< Numeri 9 >
1 Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai pa mwezi woyamba wa chaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, nati,
Le Seigneur parla à Moïse dans le désert de Sinaï, à la seconde année après qu’ils furent sortis de la terre d’Egypte, au premier mois, disant:
2 “Aisraeli azichita Paska pa nthawi yake yoyikika.
Que les enfants d’Israël fassent la Pâque en son temps,
3 Muzichita Paska pa nthawi yake yoyikika, madzulo a tsiku la 14 la mwezi uno, potsata malamulo ndi malangizo ake.”
Au quatorzième jour de ce mois, vers le soir, selon toutes ses cérémonies et ses ordonnances.
4 Choncho Mose anawuza Aisraeli kuti azichita Paska,
Et Moïse ordonna aux enfants d’Israël qu’ils feraient la Pâque.
5 ndipo anachitadi Paskayo mʼchipululu cha Sinai madzulo a tsiku la 14 la mwezi woyamba. Aisraeli anachita zonse monga momwe Yehova analamulira Mose.
Ils la firent en son temps, au quatorzième jour du mois, sur la montagne de Sinaï. Les enfants d’Israël firent selon tout ce qu’avait commandé le Seigneur à Moïse.
6 Koma ena a iwo sanathe kuchita nawo Paska pa tsiku limenelo chifukwa anali odetsedwa chifukwa chokhudza mtembo. Choncho anabwera kwa Mose ndi Aaroni tsiku lomwelo,
Or voici que quelques-uns, impurs à cause de l’âme d’un homme, et qui ne pouvaient faire la Pâque en ce jour-là, s’approchant de Moïse et d’Aaron,
7 ndipo anawuza Moseyo kuti, “Ife tadetsedwa chifukwa cha mtembo wa munthu. Nʼchifukwa chiyani taletsedwa kupereka nsembe kwa Yehova pamodzi ndi Aisraeli ena pa nthawi yake?”
Leur dirent: Nous sommes impurs à cause de l’âme d’un homme: pourquoi sommes-nous frustrés de pouvoir offrir l’offrande au Seigneur en son temps parmi les enfants d’Israël?
8 Mose anawayankha kuti, “Dikirani mpaka nditamva zimene Yehova walamula zokhudza Inu.”
Moïse leur répondit: Attendez que je consulte le Seigneur sur ce qu’il ordonnera de vous.
9 Ndipo Yehova anawuza Mose kuti,
Et le Seigneur parla à Moïse, disant:
10 “Uza Aisraeli kuti, ‘Pamene wina mwa inu kapena zidzukulu zanu adetsedwa chifukwa chokhudza mtembo wa munthu, kapena akakhala pa ulendo, akhoza kuchita nawo Paska ya Yehova.
Dis aux enfants d’Israël: Qu’un homme dans votre nation qui sera impur à cause d’une âme, ou en voyage au loin, fasse la Pâque du Seigneur
11 Azichita chikondwererochi madzulo a pa tsiku la 14 la mwezi wachiwiri. Azidya mwana wankhosa wamwamuna pamodzi ndi buledi wopanda yisiti ndi ndiwo zowawa zamasamba.
Au second mois, au quatorzième jour du mois, vers le soir; c’est avec des azymes et des laitues sauvages qu’il la mangera;
12 Iwo asasiye nyama ina iliyonse mpaka mmawa. Asaswe mafupa aliwonse. Pamene akuchita chikondwerero cha Paska, atsate malangizo onse.
Il n’en laissera rien jusque au matin et il n’en rompra point les os: il observera tout le rite de la Pâque.
13 Koma ngati munthu wina ali woyeretsedwa ndipo sali pa ulendo koma alephera kuchita Paska, munthu ameneyo achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake chifukwa sanabweretse chopereka cha Yehova pa nthawi yake. Munthu ameneyo adzalangidwa chifukwa cha tchimo lake.
Mais si quelqu’un est même pur, et n’est point en voyage, et que cependant il ne fasse point la Pâque, cette âme sera exterminée du milieu de ses peuples; parce qu’il n’a pas offert de sacrifice au Seigneur en son temps: il portera lui-même son péché.
14 “‘Mlendo amene akukhala pakati panu, nafuna kuchita nawo Paska ya Yehova, achite nawo motsata malamulo ndi malangizo ake. Muzikhala ndi malangizo ofanana a Paska; mbadwa kapena mlendo.’”
Un voyageur aussi et un étranger, s’ils se trouvent chez vous, feront la Pâque du Seigneur selon ses cérémonies et ses ordonnances. Ce sera un précepte parmi vous, tant pour l’étranger que pour l’indigène.
15 Pa tsiku limene anayimika chihema, tenti ya umboni, mtambo unaphimba chihemacho. Kuyambira madzulo mpaka mmawa, mtambo umene unali pamwamba pa chihemacho unkaoneka ngati moto.
Donc au jour que fut dressé le tabernacle, la nuée le couvrit. Mais depuis le soir, il y eut sur la tente comme une espèce de feu jusqu’au matin.
16 Zinkachitika motere mosalekeza: mtambo unkakhala pamwamba pa chihema, ndipo usiku unkaoneka ngati moto.
Ainsi arrivait-il toujours: pendant le jour la nuée couvrait le tabernacle, et pendant la nuit, comme une espèce de feu.
17 Nthawi ina iliyonse mtambo ukachoka pamwamba pa chihema, Aisraeli ankasamukanso, ndipo paliponse pamene mtambo wayima, Aisraeli ankamangapo misasa.
Et lorsque la nuée qui couvrait le tabernacle était enlevée, les enfants d’Israël partaient; et dans le lieu où elle s’arrêtait, là ils campaient.
18 Aisraeli ankasamuka pamalopo Yehova akawalamula, ndipo ankamanganso misasa Iyeyo akawalamula. Nthawi yonse imene mtambowo wayima pa chihema, ankakhalabe mʼmisasa yawo.
Au commandement du Seigneur ils partaient, et à son commandement ils dressaient le tabernacle. Pendant tous les jours que la nuée se tenait sur le tabernacle, ils demeuraient dans le même lieu.
19 Mtambowo ukakhala pa chihema nthawi yayitali, Aisraeli ankasungabe lamulo la Yehova ndipo iwo sankasamukanso.
Et s’il arrivait qu’elle demeurât longtemps sur lui, les enfants d’Israël étaient en observation du Seigneur, et partaient pas,
20 Nthawi zina mtambowo unkakhala pa chihemapo masiku owerengeka. Aisraeli ankamanga misasa molamulidwa ndi Yehova ndipo ankasamukanso molamulidwa ndi Iyeyo.
Autant de jours que la nuée était sur le tabernacle. Au commandement du Seigneur, ils dressaient les tentes, et à son commandement, ils les enlevaient.
21 Nthawi zina mtambo unkakhala kuyambira madzulo mpaka mmawa ndipo unkachoka mmawa mwake, ankasamuka. Kaya ndi masana kapena usiku, pamene mtambo wachoka, ankasamuka.
Si la nuée restait depuis le soir jusqu’au matin, et qu’aussitôt le point du jour elle quittât le tabernacle, ils partaient: et si après un jour et une nuit elle se retirait, ils détendaient les tentes.
22 Ngakhale mtambo ukhale pa chihema masiku awiri kapena mwezi kapena chaka, Aisraeli ankakhalabe pa msasa osachoka. Koma ukachoka, ankasamuka.
Mais si elle était deux jours, ou un mois ou plus longtemps sur le tabernacle, les enfants d’Israël demeuraient dans le même lieu et ne partaient pas; mais dès qu’elle s’était retirée, ils levaient le camp.
23 Molamulidwa ndi Yehova ankamanga misasa yawo ndipo ankasamukanso Yehova akawalamula. Ankamvera lamulo la Yehova kudzera mwa Mose.
C’était sur la parole du Seigneur qu’ils plantaient les tentes, et sur sa parole qu’ils partaient: et ils étaient en observation du Seigneur, selon son commandement par l’entremise de Moïse.