< Numeri 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai, mu tenti ya msonkhano, pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, mʼchaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, kuti,
Mluvil pak Hospodin k Mojžíšovi na poušti Sinai, v stánku úmluvy, prvního dne měsíce druhého, léta druhého po vyjití jejich z země Egyptské, řka:
2 “Werengani Aisraeli onse mʼmafuko awo ndi mʼmabanja awo, lemba dzina la munthu wamwamuna aliyense, mmodzimmodzi.
Sečtěte summu všeho množství synů Izraelských po čeledech jejich, a po domích otců jejich, vedlé počtu jmen každého pohlaví mužského po hlavách jejich,
3 Iwe ndi Aaroni mwawerenge mwa magulu awo mu Israeli, amuna onse a zaka makumi awiri zakubadwa ndi opitirirapo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali.
Od dvadcítiletých a výše všecky, kteříž by mohli jíti k boji v Izraeli, sečtěte je po houfích jejich, ty a Aron.
4 Munthu mmodzi wochokera ku fuko lililonse yemwe ndi mtsogoleri wa banja lake, ndiye akuthandizeni pa ntchitoyi.
A bude s vámi z každého pokolení jeden muž, kterýž by přední byl v domě otců svých.
5 Mayina a anthu amene akuthandizeniwo ndi awa: Elizuri mwana wa Sedeuri, kuchokera ku fuko la Rubeni,
Tato pak jsou jména mužů, kteříž stanou s vámi: Z pokolení Rubenova Elisur, syn Sedeurův;
6 Selumieli mwana wa Zurisadai, kuchokera ku fuko la Simeoni,
Z Simeonova Salamiel, syn Surisaddai;
7 Naasoni mwana wa Aminadabu, kuchokera ku fuko la Yuda,
Z Judova Názon, syn Aminadabův;
8 Netanieli mwana wa Zuwara, kuchokera ku fuko la Isakara,
Z Izacharova Natanael, syn Suar;
9 Eliabu mwana wa Heloni, kuchokera ku fuko la Zebuloni,
Z Zabulonova Eliab, syn Helonův;
10 Mwa ana a Yosefe: kuchokera ku fuko la Efereimu, Elisama mwana wa Amihudi; kuchokera ku fuko la Manase, Gamalieli mwana wa Pedazuri;
Z synů Jozefových, z pokolení Efraimova Elisama, syn Amiudův; z Manassesova Gamaliel, syn Fadasurův;
11 Abidani mwana wa Gideoni, kuchokera ku fuko la Benjamini,
Z Beniaminova Abidan, syn Gedeonův;
12 Ahiyezeri mwana wa Amisadai, kuchokera ku fuko la Dani,
Z pokolení Dan Ahiezer, syn Amisaddai;
13 Pagieli mwana wa Okirani, kuchokera ku fuko la Aseri,
Z Asser Fegiel, syn Ochranův;
14 Eliyasafu mwana wa Deuweli, kuchokera ku fuko la Gadi,
Z pokolení Gád Eliazaf, syn Duelův;
15 Ahira mwana wa Enani, kuchokera ku fuko la Nafutali.”
Z Neftalímova Ahira, syn Enanův.
16 Amenewa ndi anthu amene anasankhidwa kuchokera mʼmagulu mwawo, eni mbumba a mafuko a makolo awo. Iwowa anali atsogoleri a mafuko a Israeli.
Ti jsou slovoutní z lidu, knížata pokolení otců svých, ti jako hlavy tisíců Izraelských budou.
17 Mose ndi Aaroni anatenga anthu amene mayina awo anaperekedwa,
Vzal tedy Mojžíš a Aron muže ty, kteříž jmenováni byli,
18 ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, anasonkhanitsa anthu onse pamodzi. Anthuwo anafotokoza za makolo awo mwa mafuko awo ndi mabanja awo. Ndipo mayina a amuna onse amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo analembedwa, mmodzimmodzi
A shromáždili všecko množství prvního dne měsíce druhého, kteříž přiznávali se k rodům svým po čeledech svých, po domích otců svých, a vedlé počtu jmen, od dvadcítiletých a výše po osobách svých.
19 monga momwe Yehova analamulira Mose. Motero iyeyo anawawerenga mʼchipululu cha Sinai:
Jakož byl přikázal Hospodin Mojžíšovi, tak sčetl je na poušti Sinai.
20 Kuchokera mwa ana a Rubeni, mwana wamwamuna woyamba wa Israeli: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali, anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
I bylo synů Rubena prvorozeného Izraelova, rodiny jejich, po čeledech jejich, po domích otců jejich, a podlé počtu jmen, po hlavách jejich, všech pohlaví mužského, od dvadcítiletých a výše, všech, kteříž mohli jíti k boji,
21 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Rubeni chinali 46,500.
A načteno jich z pokolení Rubenova čtyřidceti šest tisíců a pět set.
22 Kuchokera mwa zidzukulu za Simeoni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Z synů Simeonových, rodiny jejich, po čeledech jejich, po domích otců jejich, sečtených jeho vedlé počtu jmen, po hlavách jejich, všech pohlaví mužského od dvadcítiletých a výše, všech, kteříž mohli jíti k boji,
23 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Simeoni chinali 59,300.
Načteno jich z pokolení Simeonova padesáte devět tisíců a tři sta.
24 Kuchokera mwa zidzukulu za Gadi: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Z synů Gádových, rodiny jejich, po čeledech jejich, po domích otců jejich, podlé počtu jmen, od dvadcítiletých a výše, všech, kteříž mohli bojovati,
25 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Gadi chinali 45, 650.
Načteno jich z pokolení Gádova čtyřidceti pět tisíců, šest set a padesát.
26 Kuchokera mwa zidzukulu za Yuda: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Z synů Judových, rodiny jejich, po čeledech jejich, po domích otců jejich, vedlé počtu jmen, od dvadcíti let a výše, všech, kteříž mohli jíti k boji,
27 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Yuda chinali 74, 600.
Načteno jich z pokolení Judova sedmdesáte čtyři tisíce a šest set.
28 Kuchokera mwa zidzukulu za Isakara: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Z synů Izacharových, rodiny jejich, po čeledech jejich, po domích otců jejich, podlé počtu jmen, od dvadcítiletých a výše, všech, kteříž mohli jíti k boji,
29 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Isakara chinali 54,400.
Načteno jich z pokolení Izacharova padesáte čtyři tisíce a čtyři sta.
30 Kuchokera mwa zidzukulu za Zebuloni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Z synů Zabulonových, rodiny jejich, po čeledech jejich, po domích otců jejich, podlé počtu jmen, od dvadcítiletých a výše, všech, kteříž mohli jíti k boji,
31 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Zebuloni chinali 57,400.
Načteno jich z pokolení Zabulonova padesáte sedm tisíců a čtyři sta.
32 Kuchokera mwa ana aamuna a Yosefe: Kuchokera mwa zidzukulu za Efereimu: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Z synů Jozefových, a nejprv, synů Efraimových, rodiny jejich, po čeledech jejich, po domích otců jejich, podlé počtu jmen, od dvadcítiletých a výše, všech, kteříž mohli jíti k boji,
33 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Efereimu chinali 40,500.
Načteno jich z pokolení Efraimova čtyřidceti tisíc a pět set.
34 Kuchokera mwa zidzukulu za Manase: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Potom z synů Manassesových, rodiny jejich, po čeledech jejich, po domích otců jejich, vedlé počtu jmen, od dvadcítiletých a výše, všech, kteříž vycházeli k boji,
35 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Manase chinali 32,200.
Načteno jich z pokolení Manassesova třidceti dva tisíce a dvě stě.
36 Kuchokera mwa zidzukulu za Benjamini: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Z synů Beniaminových, rodiny jejich, po čeledech jejich, po domích otců jejich, vedlé počtu jmen, od dvadcítiletých a výše, všech, kteříž mohli jíti do boje,
37 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Benjamini chinali 35,400.
Načteno jich z pokolení Beniaminova třidceti pět tisíců a čtyři sta.
38 Kuchokera mwa zidzukulu za Dani: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Z synů Dan, rodiny jejich, po čeledech jejich, po domích otců jejich, vedlé počtu jmen, od dvadcítiletých a výše, všech, kteříž vycházeli k boji,
39 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Dani chinali 62,700.
Načteno jich z pokolení Dan šedesáte dva tisíce a sedm set.
40 Kuchokera mwa zidzukulu za Aseri: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Z synů Asser, rodiny jejich, po čeledech jejich, po domích otců jejich, vedlé počtu jmen, od dvadcítiletých a výše, všech, kteříž mohli jíti na vojnu,
41 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Aseri chinali 41,500.
Načteno jich z pokolení Asser čtyřidceti jeden tisíců a pět set.
42 Kuchokera mwa zidzukulu za Nafutali: Aamuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Z synů Neftalímových, rodiny jejich, po čeledech jejich, po domích otců jejich, vedlé počtu jmen, od dvadcítiletých a výše, všech, kteříž mohli jíti k boji,
43 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Nafutali chinali 53,400.
Načteno jich z pokolení Neftalímova padesáte tři tisíce a čtyři sta.
44 Amenewa ndiwo anthu amene Mose ndi Aaroni anawawerenga mothandizidwa ndi atsogoleri khumi ndi awiri a Israeli, aliyense kuyimira fuko lake.
Ten jest počet těch, kteréž sečtl Mojžíš a Aron a knížata Izraelská, dvanácte mužů, kteříž byli vybráni po jednom z domů otců svých.
45 Aisraeli onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli anawawerenga monga mwa mabanja awo.
I bylo všech sečtených synů Izraelských po domích otců jejich, od dvadcítiletých a výše, všech, kteříž mohli vycházeti k boji v Izraeli,
46 Chiwerengero cha anthu onse pamodzi chinali 603,550.
Všech sečtených bylo šestkrát sto tisíc, a tři tisíce, pět set a padesáte.
47 Koma mabanja a fuko la Levi okha sanawawerenge pamodzi ndi ena.
Levítové pak vedlé pokolení otců svých nejsou počítáni mezi ně.
48 Pakuti Yehova anawuza Mose kuti,
Nebo byl mluvil Hospodin k Mojžíšovi, řka:
49 “Usawerenge fuko la Levi kapena kuliphatikiza mʼkawundula wa Aisraeli.
Pokolení Levítského nebudeš počítati, a nepřičteš jich k synům Izraelským,
50 Koma uyike Aleviwo kuti aziyangʼanira tenti yanga yopatulika, zipangizo zake ndi zonse zili mʼmenemo. Azinyamula tentiyo pamodzi ndi zipangizo zake zonse; azisamalira ndi kumanga misasa mozungulira tentiyo.
Ale ustanovíš Levíty nad příbytkem svědectví, a nade vším nádobím jeho, a nade všemi věcmi, kteréž přináležejí k němu. Oni nositi budou příbytek i všecka nádobí jeho, oni přisluhovati budou jemu, a vůkol příbytku klásti se budou.
51 Pamene akusamutsa tentiyo, Alevi ndiwo aziyitsitsa, akafuna kuyimanganso, Alevi ndiwo aziyimiritsa. Wina aliyense amene adzayandikire tentiyo adzaphedwa.
Když se pak s místa bude míti hýbati příbytek, složí jej Levítové; a když se bude klásti příbytek, vyzdvihnou jej Levítové. Kdož by koli cizí přistoupil, umře.
52 Aisraeli azimanga matenti awo mʼmagulumagulu, munthu aliyense ku gulu lake pansi pa mbendera yake.
I budouť se klásti synové Izraelští, jeden každý v ležení svém, a jeden každý pod praporcem svým, a po houfích svých.
53 Alevi nawonso, azimanga matenti awo mozungulira tenti yopatulika kuti chilango chisagwere Aisraeli onse. Ndipo Alevi aziyangʼanira ndi kusamalira tenti yopatulikayo.”
Levítové pak klásti se budou vůkol příbytku svědectví, aby nepřišlo rozhněvání mé na shromáždění synů Izraelských; i budou Levítové držeti stráž u příbytku svědectví.
54 Choncho Aisraeli anachita monga Yehova analamulira Mose.
Učinili tedy to synové Izraelští; všecko, jakž přikázal Hospodin Mojžíšovi, tak učinili.

< Numeri 1 >