< Numeri 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai, mu tenti ya msonkhano, pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, mʼchaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, kuti,
Og Herren talede til Mose i Sinai Ørk i Forsamlingens Paulun paa den første Dag i den anden Maaned i det andet Aar, efter at de vare udgangne af Ægyptens Land, og sagde:
2 “Werengani Aisraeli onse mʼmafuko awo ndi mʼmabanja awo, lemba dzina la munthu wamwamuna aliyense, mmodzimmodzi.
Tager Hovedsum paa hele Israels Børns Menighed, efter deres Slægter, efter deres Fædrenehus, ved Navnes Tal, alt Mandkøn Hoved for Hoved af dem,
3 Iwe ndi Aaroni mwawerenge mwa magulu awo mu Israeli, amuna onse a zaka makumi awiri zakubadwa ndi opitirirapo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali.
fra tyve Aar gamle og derover, hver som kan uddrage i Krig udi Israel; I skulle tælle dem efter deres Hær, du og Aron.
4 Munthu mmodzi wochokera ku fuko lililonse yemwe ndi mtsogoleri wa banja lake, ndiye akuthandizeni pa ntchitoyi.
Og med eder skal være en Mand for hver Stamme, en Mand, som er Øverste for sit Fædrenehus.
5 Mayina a anthu amene akuthandizeniwo ndi awa: Elizuri mwana wa Sedeuri, kuchokera ku fuko la Rubeni,
Og disse ere Navnene paa Mændene, som skulle staa eder bi: For Ruben: Elizur, Sedeurs Søn;
6 Selumieli mwana wa Zurisadai, kuchokera ku fuko la Simeoni,
for Simeon: Selumiel, Zurisaddai Søn;
7 Naasoni mwana wa Aminadabu, kuchokera ku fuko la Yuda,
for Juda: Nahesson, Amminadabs Søn;
8 Netanieli mwana wa Zuwara, kuchokera ku fuko la Isakara,
for Isaskar: Nethaneel, Zuars Søn;
9 Eliabu mwana wa Heloni, kuchokera ku fuko la Zebuloni,
for Sebulon: Eliab, Helons Søn;
10 Mwa ana a Yosefe: kuchokera ku fuko la Efereimu, Elisama mwana wa Amihudi; kuchokera ku fuko la Manase, Gamalieli mwana wa Pedazuri;
for Josefs Børn, for Efraim: Elisama, Amihuds Søn; for Manasse: Gamliel, Pedazurs Søn;
11 Abidani mwana wa Gideoni, kuchokera ku fuko la Benjamini,
for Benjamin: Abidan, Gideoni Søn;
12 Ahiyezeri mwana wa Amisadai, kuchokera ku fuko la Dani,
for Dan: Ahieser, Ammisaddai Søn;
13 Pagieli mwana wa Okirani, kuchokera ku fuko la Aseri,
for Aser: Pagiel, Okrans Søn;
14 Eliyasafu mwana wa Deuweli, kuchokera ku fuko la Gadi,
for Gad: Eliasaf, Deuels Søn;
15 Ahira mwana wa Enani, kuchokera ku fuko la Nafutali.”
for Nafthali: Ahira, Enans Søn.
16 Amenewa ndi anthu amene anasankhidwa kuchokera mʼmagulu mwawo, eni mbumba a mafuko a makolo awo. Iwowa anali atsogoleri a mafuko a Israeli.
Disse vare de kaldte af Menigheden, Fyrster for deres Fædres Stammer; de vare Øverster for Israels Tusinder.
17 Mose ndi Aaroni anatenga anthu amene mayina awo anaperekedwa,
Og Mose og Aron toge disse Mænd, som ere udtrykkelig nævnede ved Navne.
18 ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, anasonkhanitsa anthu onse pamodzi. Anthuwo anafotokoza za makolo awo mwa mafuko awo ndi mabanja awo. Ndipo mayina a amuna onse amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo analembedwa, mmodzimmodzi
Og de lode hele Menigheden samle sig paa den første Dag i den anden Maaned, og de opgave deres Herkomst, efter deres Slægter, efter deres Fædrenehus, efter Navnes Tal, fra tyve Aar gamle og derover, Hoved for Hoved.
19 monga momwe Yehova analamulira Mose. Motero iyeyo anawawerenga mʼchipululu cha Sinai:
Som Herren havde befalet Mose, saa talte han dem i Sinai Ørk.
20 Kuchokera mwa ana a Rubeni, mwana wamwamuna woyamba wa Israeli: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali, anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Og Rubens, Israels førstefødtes, Børns Afkom efter deres Slægter, efter deres Fædrenehus, efter Navnes Tal, Hoved for Hoved, alt Mandkøn fra tyve Aar gamle og derover, hver som kunde uddrage i Strid:
21 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Rubeni chinali 46,500.
De talte af dem til Rubens Stamme vare seks og fyrretyve Tusinde og fem Hundrede.
22 Kuchokera mwa zidzukulu za Simeoni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Simeons Børns Afkom, efter deres Slægter, efter deres Fædrenehus; de talte af dem efter Navnes Tal, Hoved for Hoved, alt Mandkøn fra tyve Aar gamle og derover, hver som kunde uddrage i Strid:
23 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Simeoni chinali 59,300.
De talte af dem til Simeons Stamme vare ni og halvtredsindstyve Tusinde og tre Hundrede.
24 Kuchokera mwa zidzukulu za Gadi: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Gads Børns Afkom, efter deres Slægter, efter deres Fædrenehus, efter Navnes Tal, fra tyve Aar gamle og derover, hver som kunde uddrage i Strid:
25 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Gadi chinali 45, 650.
De talte af dem til Gads Stamme vare fem og fyrretyve Tusinde og seks Hundrede og halvtredsindstyve.
26 Kuchokera mwa zidzukulu za Yuda: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Judas Børns Afkom, efter deres Slægter, efter deres Fædrenehus, efter Navnes Tal, fra tyve Aar og derover, hver som kunde uddrage i Strid:
27 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Yuda chinali 74, 600.
De talte af dem til Judas Stamme vare fire og halvfjerdsindstyve Tusinde og seks Hundrede.
28 Kuchokera mwa zidzukulu za Isakara: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Isaskars Børns Afkom, efter deres Slægter, efter deres Fædrenehus, efter Navnes Tal, fra tyve Aar gamle og derover, hver som kunde uddrage i Strid:
29 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Isakara chinali 54,400.
De talte af dem til Isaskars Stamme vare fire og halvtredsindstyve Tusinde og fire Hundrede.
30 Kuchokera mwa zidzukulu za Zebuloni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Sebulons Børns Afkom, efter deres Slægter, efter deres Fædrenehus, efter Navnes Tal, fra tyve Aar gamle og derover, hver som kunde uddrage i Strid:
31 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Zebuloni chinali 57,400.
De talte af dem til Sebulons Stamme vare syv og halvtredsindstyve Tusinde og fire Hundrede.
32 Kuchokera mwa ana aamuna a Yosefe: Kuchokera mwa zidzukulu za Efereimu: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Josefs Børn, nemlig Efraims Børns Afkom, efter deres Slægter, efter deres Fædrenehus, efter Navnes Tal, fra tyve Aar gamle og derover, hver som kunde uddrage i Strid:
33 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Efereimu chinali 40,500.
De talte af dem til Efraims Stamme vare fyrretyve Tusinde og fem Hundrede.
34 Kuchokera mwa zidzukulu za Manase: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Manasse Børns Afkom, efter deres Slægter, efter deres Fædrenehus, efter Navnes Tal, fra tyve Aar gamle og derover, hver som kunde uddrage i Strid:
35 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Manase chinali 32,200.
De talte af dem til Manasse Stamme vare to og tredive Tusinde og to Hundrede.
36 Kuchokera mwa zidzukulu za Benjamini: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Benjamins Børns Afkom, efter deres Slægter, efter deres Fædrenehus, efter Navnes Tal, fra tyve Aar gamle og derover, hver som kunde uddrage i Strid:
37 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Benjamini chinali 35,400.
De talte af dem til Benjamins Stamme vare fem og tredive Tusinde og fire Hundrede.
38 Kuchokera mwa zidzukulu za Dani: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Dans Børns Afkom, efter deres Slægter, efter deres Fædrenehus, efter Navnes Tal, fra tyve Aar gamle og derover, hver som kunde uddrage i Strid:
39 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Dani chinali 62,700.
De talte af dem til Dans Stamme vare to og tresindstyve Tusinde og syv Hundrede.
40 Kuchokera mwa zidzukulu za Aseri: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Asers Børns Afkom, efter deres Slægter, efter deres Fædrenehus, efter Navnes Tal, fra tyve Aar gamle og derover, hver som kunde uddrage i Strid:
41 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Aseri chinali 41,500.
De talte af dem til Asers Stamme vare eet og fyrretyve Tusinde og fem Hundrede.
42 Kuchokera mwa zidzukulu za Nafutali: Aamuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Nafthali Børns Afkom, efter deres Slægter, efter deres Fædrenehus, efter Navnes Tal, fra tyve Aar gamle og derover, hver som kunde uddrage i Strid:
43 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Nafutali chinali 53,400.
De talte af dem til Nafthali Stamme vare tre og halvtredsindstyve Tusinde og fire Hundrede.
44 Amenewa ndiwo anthu amene Mose ndi Aaroni anawawerenga mothandizidwa ndi atsogoleri khumi ndi awiri a Israeli, aliyense kuyimira fuko lake.
Disse ere de talte, som Mose og Aron talte, og hver af de tolv Israels Fyrster; hver Mand var for sit Fædrenehus.
45 Aisraeli onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli anawawerenga monga mwa mabanja awo.
Og alle de, som bleve talte af Israels Børn, efter deres Fædrenehus, fra tyve Aar gamle og derover, hver som kunde uddrage i Strid i Israel,
46 Chiwerengero cha anthu onse pamodzi chinali 603,550.
ja, alle de talte vare seks Hundrede Tusinde og tre Tusinde og fem Hundrede og halvtredsindstyve.
47 Koma mabanja a fuko la Levi okha sanawawerenge pamodzi ndi ena.
Men Leviterne efter deres Fædres Stamme, de bleve ikke talte iblandt dem.
48 Pakuti Yehova anawuza Mose kuti,
Thi Herren talede til Mose og sagde:
49 “Usawerenge fuko la Levi kapena kuliphatikiza mʼkawundula wa Aisraeli.
Dog skal du ikke tælle Levi Stamme og ej tage Hovedsum paa dem, midt iblandt Israels Børn;
50 Koma uyike Aleviwo kuti aziyangʼanira tenti yanga yopatulika, zipangizo zake ndi zonse zili mʼmenemo. Azinyamula tentiyo pamodzi ndi zipangizo zake zonse; azisamalira ndi kumanga misasa mozungulira tentiyo.
men du skal beskikke Leviterne over Vidnesbyrdets Tabernakel og over alt Redskabet dertil og over alt det, som dertil hører, de skulle bære Tabernaklet og alt Redskabet dertil, og de skulle tjene ved det; og de skulle lejre sig trindt omkring Tabernaklet.
51 Pamene akusamutsa tentiyo, Alevi ndiwo aziyitsitsa, akafuna kuyimanganso, Alevi ndiwo aziyimiritsa. Wina aliyense amene adzayandikire tentiyo adzaphedwa.
Og naar Tabernaklet skal rejse, skulle Leviterne tage det ned; men naar Tabernaklet skal lejre sig, skulle Leviterne rejse det op; og kommer nogen fremmed nær derved, skal han dødes.
52 Aisraeli azimanga matenti awo mʼmagulumagulu, munthu aliyense ku gulu lake pansi pa mbendera yake.
Og Israels Børn skulle lejre sig, hver i sin Lejr og hver hos sit Banner efter deres Hære.
53 Alevi nawonso, azimanga matenti awo mozungulira tenti yopatulika kuti chilango chisagwere Aisraeli onse. Ndipo Alevi aziyangʼanira ndi kusamalira tenti yopatulikayo.”
Men Leviterne skulle lejre sig omkring Vidnesbyrdets Tabernakel, at ikke en Vrede skal være over Israels Børns Menighed; derfor skulle Leviterne tage Vare paa, hvad der er at varetage ved Vidnesbyrdets Tabernakel.
54 Choncho Aisraeli anachita monga Yehova analamulira Mose.
Og Israels Børn gjorde det; efter alt det, som Herren havde befalet Mose, saa gjorde de.

< Numeri 1 >