbered, and the princes of Israel, the twelve men: each one was for the house of his fathers.
45 Aisraeli onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli anawawerenga monga mwa mabanja awo.
And all those that were numbered of the children of Israel, according to their fathers' houses, from twenty years old and upward, all that went forth to military service in Israel,
46 Chiwerengero cha anthu onse pamodzi chinali 603,550.
all they that were numbered were six hundred and three thousand five hundred and fifty.
47 Koma mabanja a fuko la Levi okha sanawawerenge pamodzi ndi ena.
But the Levites after the tribe of their fathers were not numbered among them.
48 Pakuti Yehova anawuza Mose kuti,
For Jehovah had spoken to Moses, saying,
49 “Usawerenge fuko la Levi kapena kuliphatikiza mʼkawundula wa Aisraeli.
Only thou shalt not number the tribe of Levi, neither take the sum of them among the children of Israel.
50 Koma uyike Aleviwo kuti aziyangʼanira tenti yanga yopatulika, zipangizo zake ndi zonse zili mʼmenemo. Azinyamula tentiyo pamodzi ndi zipangizo zake zonse; azisamalira ndi kumanga misasa mozungulira tentiyo.
But thou, appoint the Levites over the tabernacle of testimony, and over all the vessels thereof, and over all things that belong to it: they shall bear the tabernacle, and all its vessels; and they shall serve it, and round about the tabernacle shall they encamp;
51 Pamene akusamutsa tentiyo, Alevi ndiwo aziyitsitsa, akafuna kuyimanganso, Alevi ndiwo aziyimiritsa. Wina aliyense amene adzayandikire tentiyo adzaphedwa.
and when the tabernacle setteth forward, the Levites shall take it down; and when the tabernacle encampeth, the Levites shall set it up; and the stranger that cometh near shall be put to death.
52 Aisraeli azimanga matenti awo mʼmagulumagulu, munthu aliyense ku gulu lake pansi pa mbendera yake.
And the children of Israel shall encamp every man in his camp, and every man by his own standard, according to their hosts;
53 Alevi nawonso, azimanga matenti awo mozungulira tenti yopatulika kuti chilango chisagwere Aisraeli onse. Ndipo Alevi aziyangʼanira ndi kusamalira tenti yopatulikayo.”
but the Levites shall encamp round about the tabernacle of testimony, that there come not wrath upon the assembly of the children of Israel; and the Levites shall keep the charge of the tabernacle of testimony.
54 Choncho Aisraeli anachita monga Yehova analamulira Mose.
And the children of Israel did so; according to all that Jehovah had commanded Moses, so did they.

< Numeri 1 >